Top Banner
1 NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSA HARVESTIME INTERNATIONAL INSTITUTE Phunziro limeneri ndi gawo limodzi la maphunziro a Harvest International Institute ndipo cholinga chake ndi kukonzekeretsa okhulupilira kuti akatute zokolora zambiri zauzimu. Mutu waukulu mumaphunzirowa ndikuphunzitsa zimene Yesu anaphunzitsa, zimene zinasandulitsa anthu wamba monga asodzi, otolera misonkho ndi ena kulalikira Uthenga Wabwino ndi kuwonetsera mphamvu ya uthengawo mu nthawi yawo. Bukuli ndi phunziro limodzi mwa maphunziro ambiri amene cholinga chake ndikuwakopa okhulupilira kuti akakonze dongosolo, kuyendetsa, ndi kubweretsa pamodzi anthu kuti Uthenga Wabwino ukalalikidwe. @Harvestime International Institute
168

NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

Jan 19, 2020

Download

Documents

dariahiddleston
Welcome message from author
This document is posted to help you gain knowledge. Please leave a comment to let me know what you think about it! Share it to your friends and learn new things together.
Transcript
Page 1: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

1

NDONDOMEKO ZA NJIRA

ZA

KUCHULUKITSA

HARVESTIME INTERNATIONAL INSTITUTE

Phunziro limeneri ndi gawo limodzi la maphunziro a Harvest International Institute ndipo

cholinga chake ndi kukonzekeretsa okhulupilira kuti akatute zokolora zambiri zauzimu.

Mutu waukulu mumaphunzirowa ndikuphunzitsa zimene Yesu anaphunzitsa, zimene

zinasandulitsa anthu wamba monga asodzi, otolera misonkho ndi ena kulalikira Uthenga

Wabwino ndi kuwonetsera mphamvu ya uthengawo mu nthawi yawo.

Bukuli ndi phunziro limodzi mwa maphunziro ambiri amene cholinga chake ndikuwakopa

okhulupilira kuti akakonze dongosolo, kuyendetsa, ndi kubweretsa pamodzi anthu kuti Uthenga

Wabwino ukalalikidwe.

@Harvestime International Institute

Page 2: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

2

ZAMKATI MWA BUKULI

Kagwiritsidwe Ntchito Ka Bukuli……………………………………………………….…..........3

Ndondomeko Zothandizira Kuphunzira Limodzi Pagulu…………………………………………4

Mau Oyamba……………………………………………………………………………………....5

Zolinga za Maphunzirowa…………………………………………………………………...........7

NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSA

1. Asodzi a Anthu……………………………………………………………………………......8

2. Tsiku la Zinthu Zochepa………………………………………………………………..........16

3. Mafanizo a Kuchuliktsa……………………………………………………………………...40

4. Chimodzi Kuphatikiza Chimodzi Zimakhala Zopitilira Ziwiri…………………………...…50

5. Mawu Oyamba a Kukula kwa Mpingo………………………………………………………58

6. Kukula kwa Mkati……………………………………………………………………………70

7. Kukula mu Chiwerengero…………………………………………………………………....90

8. Kukula Mmadera…………………………………………………………………………...104

9. Kukula Polumikiza…………………………………………………………………………112

10. Zisankho Kapena Ophunzira……………………………………………………………….127

11. Kukula Mopinimbira……………………………………………………………………….143

12. Malo Ochitirapo Maphunziro………………………………………………………………154

13. Mayankho a Mafunso Odziyetsa Nokha……………………………………………………163

Page 3: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

3

KAGWIRITSIDWE NTCHITO KA BUKULI

KAKONZEDWE KA BUKULI

Phunziro liri lonse limakhala ndi zinthu izi:

Zolinga: Izi ndi zimene mukuyenera kukwaniritsa kapena kudziwa pa mapeto pa phunziro.

Welengani zimenezi musanayambe phunziro lanu.

Vesi Yotsogololera: Ndimeyi imatsindika mfundo yayikulu mu phunziro lathu.

Zopezeka mu Magawo: Gwiritsani ntchito Baibulo lanu kuti mufufuze mavesi amene

sanalembedwe mu bukuli koma angotchulidwa.

Mayeso Odziyesa Nokha: Osathamangira kulememba mayeso musanamalize kuwerenga

chaputala, komanso polemba musagwiritse ntchito Baibulo kapena bukuli polemba mayesowa.

Mayankho amayesowa muwapeza kumapeto a bukuli.

Zophunzira Zowonjezera: Ndime imeneyi ikuthandizani kuti muwerenge mau Mulungu ndi

kuzamitsa ukadaulo wanu pophunziro komanso kugwiritsa ntchito mu utumiki zimene mwa.

Mayeso Omaliza: ngati mwayamba kuphunzira phunziroli mukuyenera kulemba mayeso

pamapeto a phunziroli ndipo mayesowo aperekedwa kwa aphunzitsi anu kuti mupatsidwe

malikisi.

ZOWELENGA ZINA ZOFUNIKA POPHUNZIRA PHUNZIROLI

Mudzafunikira Buku Lopatulika

Page 4: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

4

NDONDOMEKO ZOTHANDIZIRA KUPHUNZIRA LIMODZI PAGULU

MKUMANO WOYAMBA

Kutsekulira: Yamabani ndi pemphero ndi kudziwana wina ndi mnzake ndipo ophunzira

alembetse mayina.

Khazikitsani Ndondomeko Zapagulu: Musankhe amene atsogolere mkumano wanu,

sankhaninso malo ndi masiku amene mudzikumana.

Mayamiko ndi Matamando: Yitanirani kupezeka kwa Mzimu Woyera pamene muchita

mkumano wanu.

Gawani Mabuku Kwa Ophunzira: Awuzeni ophunzira dzina laphunziro, zolinga zake ndi

dongosolo.

Perekani Nchito Yoyamba. Ophunzira ayenera kuwerenga ma chaputala amene apatsidwa

ndikulemba mayeso odziyesa okha isanafike nthawi ya mkumano wina. Ndipo kuchuluka kwa

machaputala amene adziphunzitsidwa pa mkumano uli onse kuzitengera kutalika kwa chaputala

komanso kumvetsetsa kwa ophunzira.

MKUMANO WACHIWIRI NDI KUKUMANA KWINA PATSOGOLO

Kutsekulira: Tsekulirani ndi pemphero kenako lembani mayina awophunzira atsopano

ndikuwapatsa buku lawo. Muyitane mayina a wophunzira amene abwera. Komanso osayiwala

mayamiko ndi matamando kwa Mulungu.

Kukumbutsira: Yambani ndi kubwereza mwachidule zimene munaphunzitsa mu mkumano

wanu womaliza.

Phunziro: Afunseni ophunzira ndemanga zawo kapena mafunso okhudza phunziro limene

aphunzira komanso mmene angagwiritsire ntchito zimene aphunzira pamoyo wawo ndi utumiki.

Mayeso Odziyesa Nokha: Konzetsani mayeso amene ophunzira amaliza ndipo mukhonza

kusankha kupereka mayankha kapena kuwachotsa mubukuli kuti ophunzira adzipezere okha

mayankho.

Mayeso omaliza: Pamapeto pa maphunziro amenewa, gulu la ophunzira onse lidzapemphedwa

kulemba mayeso omaliza ndipo aphunzitsi awonetsetse kuti ophunzira wina aliyense ali ndi buku

laphunziroli.

Page 5: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

5

MAWU OYAMBA

Baibulo limakamba za kulengedwa kwa dziko lapansi komanso Adamu ndi Hava (Genesis 1).

Lamulo loyamba limene Mulungu anawapatsa ndi loti achulukane:

Mulungu ndipo adalenga munthu m'cifanizo cace, m'cifanizo ca Mulungu

adamlenga iye; adalenga iwo mwamuna ndi mkazi.

Mulungu ndipo anadalitsa iwo, ndipo adati kwa iwo, Mubalane, mucuruke,

mudzaze dziko lapansi, muligonjetse: mulamulire pa nsomba za m'nyanja, ndi pa

mbalame za m'mlengalenga, ndi pa zamoyo zonse zakukwawa pa dziko lapansi.

(Genesis 1:27-28).

Kuchulukanaku sikunali kwa kuthupi kokha ayi, komanso kunali kwa ku uzimu. Monga mmene

Adamu ndi Hava amachulukana ku thupindiye kuti akanalidzadza dzikoli ndi enanso ngati

iwowo; amene anamdziwa Mulungu ndi kuyenda mu chiyanjano ndi Iye. Akanakhala

akuchulukana mu uzimu monganso kuthupi.

Kugwa kwa munthu ku uchimo kunaika dongosolo lochulukanali pa chiposezo (Genesis 3).

Tchimo linabweretsa imfa ya kuthupi imene inatchinga kuchulukana kwa kuthupi (Genesis

2:17). Tchimo linabweretsanso imfa ya uzimu imene ndi kulekana kwa uzimu kwa munthu

wochimwa ndi Mulungu wolungama. Ukunso kunatchinga kuchulukana kwa uzimu.

Pakuti Mulungu anamkonda munthu kwambiri, choncho adapanga dongosolo lopulumutsa anthu

ku imfa ya uzimu yowawayi. Mulungu anatumiza Yesu Khristu kufera zolakwa za anthu onse.

Yesu analipira chilango cha imfa mmalo mwathu, keneko anagonjetsa imfa pa kuukanso ku imfa

(Yohane 20).

Munthu aliyense ayenera kusankha kulandira dongosolo la Mulungu la chipulumutso pa

kupempha chikhululukiro cha machimo ndi kulandira Yesu ngati Mpulumutsi. Monga

wokhulupirira mwa Yesu amene machimo ake akhululukidwa, ndiye kuti mwapulumutsidwa ku

imfa ya uzimu.

Ngakhale kuti thupi loonekali lidzafa tsiku lina, mudzakhalabe ndi moyo ku uzimu ndipo

mudalandira matupi atsopano amene adzakhala ndi moyo nthawi zonse.

...Koma tonse tidzasandulika, m'kamphindi, m'kutwanima kwa diso, pa lipenga

lotsiriza; pakuti lipenga lidzalira, ndipo akufa adzaukitsidwa osabvunda, ndipoife

tidzasandulika…Ndipo pamene cobvunda ici cikadzabvala cisabvundi ndi caimfa ici

cikadzabvala cosafa, pamenepo padzacitika mau olembedwa, 20 Imfayo yamezedwa

m'cigonjetso (1 Akorinto 15:51,52,54).

Page 6: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

6

Pamene mwalandira Yesu ngati mpulumutsi wanu, zili ngati kulengedwanso ndi Mulungu

kachiwiri. Baibulo limati “kubadwanso mwatsopano”:

Yesu anayankha nati kwa iye, Indetu, indetu, ndinena ndi iwe, Ngati munthu

sabadwa mwatsopano, sakhoza kuona Ufumu wa Mulungu (Yohane 3:3).

Moti “Kubadwa mwatsopano” sikutanthauza kubadwa kuthupi. Kumatanthauza kubadwa ku

uzimu. Mumalengedwanso ku uzimu monga olengedwa atsopano mwa Khristu. Ndinu

“atsopano” chifukwa simukhalanso mu uchimo ndi kuchita makhalaidwe akale a uchimo:

Cifukwa cace ngati munthu ali yense ali mwa Kristu ali wolengedwa watsopano;

zinthu zakale zapita, taonani, zakhala zatsopano (2 Akorinto 5:17).

Pa chiyambi cha dziko lapansi, Mulungu koyambirira analamulira anthu ake olengedwe

mwatsopano kuti achulukane. Lamulo lake loyamba lolenganso, okhulupirira “obadwa

mwatsopano” ndi chimodzimodzi. Tikuyenera kuchulukana mu uzimu ndi kulidzadza dziko

lapansi ndi ena ngati mmene ifeyo tilili; anthu amene ndi okonda Mulungu ndi kuyenda

muchiyanjano ndi Iye.

Pamene Yesu anayitana anthu kuti amutsatire, uku kunali kuitanira anthu ku chichulukitso cha

uzimu (Luka 5:10). Lamulo lake lomaliza kwa okhulupirira linali loti achulukane ku uzimu

(Machitidwe 1:8). Kuti tikwanitse kufikira anthu zikwi amene akufa ku uchimo asanamve

uthenga, okhulupirira aliyense akuyenera kukhala ochitachita ndi kuphunzira mfundo za

kuchukana ku uzimu.

Phunziroli limagawanso ndi njira za Mbaibulo za kukhala ochitachita mu uzimu zimene

zikupangitsani inu kuchuluka mwa kumvera lamulo la Mulungu. Muphunzira za mmene

mungachulukanire ku uzimu monga munthu komanso ngati gulu pa tchalitchi. Ngati mugwiritse

ntchito mfundo za Mbaibulo zimene zikuphunzitsidwa mu phunziro, muzakhala ndi udindo wa

kuchulukana zikwi kwa okhulupirira ophunzitsidwa ndi olimbikira.

Ngati mukuphunzira maphunziro a Havestime International Institute mwandondomeko, phunziro

ili ndi lachitatu mu mabuku atatu, amene amakamba za kuchulukitsa antchito ophunzitsika a ku

uzimu kupyolera kumapeto kwa buku lachiwiri.

Maphunziro amene akupezeka mu buku la chitatu ndi awa “Kuumba Maonedwe a Dziko a

Mbaibulo,” “Njira Zophunzitsira,” Njira Zochukitsa,” ndi “Mfundo za Mphamvu.” Maphunziro

amenewa amabweretsa chidziwitso cha chosowa cha ku uzimu cha dziko lapansi ndi

kulongosolo za mmene mungafikirire chosowacho kudzera mu ziphunzitso ndi maulaliki a

Mbaibulo, kuchulukana ndi machitachita a mphamvu za uzimu.

Page 7: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

7

ZOLINGA ZA MAPHUNZIROWA

Pakutha pa phunziroli muyenera:

Kubalana ku uzimu kudzera mu kugwiritsa ntchito njira zochulukana za Mbaibulo.

Kuomba mkota pa mfundo za kuchulukana zimene zinaphunzitsidwa mu mafanizo a

Mchipanagano Chatsopano.

Kulongosola mmene okhulupirira angachulukanire ku uzimu pa kubadwisa mazana a

okhulupirira atsopano.

Kupanga kunyumba kwanu ngati malo ochulukaniranapo ku uzimu.

Kuomba mkota pa mfundo za kuchulukana mkati mwa mpingo.

Kuomba mkota pa mfundo za kukulitsa kuchulukana kwa mpingo.

Kuomba mkota pa mfundo za kutalikitsa kuchulukana kwa mpingo.

Kuomba mkota pa mfundo za kulumikiza kuchulukana kwa mpingo.

Kulimbikitsa otembenuka mtima kumene kuti asangokhala ophunzira kokha ayi.

Kudziwa zinthu zimene zimatchinga kuchulukana ku uzimu.

Kukhazikitsa Havestime International Institute ngati malo ochulukana ku uzimu.

Page 8: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

8

CHAPUTALA CHA 1

ASODZI A ANTHU

ZOLINGA:

Pakutha pa chaputalachi muyenera:

Kulemba Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

Kudziwa lamulo loyamba ndi lotsiriza la Yesu kwa ophunzira ake.

Kupereka tanthauzo la “kuchukitsa.”

Kulongosola za kuchulukana kwa ku uzimu.

Kupereka tanthauzo la “njira.”

Kupereka tanthauzo la “ndondomeko za njira”

Kulongosola “njira zosiyanasiyana za kuchulukitsa ku uzimu”

Kuomba mkota pa mfundo za usodzi wodziwika umene tingautanthauzire ku usodzi wa

uzimu.

VESI LOTSOGOLERA:

Ndipo Yesu ananena nao, Idzani pambuyo panga, ndipo ndidzakusandutsani inu

asodzi a anthu (Marko 1:17).

MAWU OYAMBA

Pamene Yesu anayamba utumiki wake pa dziko lapansi, anayitana anthu ambiri kuti akhala

ophunzira ake oyamba:

Ndipo Yesu ananena nao, Idzani pambuyo panga, ndipo ndidzakusandutsani inu

asodzi a anthu (Marko 1:17).

Lamulo loyamba kwa akuphunzira amenewa linali likuti achulukane ku uzimu. Ngati

amamutsatira, Iye anawapanga “asodzi a anthu.” Akanachulukana pamene “amasodza” amuna

ndi akazi ku uzimu.

Uthenga wotsiriza wa Yesu kwa akuphunzira ake unali owaytanira ku kuchulukana ku uzimu:

Komatu mudzalandira mphamvu, Mzimu Woyera atadza pa inu: ndipo

mudzakhala mboni zanga m'Yerusalemu, ndi m'Yudeya lonse, ndi m'Samariya, ndi

kufikira malekezero ace a dziko.

Page 9: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

9

Ndipo m'mene adanena izi, ali cipenyerere iwo, ananyamulidwa; ndipo mtambo

unamlandira iye kumcotsa kumaso kwao (Machitidwe 1:8-9).

Kodi ophunzira akanakwaniritsa bwanji ntchito yotumidwa ndi Yesu? Kodi zikanatheka bwanji

gulu la anthu ochepawa kuchulukana mkufikira dziko lonse?

NJIRA ZOCHULUKITSA

Yesu anaulula njira zenizeni zimene zikanapangisa ophunzira ake kukwaniritsa lamulo

lochulukana ku uzimu. Lamulo loyamba limenenso ndi lofunika linaperekedwa ngati gawo la

kutumidwa ku Machitidwe 1:8. Ophunzira akanachulukana kudzera mu kulandira mphamvu ya

Mzimu Woyera. Njira zina zinaululidwa pamene ophunzira a Yesu anayamba kuchuluka ndi

kufikira dziko lapansi ndi uthenga wabwino. Njira zimenezi zikupezeka mmabuku a Machitidwe

ndi Makalata mu Chipangano Chatsopano.

Phunziroli limalongosola njira za kuchulukanaku. Limaphunzitsa za mmene mungagwiritsire

ntchito kuti muchulukane ku uzimu ndi kukwaniritsa lamulo la Mulungu. Koma koyamba,

muyenera kumvetsetsa pamene tikuti “kuchulukana.” Mawu oti “kuchulukana” akutanthauza

kuti kukhala ambiri mu chiwerengero pa kuberekana. Kuchulukana ndi njira yochulukitsa.

Pamene chinthu chachulukitsidwa, ndiye kuti chikuonjezeraka mobwereza mu mchitidwe

ofanana.

Mu dziko limene timakhalali, amuna ndi akazi amachulukana pokhala ndi ana. Amachulukana

kuthupi. Kuchulukana ku uzimu kumachitika pochulukana ku uzimu. Okhulupirira

amachulukana pogawana uthenga wabwino ndi anthu ena, ndi kuwatsogolera kukhala

okhulupirira, ndi kuwakhazikitsa kukhala ophunzira a Ambuye Yesu Khristu.

Baibulo limaulula za njira za Mulungu za kuchulukana ku uzimu. Choncho “njira” ndi dongosolo

lofuna kukwaniritsa cholinga chapaderadera. Tsono “ndondomeko za njira” ndi dongosolo la

njira zimene zimaikidwa pamodzi kuti mukathe kufikira cholinga chanu.

Motero “Ndondomeko za njira zochulukitsa” ndi njira zimene zimapangitsa okhulupirira kufikira

cholinga chawo cha kuchulukana ku uzimu. Cholinga sichisintha. Tikuyenera kuchulukana ku

uzimu pa kufikira dziko lonse lapansi ndi uthenga wabwino. Pali njira zambiri zimene tingathe

kugwiritsa ntchito kuti tithe kufikira cholingachi. Njirazi ndi “ndondomeko” kapena

madongosolo osiyanasiyana amene tingathe kuchuluka.

Pamene munthu agwira ntchito limodzi ndi njira za Mulungu zochulukitsa, zotsatira zake ndi

kuchulukana ku uzimu. Moti okhulupirira amachulukana mkati mwa mmimba umene ndi

mpingo.

Page 10: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

10

KUITANIDWA KU NTCHITO

Anthu amene Yesu anawaitana koyamba ngati akuphunzira ake anali asodzi. Anali anthu a

ntchito zawo. Samasodza nsomba zawo pakamodzi. Amagwiritsa ntchito maukonde a akulu

ndipo amapha nsomba zochuluka zosiyanasiyana.

Pamene Yesu anawaitana kuti akhale “asodzi a anthu,” amawaululira dongosolo la kuchulukana

ku uzimu. Ophunzira ake amayenera “kusodza” amuna ndi akazi kuchokera ku maiko onse,

zikhalidwe, ziyankhulo ndi mbali zonse za anthu. Maukonde awo a uzimu amayenera adzadze.

Yesu anaitanira anthu ku ntchito. Iye ananena kuti adzawapanga kukhala asodzi a wanthu.

Sadzakhala ozangoyang’anira ntchito dongosolo la Mulungu. Koma adzakhala otenga nawo

mbali pamene adzakhala akusodzera miyoyo ya muyaya ya amuna ndi akazi.

Kuitana kwa Yesu kukadali chimodzimodzi lero lino. Tikuyenera kukhala asodzi a anthu. Ngati

sitikusodza, ndiye kuti sitikutsatira.

ASODZI A ANTHU

Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana ophunzira ake?

Koyamba, chifukwa choti chanali chitsanzo choti akanatha kuchimvetsa mwachangu. Anthu

amenenewa moyo wawo unali usodza. Moti kusodzaku chinali chinthu chimene amachipatsa

nthawi ndi mphamvu yawo. Pamene Yesu anawaitana kuti akhale asodzi a anthu, iwowo

anamvetsa kuti ayamba “kusodza” anthu ku uzimu, monganso mmene amasodzera nsomba

kudziko lapansi. Amatha kumvetsanso zimene zimafunika pa kuitanaku. Kusodza ku uzimu

kumafuna kupereka nthawi komanso mphamvu zawo.

Chachiwiri, Yesu anagwiritsa ntchito chitsanzo cha usodzi poitana ophunzira chifukwa pali

mfundo za kusodza kwa kuthupi kumene kutha kugwiritsidwa ntchito ku uzimu. Mfundozi ndi

izi:

MUKUYENERA KUPITA KUMENE KUMAPEZEKA NSOMBA:

Ngati mukufuna kusodza nsomba, mukuyenera kupezeka kumene nsomba zimapezeka. Nsomba

zimapezeka mmadzi. Simuzasodza nsomba pamene mukuzidikira pamwamba pa phiri kapena

mkatimkati mwa chipululu.

Monga wokhulupirira, mukuyenera kumene kupita kumene nsomba zili ku uzimu. Amuna ndi

akazi amakhala mdziko. Simungamadikirire mu mpingo kuti osakhulupirira akupezeni

Page 11: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

11

momwemo. Mukuyenera kupita kaya ndi pamsika, kusukulu, mmalo ogwiramo ntchito ndi

“kusodza” paliponse pamene pali anthu osapulumutsidwa.

MUKUYENERA KUZINDIKIRA MALO:

Pamene mukusodza ku dziko lapansi, ndi zofunikira kuganizirapo za malo. Mukuyenera

kuonetsetsa kuya kwa madzi pa nthawi imeneyo. Mukuyenera kudziwa kuti madziwo ndi

amchere kapene ayi. Mukuyenera kuonetsetsa mmene mphepo ikuombera. Zinthu zonsezi za

kudzikozi zimatha kukudziwitsani za mtundu wa ngalawa imene komanso njira zimene

mugwiritse ntchito pofuna kusodza.

Momwemonse kudziko lapansi. Mukuyenera kuzindikira malo anu amene mukapezeko amuna

ndi akazi. Kodi zosowa zawo ndi chani? Nanga zimene zikuchitika mmoyo wawo ndi chani? Izi

zidzakuthandizani kudziwa njira zimene mugwiritse ntchito posodza miyoyo yawo.

Pamene Yesu anakumana ndi mkazi pa chitsime ku Yohane 4, Anazindikira malo amene

anampeza iye. Mkaziyo amafuna madzi. Yesu anagwiritsa ntchito madziwo kuti adziwe chosowa

chake cha ku uzimu. Njira imene anagwiritsa ntchito “inamuululira” mu Ufumu wa Mulungu.

Mudzikoli ngati mukugwiritsa ntchito njira zosodzera mtundu wa nsomba umene umakhala

mmadzi amchere, simungasodze nsomba za mtundu umenewo chifukwa sizikhala mmadzi

amchere. Koma zimapezeka mmadzi a bwinobwino.

Ngati simuzindikira malo a mudziko la uzimu, muzapezeka kuti mukusodza mtundu wa nsomba

mmadzi amchere amene nsombazo sizikhalamo. Izi zili chonchi chifukwa simutha kumvetsa

kumene anthu amapezeka ndi mmene mungawafikirire.

MUKUYENERA KUGWIRTSA NTCHITO NJIRA ZOSIYANASIYANA:

Msodzi wabwino amagwiritsa ntchito njira zosiyanasiyana zosodzera nsomba. Amagwiritsa

ntchito zakudya zosiyanasiya kuti athe kukopa nsomba. Amagwiritsanso zipangizo

zosiyanasiyana zophera nsomba monga zitsulo, maukonde, mikondo kapena madengu. Motero

nsomba zosiyana zimakopekanso ndi njira zosiyana zophera. Ichi ndi chifukwa chake nsodzi

ayenera kugwiritsa ntchito njira zosiyanasiyana zophera nsomba.

Choncho nsodzi atha kuphunzira zina mwa njirazi mmabuku omwe amakamba za usodzi. Atha

kuphunzira njirz zina ndi zimene zimachitika komanso kuoneka zokhudza usodzi. Motero njira

zimene amagwiritsa ntchito zimasintha, koma cholinga sichimasintha ndiko kusodza nsomba.

Page 12: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

12

Choncho ngati muli nsodzi wa uzimu wochitachita, mukuyenera kugwiritsa ntchito njira

zosiyanasiyana. Chomwechonso anthu osiyanasiyana amakopeka ndi uthenga wabwino

wolalikidwa mu njira zosiyana. Ena amatha kuvulazidwa ndi uthenga wabwino pomwe ena

amatha kutonthozedwa ndi uthenga wabwino omwewo mu nthawi yosowa. Ena “amakhuzidwa”

ndi njoranzo zosiyanasiyana.

Njira za kusodza mu uzimu ndi zosiyananso, koma cholinga nthawi zonse chimakhala

chomwecho…ndiko kusodza miyoyo ya anthu.

MUKUYENERA KOPONYA NDI KUKOKA:

Kaya mukugwirtsa ntchito chitsulo chosodzera, ukonde, mkondo kumene mumasodza,

mukuyenera kuponya mmadzi ndi kukokanso kawiri.

Mu dziko lathuli, mmene mumaponyera ukonde mmadzi ndizofunuka ndithu. Kuponya kwanu

kukuyenera kukhala kwa chindunji. Mukuyeneranso kugwitsa ntchito chotengera kuti

musungiremo nsomba zanu mukasodza.

Mu dziko la uzimu, talonjezedwa kuti “ngati tiponya mawu a Mulungu” sadzabwerera chabe.

Adzakwaniritsa cholinga chimene chake mmitima ndi mmiyoyo ya anthu (Yesaya 55:11).

Pamene mugwiritsa ntchito mawu a Mulungu, mudzakhala chindunji nthawi zonse. Zotsatira

zake “azasodza” amuna ndi akazi.

MUKUYENERA KUDZIWA NTHAWI:

Nthawi ya tsiku ndi nyengo za pachaka zimakhudza usodzi mdziko lathu. Nsomba zina

zimathawa ndipo simungazisodze mmadera komanso mnyengo zina. Nsomba zambiri

zimasodzedwa kumayambiriro a tsiku pamene zikuyanndikira pamwamba pa madzi kuti zidye.

Ngati mukusodza mu nyengo yolakwika kapene mu nthawi yosayenera, simungasodze nsomba

zambiri.

Nthawi ndi yofunikira ngakhale ku usodzi wa ku uzimu. Muphunzira kutsogolo kwa phunziroli

za kufunika kwa “kusodza” malo olandirika a mdziko pamene nsomba “zimaluma” ku uzimu.

MUKUYENERA KUKHALA ODEKHA:

Munthu amene ndi nsodzi wa kudera lathu amayenera kukhala odekha. Amayenera kudikira

nsomba kuti zilowe mu ukonde. Momwemonse usodzi wa ku uzimu wa kudziko:

Page 13: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

13

Potero, lezani mtima, abale, kufikira kudza kwace kwa Ambuye. Taonani, wolima

munda alindira cipatso cofunikatu ca dziko, ndi kuleza mtima naco kufikira

cikalandira mvula ya myundo ndi masika (Yakobo 5:7).

KUCHULUKANA KU UZIMU

Kusodza kwa dziko lapansi kumachulukitsa nsomba. Kusodza kwa dziko la uzimu

kumachulukitsa anthu mu Ufumu wa Mulungu. Kuberekana kwa anthu kumachulukitsa

chiwerengero cha anthu. Kubalananso mu uzimu kumachulukitsa anthu ku uzimu.

Kuchulukana kwa umunthu ndi zotsatira za moyo. Kuberekana kwa ku uzimu ndi zotsatiranso za

moyo. Sizimabwera kudzera mu dongosolo la munthu ayi. Kuchulukana ku uzimu kumabwera

kudzera mmoyo wa uzimu ochokera kwa Mulungu.

Mu thupi la munthu, kubalana kumayamba mmimba mwa mkazi ndi dzila limodzi la moyo.

Dzilalo limachulukana ku “mimba” ya uzimu ya mpingo. Muphunzira za mmene kuchulukana

kwa ku uzimu kumayambira pamene mukuphunzira za “Tsiku la Zinthu Zochepa” mu chaputala

chikudzachi.

Page 14: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

14

MAYESO ODZIYETSA NOKHA

1. Lembani Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

2. Kodi malamulo oyamba ndi otsiriza amene Yesu anapereka kwa ophunzira ake ndi ati?

___________________________________________________________________________

3. Kodi kuchulukana ndi chani?

___________________________________________________________________________

4. Kodi wokhulupirira amachulukana bwanji ku uzimu?

___________________________________________________________________________

5. Perekani tanthauzo la mawu oti “njira.”

___________________________________________________________________________

6. Perekani tanthauzo la mawu oti “ndondomeko za njira.”

___________________________________________________________________________

7. Longosolani kutanthauza kwa mawu awa “ndondomeko za njira zochulukana ku uzimu.”

___________________________________________________________________________

8. Ombani mkota pa za mfundo usodzi wa kudziko umene umapereka tanthauzo la usodzi

wa ku uzimu.

___________________________________________________________________________

(Mayankho a mafunsowa akupezeka kumapeto kwenkweni kwa bukuli).

Page 15: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

15

KUPITILIZA KUPHUNZIRA

Maitanidwe a Yesu ochulukana ku uzimu si oti munthu atha kusankha kapena kuganizira.

Ndi lamulo ndithu. Werengani tchatili limaene likufananitsa kutuma kwakukulu kumene

Baibulo limakamba. Onani mavesi onse mu Baibulo lanu. Onaninso ulamuliro umene

mulinawo kuti mukwaniritse lamulolo. Onetsetsani kukula kwake kwa utumiki wanu,

uthenga wake, ndi ntchito zimene mukuyenera kuchita mkatikati mochulukana.

Mabuku Ulamuliro Kukula kwake Uthenga Ntchito

Mateyu Ulamuliro Mitundu yonse Zinthu zonse Kupanga

28:1-20 onse zimene Yesu ophonzira

Analamulira pa kupita,

Kubatiza

kuphunzitsa

Marko Dzina la Dziko lonse Uthenga Mukani

16:15 Yesu kwa zolengedwa wabwino mukalalikire,

Zonse kuchiritsa

odwala

Luka Dzina la Mitundu yonse Kulapa kulalikira

24:46-49 Yesu kuyambira Kukhululukidwa kulengeza

Yerusalemu machimo kuchita umboni

Yohane otumidwa ndi (Kukula kwa utumiki, uthenga, ndi ntchito ndi zofanana

20:21 Yesu monga monga ngati Yesu).

Otumidwa ndi

Atate

Machitidwe Mphamvu ya Yerusalemu Mkhristu Mboni

1:8 Mzimu Woyera Yudeya, Samaria

Ndi malekezero a

Dziko lapansi

Page 16: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

16

CHAPUTALA CHA 2

TSIKU LA ZINTHU ZOCHEPA

ZOLINGA:

Pakutha pa chaputalachi muyenera:

Kulemba Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

Kuomba mkota pa za mfundo za kuchukukitsa.

Kudziwa mitundu ya kukula mu uzimu.

Kulemba mndandanda wa mavesi amene amasonyeza kuti kuchukana ndi za Malemba.

Kudziwa zinthu zimene zimaulula zolakwika zokhuza kukula mu chiwerengero.

VESI LOTSOGOLERA:

Pakuti wapeputsa tsiku la tinthu tating'ono ndani? (Zakariya 4:10).

MAWU OYAMBA

Kukula mu thupi la munthu kumayamba ndi dzira limodzi la moyo zimene ndi zotsatira za ubale

waukulu pakati pa mkazi ndi mamuna. Dziralo limachulukana mkati mwa mmimba ya mkazi

kufikira munthu wina amalengedwa. Pamene chakhwima, munthu watsopanoyi amakhalanso ndi

kuthekera kochulukana.

Kukula ku uzimu kumayamba ndi ubale wa pakati pa munthu ndi Ambuye Yesu Khristu. Moyo

wa uzimu umalowa mkati mwa moyo ndi mzimu wa munthu amene walandira Yesu ngati

mpulumutsi. Malawi a moyo, utetezedwa mkati mwa mimba ya uzimu ya mpingo, umakula

kufikira wophunzira watsopano amalengedwa. Wophunzira ameneyi amakhalanso ndi kuthekera

kubadwisa ku uzimu potsogolera enanso kwa Ambuye Yesu Khristu.

Palibe kanthu ndi kudziko la kuthupi kaya la ku uzimu, kuchulukana kumayamba ndi chithu

chimodzi chamoyo ngati dzira. Izi ndi zimene Mulungu ananena:

Pakuti wapeputsa tsiku la tinthu tating'ono ndani? (Zakariya 4:10).

Muchaputala ichi muyamba ndi zinthu zazing’ono. Muphunzira mfundo zenizeni za kuchulukana

ndi mitundu ya kukula mu uzimu. Muphunziranso chidwi cha Mulungu pa kuchulukana kwa ku

uzimu ndi zinthu zina zimene zimaonetsa maganizo olakwika pa kukula mu chiwerengero.

Muyamba ndi mfundo zenizeni, zinthu zochepa zimene zazikulu zimachokerapo.

Page 17: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

17

MFUNDO ZENIZENI ZA KUCHULUKANA

Mukuyenera kumvetsa mfundo zenizeni za kuchulukana ku uzimu kuti muthe kuphunzira ndi

kugwiritsa ntchito ndondomeko za njira zake. Mfundo za kuchulukana sizimasintha, komano

njira zimene mumagwiritsa ntchito ndi zimene zimasintha. Njira zimasintha, koma cholinga

chimakhala chomwecho chomwecho sichimasintha.

Cholinga komanso mfundo za Mulungu nthawi zonse zimakhala zomwezo, koma njira zofikira

zolingazi zimasintha. Cholinga cha Mulungu kuchokera pachiyambi chakhala….

...Kuti pa tinakonzedwe a makwaniridwe a nyengozo, akasonkhanitse pamodzi

zonse mwa Kristu, za kumwamba, ndi za padziko (Aefeso 1:10).

Monga moyo wawo wa uzimu wa anthu ake ndi masinthidwe a mbiri ya nyengo za amitundu,

Mulungu amasintha njira zake monga zifunikira kuti akwaniritse cholinga chake. Mwachitsanzo,

pamene atate mbanja la Israyeli analephera ntchito yawo ku uzimu, Mulungu anadzutsa

ansemba. Pamene ansembe anayamba za chinyengo, anaitana aneneri kukhala ngati atsogoleri a

kuuzimu.

Yesu anagwiritsa ntchito njira zosiyana za utumiki. Sanathandize anthu onse mofanana. Njira

zake zinali zosiyana, koma cholinga chake chinali sichinasinthe ndiko …Kukhudza ndi kusintha

miyoyo ya anthu.

Izi ndi zina mwa mfundo zenizeni zimene mukuyenera kudzimvetsa mu “tsiku la zinthu

zochepa” musanayambe kuchulukana:

MULUNGU AMAKHALA NDI CHIDWI NDI GULU LA ANTHU:

Chidwi cha Mulungu nthawi zonse chakhala pa dziko lonse:

Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi kotero, kuti anapatsa Mwana wace

wobadwa yekha, kuti yense wakukhulupirira iye asatayike, koma akhale nao moyo

wosatha (Yohane 3:16).

Mulungu….

...wosafuna kuti ena aonongeke, koma kuti onse afike kukulapa (II Petro 3:9).

Yesu anaonetsa chidwi chomwecho pamene anati:

Page 18: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

18

Pakuti Mwana wa munthu anadza kufunafuna ndi kupulumutsa, cotayikaco (Luka

19:10).

…pakuti sindinadza kudzaitana olungama, koma ocimwa (Mateyu 9:13).

Mulungu amakhuzidwa ndi gulu la anthu. Amakhuzidwanso ndi chiwerengero. Komanso

amkhuzidwa ndi kuchulukana kwa okhulupirira amene amachulukana pa kulalikira uthenga

wabwino. Pamene mukuyamba phunziro la njira zochulukitsa, muyamba ndi chidwi chomwecho

ngati Mulungu—amene akufikira dziko lonse ndi uthenga wabwino.

NDI MULUNGU AMENE AMABWERETSA KUKULA:

Kuchulukana mu uzimu sikungakwaniritsidwe popandapo Mulungu. Mulungu ndiye amene

amabweretsa kukula:

…kama Mulungu anakulitsa (I Akorinto 3:6).

MUNTHU AYENERA KUGWIRIZANA NDI MFUNDO ZA MULUMGU:

Mmawu mulu mfundo za Mulungu zimene zimagwiritsidwa ntchito mmagawo onse a moyo ndi

utumiki wathu. Mulungu amagwira ntchito kudzera mwa anthu amene amadziwa kugwiriza ndi

mfundozi. Kuchokera pa chiyambi cha dziko lapansi, Mulungu wakhala akugwira ntchito

padzikoli kudzera mwa anthu. Adampatsa Adamu ndi Hava ntchito yosamalira munda.

Anagwiritsa ntchito munthu wotchedwa Nowa kuti ateteze moyo pa dziko munthawi ya

chigumula cha madzi.

Mulungu anadzutsa Abrahamu kukhala woyamba wa mtundu wa Israyeli umene kudzera mwa

iye anadziululu yekha kwa mitundu ina ya dziko lapansi. Mulungu anagwiritsanso ntchito

aneneri, mafumu ndi oweruza kuti akwaniritse cholinga chake mu nthawi ya Chipangano

Chakale.

Muchipangano Chatsopano, munthu wotchedwa Yohane Mbatizi, “anakonzekeretsa njira ya

Ambuye.” Yesu anayamba utumiki wake ndi anthu wamba ndipo pamene anabwerera

kumwamba adasiya tsogolo lake la Uthenga wabwino mmanja mwa akuphunzira ake. Nkhani

yonse ya Mbaibulo ndi imodzi ya kwa munthu amene akugwirizana ndi mfundo za Mulungu ndi

cholinga chofuna kufikira cholinga chake.

Izi ndi zoona mu kuchulukana kwa ku uzimu. Mulungu samusiya munthu kumbali kuti afalitse

mau ake. Amagwiritsa ntchito anthu amene amavetsa ndi kugwirizana ndi mfundo zake za

kuchulukana. Paulo anaomba mkota za mgwirizano wa ubalewu:

Page 19: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

19

Ndinanka ine, anathirira Apolo; kama Mulungu anakulitsa (I Akorinto 3:6).

Paulo anatsindika za change cha okhulupirira kukwaniritsa udindo wawo mu dongosolo la

Mulungu.

Pakuti, amene ali yense adzaitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka. 14Ndipo iwo

adzaitana bwanji pa iye amene sanamkhulupirira? ndipo adzakhulupirira bwanji

iye amene sanamva za iye? ndipo adzamva bwanji wopanda wolalikira? Aroma

(10:13-14).

YESU NDIYE MASO ATHU A KUCHULUKITSA:

Yesu anati:

Ndipo Ine, m'mene ndikakwezedwa kudziko, ndidzakoka anthu onse kwa Ine

ndekha (Yohane 12:32).

Yesu apapa amalankhula za “kukweza pamwamba” pa mtanda pamene anafera zochimwa za

anthu onse. Kupyolera mu imfa yake, adzakoka anthu onse mwa mphamvu ya uthenga wake.

Pamene mugawira anthu uthenga wabwino, Yesu amakwezedwa pamwamba. Pamene

wakwezedwa mmoyo wanu ndi mumpingo wanu, anthu amaitanidwa ndi mphamvu ya uthenga

wabwino. Kuchulukanatu ndi kotheka ngati Yesu wakwezedwa pamwamba.

MAWU A MULUNGU AMAYAMBITSA KUKULA:

Yesu anafotokozapo za fanizo la kukula mu Mateyu 13:1-9. Analongosola fanizolo kuyambira

Mateyu 13:18-23. Werengani ndimeyi mu Baibulo lanu. Mu fanizoli, mbewu zimaimira Mau a

Mulungu. Mulungu analonjeza kuti pamene tabzala Mau ake, sadzapita pachabe.

Momwemo adzakhala mau anga amene aturuka m'kamwa mwanga, sadzabwerera

kwa Ine cabe, koma adzacita cimene ndifuna, ndipo adzakula m'mene

ndinawatumizira (Yesaya 55:11).

…Waona bwino pakuti Ine ndidzadikira mau anga kuwacita (Yeremiya 1:12).

Mawu a Mulungu ndiwo amene amabweretsa kusintha mmiyoyo ya anthu. Kusinthako

kumabweretsa kukula komanso kuchukukana molingana ndi Mau a Mulungu.

MZIMU WOYERA AMABWERETSA KUCHULUKANA:

Page 20: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

20

Mu unthenga wake otsiriza wa Yesu kwa ophunzira ake anati:

Komatu mudzalandira mphamvu Mzimu Woyera atadza pa inu: ndipo mudzakhala

mboni zanga m'Yerusalemu, ndi m'Yudeya lonse, ndi m'Samariya, ndi kufikira

malekezero ace a dziko (Machitidwe 1:8).

Mphamvu ya Mzimu Woyera ndi imene imapangitsa kuchulukana. Mphatso za Mzimu Woyera

zimakonzekeretsa kuchulukana. Chipatso cha Mzimu Woyyera chimapangitsa kuberekana.

Tisanthula nchito ya Mzimu Woyera mu kuchulukana kwa ku uzimu kumapeto kwa phunziroli.

KUCHULUKANA NDI UDINDO WOTHANDIZANA:

Mu nthawi ya mpingo woyamba, kufalikira kwa uthenga wabwino sikunali kwa azibusa, aneneri,

alaliki, ndi aphunzitsi amene anali ndi mipingo yawo ayi. Okhulupirira wina aliyense wa

Chipangano Chatsopano amachulukana ku uzimu. Ngati tikufuna tifikire dziko ndi uthenga

wabwino tikuyenera kuchita ngati mpingo woyamba. Kuyambira atsogoleri ndi anthu wamba

akuyenera kugawana udindo wa kuchulukana ku uzimu. Kukula kwa dziko mu chiwerengero

kukufunika membala wina aliyense amene ali mu thupi la Khristu kubwerera ku dongosolo la

utumiki wa mu Chipangano Chatsopano. Sitingafikira dziko lapansi ndi kumangodzionetsera

kapena kudzipereka mosakwanira.

Pali ndithu akhristu okwanira mu dziko lapansi amene angathe kufikira dziko lonse lapansi ndi

uthenga wabwino. Koma amene akusowa ndi chiwerengero chokwanira cha akhoza kukhudzika

ndi kuvomera mwayi wa kuchulukana.

Lamulo limene linaperekedwa ndi Yesu kwa okhulupirira loti “mukani” kudziko lonse ndi

uthenga wabwino. Simukuyenera kudikira lamulo loti “mukani” chifukwa linaperekedwa kale.

Mogwirizana ndi uthenga wabwino, lamulo ndi lakuti “mukani” ndipo penyetsetsani zoletsa,

osati kusiya ndi kudikira “kumuka.”

MITUNDU YA KUKULA

Baibulo limatiuza za mitundu inayi ya kukula kapena kuchulukana:

KUKULA MU MADERA:

Kukula kumeneku kunaloseredwa kale ndi Ambuye Yesu:

Page 21: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

21

Komatu mudzalandira mphamvu Mzimu Woyera atadza pa inu: ndipo mudzakhala

mboni zanga m'Yerusalemu, ndi m'Yudeya lonse, ndi m'Samariya, ndi kufikira

malekezero ace a dziko (Machitidwe 1:8).

Kukula kukuyenera kufikira ngakhale madera a mitundu yonse ya dziko lapansi.

KUKULA MU CHIWERENGERO:

Mpingo ukuyenera kukula mu chiwerengero pamene ukukula mmadera. Kukula mu

chiwerengero kwa mpingo kumapezeka mu buku la Machitidwe. Mwachitsanzo, mpingo unakula

kuchokera 12 kufika 120 Machitidwe 1:15, mkuzafika 3,000 Mchitidwe 2:41 ndi kuzafika 5,000

Machitidwe 4:4.

KUKULA KU MITUNDU:

Mpingo woyamba unakulanso ku mitundu. Uthenga wabwino unafalikira kupitilira Ayuda

mpaka amitundu (anthu a mitundu yonse).

KUKULA KU UZIMU:

Kukula mu chiwerengero si ndiye kuti ndi kukuchukana ku uzimu. Pamene mukuphunzira

phunziroli, kukula ku uzimu kwa mkati ndikofunikiranso. Otsatira a Yesu akuyenera kukula mu

makhalidwe a uzimu momwemonso mu chiwerengero.

Koma kulani n'cisomo ndi cizindikiritso ca Ambure wathu ndi Mpulumutsi Yesu

Khristu (II Petro 3:18).

Khumbo la Mulungu ndi loti…

Koma ndi kucita zoona mwa cikondi tikakule m'zinthu zonse, kufikira iye amene ali

mutu ndiye Kristu (Aefeso 4:15).

KUSINDIKA ZA CHIWERENGERO

Anthu ambiri amakana nkhani ya kuchulukana ku uzimu ndi kukula kwa mpingo chifukwa

amakhulupirira kuti kumakamba za chiwerengero ndi zolakwika. Komatu Mbaibulo muli mawu

ambiri amene amakamba za chiwerengero. Mwachtsanzo onani Numeri 1:1-3; 2:23-24; 26:1-4;

Chibvumbulutso 7:9; 20:8; Genesis 22:17; ndi Ahebri 6:14.

Page 22: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

22

Yesu analankhulapo za mafanizo ambiro okhuza kukula mu chiwerengero. Muziphunzira

zimenezi mu phunziro lina. Anaonetseranso kuti kukula kwenikweni kwa chiwerengero

kunalembedwa Kumwamba:

Ndinena kwa inu, kotero kudzakhala cimwemwe Kumwamba cifukwa ca wocimwa

mmodzi wotembenuka mtima, koposa anthu olungama makumi asanu ndi anai

mphambu asanu ndi anai, amene alibe kusowa kutembenuka mtima (Luka 15:7).

Kuchulukanaku kumapezekanso mu mbiri ya mpingo mu buku la Machitidwe. Chidule cha

kukula kwa mpingo kumapezeka mu buku la Machitidwe monga 1:15; 2:41; 4:4; 6:7; 9:31;

12:24; 16:5; 19:20; ndi 28:30-31.

Simukuyanera kukana nkhani ya kuchulukana chifukwa cha mavuto ochepa amene apezeka

chifukwa cha maganizo olakwika a zakuchulukana. Komano, mukuyenera kudziwa ndi kuthana

ndi mavutowo. Pali kuganiza kolakwika pa nkhani ya kuchulukana pamene zinthu izi

zikupezeka:

KUKULA MU CHIWERENGERO NKOFUNIKA KUPOSA KUKULA MU UZIMU:

Pamene kukula mu uzimu kwaleka kukopa gulu la anthu, pamakhala kulakwa kolankhulano za

chiwerengero. Atumiki ambiri amalankhula zimene anthu amazikonda kuzimva ndi cholinga

chofuna kukopa khamu lambiri. Koma Baibulo limachenjeza kuti…

Pakuti idzafika nthawi imene sadzalola ciphunzitso colamitsa; komatu poyabwa

m'khutu adzadziuniikitsa aphunzitsi monga mwa zilakolako za iwo okha: ndipo

adzalubza dala pacoonadi, nadzapatukira kutsata nthanu zacabe (II Timoteo 4:3-4).

KUDZIKWEZA KUMATSOGOLA:

Werengani I Mbiri 21:18. Chidwi cha Davide pa chiwerengero chimogozana ndi Satana ndipo

unali mchitidwe wa kudzikudza. Pamene muyamba kusangalala ndi khamu lalikulu la anthu,

ndiye kuti chidwi chanu ndi cholakwika.

KUDZIYENEREZA KUMAKHALAPO:

Pali tchimo la kuthupi limeme pa Agalatiya 5:20 amalitcha kuti “kudzidierekeza” kumene ndi

mchitidwe wa ngati nsanje, umene zotsatira zake ndi kuzifanizira ndi anthu ena pa nkhani ya

chipambano. Pamene muli a nsanje chifukwa cha mautumiki a pamwamba ndi kuyamba

kumazifanizira ndi ena ndi cholinga choti mukule, ndiye kuti muli ndi maganizo pa nkhani ya

chiwerengero.

Page 23: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

23

CHIDWI CHIMAKHALA PA KUKULA KWA MPINGO MMALO MWA UFUMU WA

MULUNGU

Cholinga cha kuchulukana mu uzimu ndiko kutembenuza anthu anthu kupita kwa Yesu Khristu

ndi kuyamba kuwaphunzitsa kufikira akhala anthu odalilika, ndi wochitachita mu ufumu wa

Mulungu. Pali kusiyana pakati pa kukula kwa mpingo ndi kukula kwa ufumu. Ngati mpingo

woyamba ugawanika ndipo 100 mwa mamembala awo akupita ku mpingo wachiwiri, ndiye kuti

kukula kwa mpingo kwachitika mu mpingo wachiwiri, koma palibe kukula kwa Ufumu.

Kuchulukana sikunachitike. Kwangokhala kusinthana kwa mamembala omwe analipo kale.

Cholinga cha kuchulukana si kukopa mamembala atsopano kuchoka mu mpingo wina, koma

kufikira iwo amene sanamve uthenga wabwino. Kuika chidwi pa chiwerengero ndi zolakwika

pamene cholinga cha kukula kwa mpingo chikusinthana ndi kukula kwa Ufumu.

MUNTHU MMODZI AMAKANIDWA:

Yesu anatumikira kwa anthu ambiri panthawi ya utumiki wake (Luka 6:17; 7:11; 8:37; 9:14-16;

14:26; 23:27; Yohane 6:2). Koma Yesu sanakane munthu ngakhale mmodzi chifukwa cha

khamu la anthu. Amaitana anthu ngakhale pakati pa khamu la anthu ndi kuwatumikira (Yohane

5:3-13; Marko 5:24-34). Mu Yohane 4, anatumikira kwa mkazi mmodzi amene pamapeto pake

anabweretsa khamu la mudzi wonse kwa Yesu.

Ku machitidwe 8 pali nkhani ya chitsitsimutso chachikulu chimene analalikira Filipo mu mzinda

wa Samariya. Mkatikati mwa mikumano yawo Mulungu analankhula kwa Filipo kuti achoke ku

Samariya ndi kupita ku chipululu pakati pa Yerusalemu ndi Gaza.

Filipo mwachangu anachoka mkusiya chitsitsimutso chachikulu chimene amatumikira.

Anachoka kudziko kumene kunali anthu ambiri pamodzi mkupita kumalo ayekha. Annsiya

khamu ndi cholinga chofuna kutumikira munthu mmodzi, mdindo wa ku Itopiya amane

amachokera ku Yerusalemu. Munthuyi mkutheka anali ndi kuthekera kofalisa uthenga wabwino

mu mbali yonse ya Afilika.

Zaka zambiri zapitazo ku Mangalande pa ntchito ya umishoni anthu awiri okha ndi amene

amapezeka chifukwa cha nyengo yoipa. Mtumiki woyitanidwayo amayesera kupempha

Achimwenye amane amkagwira ntchito kummawa kwa Amerika, koma anaganiza kuti

amaononga nthawi chifukwa cha kuchepa kwa anthu. Koma mmodzi wa anthu awiriwa anamva

kuitana kwa Mulungu ndipo anapereka moyo wake kwa Mulungu. Mwezi usanathe anagulitsa

malonda ake ndipo amakonzeka kukagwira ntchito kwa Amwenye kummawa kwa Amerika.

Anakhalako zaka 35 akuchita utumiki pakati pa athuwa. Dzina lake linali David Brainard.

Page 24: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

24

Musanyoze zinthu zochepa. Kumbukirani, kuwala kochepa kungawale kuposa mmene dzuwa

limawalira…kukhoza kuwala usiku.

CHIDWI CHIMACHOKA PA ANTHU MKUKHALA PA ZINTHU:

Pamene kuchulukana kwabweretsa kukula kwa mpingo, chidwi chathu nthawi zambiri

chimachoka pa anthu mkupita pa zinthu. Chifukwa cha kukula, mamangidwe a mpingo waukulu

amafunika ndipo zochita zimachoka pa kuchulukitsa ophunzira mkupita pa mamangidwe a

mpingo. Pamene chidwi chanu chachikulu chili pa mamangidwe ndi cholinga chofuna kukhala

ndi anthu ambiri, chiwerengero chimapangitsa inu kuiwala cholinga chanu chenicheni.

Mulungu amakhuzidwa kwambiri ndi anthu kuposa mamangidwe. Mbiri ya Baibulo ya ntchito

ya Mulungu mdziko imakhala pa anthu. Pamene kuchuluka kwapangitsa kuchotsa chidwi pa

anthu mkuika pa zinthu monga mamangidwe, ndiye kuti zimenezi ndi zolakwika.

ENA AMAWERUZIDWA POYANG’ANA CHIWERENGERO:

Sibwino kuweruza uzimu wa munthu wina kapena utumiki poyang’ana chiwerengero. Khamu

lanthu si chizindikiro cha uzimu. Chipambano mu chiwerengero nthawi zina si umboni oti

mpingo walephera kukhala mpingo. Nthawi zina, kukhulupirika ku Mau a Mulungu ndipo Yesu

Khristu amabweza osati kukopa. Mwachitsanzo, pamene Yesu anayamba kuphunzitsa uthenga

wosatchuka wa imfa yake, ambir amene amamutsata Iye amasiya kumutsata (Yohane 6:52-64).

Pali zifukwa zina zimene zimapangitsa kuti kukula kusaoneke. Baibulo limaphunzitsa kuti pali

nyengo zina za kukula mu zimu monganso pali kukula kwa zinthu ku dziko. Mu dziko lathuli,

nyengo zina za chaka zomera sizimaberekana. Zimakhala opanda masamba kapena zipatso

mkumaoneka ngati nthambi zokufa pa nthaka. Koma mu nyengo yoyenera, zomerazi

zimaberekana moti masamba komanso zipatso zimaonekera.

Momwemonso kudziko la uzimu. Pali nthawi zina pamene malo ena mdzikomu amalandira

uthenga wabwino kuposa malo ena. Pa kudziwa ndandandawu wa kakulidwewu mukhoza kuika

chidwi pa zochita zanu za moyo wa uzimu mmunda “kupsa mkukolora.”

Ndondomeko za chiwerengero cha Mulungu sizifanana ndi za munthu. Tipaphatikiza kuti

tichukulukane. Koma nthawi zina Mulungu amachotsera ndi cholinga chofuna kuchulukana.

Pamene Hananiya ndi Safira anachotsedwa mu mpingo chifukwa cha uchimo (Machitidwe 5),

okhulupirira anaonjezeredwa (Machitidwe 5:14). Nthawi zina Mulungu amagwiritsa ntchito

mgawano pofuna kuchulukitsa. Pamene Paulo ndi Banaba anagawana, Mulungu anachulukitsa

mphamvu ya umishoni (Machitidwe 15:36-41). Nthawi zambiri Mulungu amachepetsa

Page 25: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

25

chiwerengero ndi cholinga chofuna kukwaniritsa cholinga chake chachikulu. Werengani nkhani

ya Gideoni mu Oweruza 7.

Musaweruze utumiki kapena munthu poyang’ana chiwerengero. “Osapeputsa zinthu zochepa.

Pamene mnyamata anapereka mkatendi nsomba ziwiri kwa Yesu, zinafikira chosowa cha khamu

la anthu amene anali ndi njala. Mulungu amagwiritsa ntchito zinthu zonyozeka, mkuzidalitsa, ndi

kudzigwiritsa ntchito ku ulemerero wa dzina lake.

ZOTSATIRA ZAKE NDI KUBWERETSA KHOLOLA

Pokana maganizo olakwikwa otsindikiza za chiwerengero zisalepheretse maphunzirowa ndi

kugwiritsa ntchito njira za kuchulukutsa. Fanizo la (Mateyu 25:14-30) likuonetseratu kuti

Mulungu amayembekezera inu kuti muchulukane ndi zimene mwapatsidwa choncho kukhala ndi

madandaulo chifukwa cha mantha sizoloredwa.

Kodi simunena inu, kuti, Yatsala miyezi inai, ndipo kudza kumweta? Onani

ndinena kwa inu, Kwezani maso anu, nimuyang'ane m'minda, kuti mwayera kale

kufikira kumweta (Yohane 4:35).

Pamene Mulungu atumiza okolola mmunda wa uzimu ku dziko, amafuna iwo abwere ndi kholola

osati madandaulo:

Akubzala ndi misozi adzatuta ndi kupfuula mokondwera.

Iye amene ayendayenda nalira, ponyamula mbeu yakufesa;

Adzabweranso ndithu ndi kupfuula mokondwera, alikunyamula mitolo yace

(Masalmo 126: 5-6).

Page 26: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

26

MAYESO ODZIYETSA NOKHA

1. Lembani Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

___________________________________________________________________________

2. Lembani mfundo zenizeni za kuchulukitsa zimene mwaphunzira mu phunziroli.

___________________________________________________________________________

3. Tchulani mitundu inayi ya kukula mu uzimu.

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

4. Lembani mavesi amene amaonetsa chidwi kuti kuchulukana ndi zochokera Mmalemba.

___________________________________________________________________________

5. Lembani mwachidule zinthu zimene mwaphunzira zosonyeza kuganiza kolakwikwa pa

kukula mu chiwerengero.

________________________________________________________________________

6. Zoona kapena Zonama: ngati chiganizo chili choona, lembani “zoona” mumpata

koyambirira kwa chiganizo. Ngati chiganizo chili chonama, lembani “zonama mumpata.

a. _______________Amaika chidwi pa chiwerengero si za Mmalemba.

b. _______________Ngati mpingo sukukula, ndiye kuti uzimu palibe.

(Mayankho a mafunsowa akupezeka kumapeto kweikweni kwa bukuli).

Page 27: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

27

KUPITILIZA KUPHUNZIRA

Buku la Machitidwe limatiuza nkhani ya kuchulukana kwa mpingo woyamba. Gwiritsani ntchito

magawowa kuti muphunzire bukuli la Chipangano Chatsopano. Magawowa amatsata dongosolo

la kuchulukana la Ambuye limene limnaperekedwa pa Machitidwe 1:8 pa za kufalitsa uthenga

wabwino kuchokera ku Yerusalemu, kupita ku Yudeya, Samariya, ndi malekedzero a dziko

lapansi.

Wolemba buku: Luka

Kumene amalembera: Bukuli amalembera okhulupirira onse, ngakhale amalembera kwa

munthu wotchedwa Tiofelo.

Cholinga chimene amalembera buku: Ichi chikupezeka mu Machitidwe 1:1-2. Bukuli limaika

chidwi pa zimene Yesu anapitiliza kuchita ndi kuphunzitsa atangokwera kupita kumwamba mu

thupi lake la uzimu, ndiye Mpingo.

Vesi Lotsogolera: Machitidwe 1:8

Mawu oyamba

Machitdwe 1:1-11

I. Mawu oyamba: 1:1-2

A. Kwa: Teofelo: 1:1

B. Okhuzana: Zimene Yesu adapitiliza kuchita ndi kuphunzitsa atangopita kumwamba

mu thupi lake la ulemerero, Mpingo: 1:1-2

II. Utumiki wa Yesu atatha kuukitsidwa: 1:3

A. Masiku ake: Makumi anayi: 1:3

B. Cholinga chake: Zitsikimizo zosakaikitsa: 1:3

C. Uthenga wake: Ufumu wa Mulungu: 1:3

III. Mkumano wotsiriza wa Yesu ndi akuphunzira ake: 1:4-8

Page 28: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

28

A. Lamulo la ophunzira: 1:4-5

B. Funso la ophunzira: 1:6

C. Chenjezo kwa ophunzira: 1:7

D. Kutuma ophunzira: 1:8

IV. Kukwera kwa Yesu kupita kumwamba: 1:9-11

A. Kulongosola za kukwerako: 1:9

B. Kulengeza za kubwera kwake kwachiwiri: 1:10-11

Gawo Loyamba:

Kupanga mboni ku Yerusalemu

Machitidwe 1:12-7

I. Kukonzekeretsa mboni: 1:12-2:4

A. Ophunzira aYesu kudikirira ku Yerusalemu: 1:12-26

1. Kusonkhana kwa ophunzira: 1:12-15

a. Malo awo okumaniranapo: 1:12-13

b. Chiwerengero chawo ndi mayina awo: 1:13-15

c. Cholinga chawo: 1:14

2. Chilimbikitso chopita kwa ophunzira: 1:15-22

a. Wolankhula: Petulo: 1:15

b. Uthenga 1:16-22

(l) Chiyambi: 1:16-20

(2) Malangizo: 1:21-22

3. Yankho la akuphunzira: 1:23-26

a. Maina oti asankhidwe: 1:23

b. Pemphero: 1:24-25

c. Maere: 1:26

B. Ubatizo mwa Mzimu Woyera: 2:1-4

1. Mmene zinakhalira: 2:1

2. Anthu: 2:1

3. Malo ake: 2:1

4. Chochitikacho: 2:2-4

a. Mphepo: 2:2

Page 29: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

29

b. Malilime a moto: 2:3

c. SKulankhula: 2:4

Gawo Lachiwiri: Ntchito yochitira umbini ku Yerusalemu

Machitdwe 2:5-7

I. Mboni zoyamba: 2:4-40

A. Mmene umboni unaperekedwera: 2:4-6

B. Zotsatira za umboni: 2:7-13

C. Ulaliki wa Petulo: 2:14-36

1. Uneneri wokhuzana ndi nthawi: 2:17

2. Uneneri wokhuzana ndi mzimu: 2: 17-18

3. Uneneri wokhuzana ndi chochitikacho: 2:19-20

4. Uneneri wokhuzana ndi chipulumutso: 2:21

5. Ntchito ya Yesu: 2:22-36

a. Yesu adatsimikizidwa ndi Mulungu: 2:22

b. Yesu adapachikidwa: 2:23

c. Yesu adauka kwa akufa: 2:24-32

d. Yesu adakwezedwa pa dzanja lamanja la Mulungu: 2:33-35

e. Yesu ndi Mbuye ndi Khristu: 2:36

D. Zotsatira atamva uthenga: 2:37-40

1. Kutsutsika: 2:37

2. Kufunsa: 2:37

3. Langizo: 2:38

4. Malonjezo: 2:38-39

5. Chilimbikitso: 2:40

II. Mpingo woyamba: 2:41-47

A. Chiwerengero cha anthu mu mpingo woyamba: 2:41

1. Chizindikiro chawo: Iwo amene adalandira Mawu.

2. Chiwerengero chinali: Zikwi zitatu 3,000

B. Makhalidwe a Uzimu a mpingo woyamba: 2:42

1. Chiphunzitso cha atumwi.

2. Chiyanjano cha oyera mtima.

3. Mgonero.

4. Pemphero.

C. Chikhalidwe cha mpingo woyamba: 2:44-46

Page 30: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

30

1. Machitdwe awo a moyo watsiku ndi tsiku: 2:44-45

2. Kulambira ndi kuchitira umboni tsiku ndi tsiku: 2:46

3. Kuchita chiyanjano mmanyumba: 2:46

4. Umodzi: 2:46

D. Umboni wa mpingo watsopano: 2:46-47

1. Chikhalidwe cha umboni: 2:46-47

2. Zotsatira za umboni: 2:47

III. Chozizwa choyamba: 3:1-26

A. Mmene chozizwa chinalili: 3:1-11

1. Malo ake: 3:1

2. Munthu ndi chosowa chake: 3:2-3

3. Uthenga: 3:4-6

4. Chozizwa: 3:7-8

5. Zimene khamu linachita: 3:9-11

B. Kulongosola chozizwa: 3:12-18

1. Munthuyo sanachiritsidwe ndi mphamvu ya atumwi: 3:12

2. Munthuyo anachiritsidwa ndi Mulungu kuti apereke ulemerero kwa Yesu:

3:13-15

3. Munthuyo anachiritsidwa mwa chikhulupiriro mdzina la Yesu: 3:16

4. Munthuyo anachiritsidwa kuti akaonetsere kukwaniritsidwa kwa uneneri:

3:17-18

C. Uthenga wa Petulo: 3:19-26

1. Lonjezo limene Petulo adalinena: 3:19-21

a. Chimene Mulungu adatsimikizira Israyeli kuchita: 3:19

b. Chimene Mulungu adalonjeza kuchita: 3:19-21

2. Uneneri wa aneneri: 3:22-26

a. Uneneri wa Mose ndi aneneri: 3:22-24

b. Lonjezo la pangano: 3:25

c. Dongosolo la Mesiya: 3:26

IV. Chitsutso choyamba: 4:1-31

A. Kumangidwa: 4:1-4

1. Choyambitsa chitsutso: 4:1

2. Cholinga cha chitsutso: 4:2

3. Mtundu wa chitsutso: 4:3

Page 31: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

31

B. Kuyesedwa: 4:5-14

1. Kubwalo la milandu: 4:5-6

2. Mafunso akubwalo la minlandu: 4:7

3. Mawu a Petulo: 4:8-12

a. Maziko a yankho lake: 4:8

b. Yankho lake: 4:9-10

c. Umboni wake wa Yesu: 4:10-12

d. Chilengezo chake cha chipulumutso: 4:12

4. Umboni wa oweruza milandu: 4:13-14

a. Chikhalidwe cha umboni: 4:13

b. Umboni wa munthu amene anachiritsidwa: 4:14

5. Chisankho: 4:15-22

a. Kufuna uphungu: 4:15-17

b. Chisanhko: 4:17-18

c. Yankho la Petulo ndi Yohane: 4:19-20

d. Kumasulidwa: 4:21-22

6. Zimene adachita: 4:21-31

a. Pemphero la mpingo: 4:23-30

b. Ntchito ya mpingo: 4:31

V. Mwambo oyamba wa tchimo: 4:32-5:16

A. Dongosolo la mpingo: 4:32-37

1. Chiyanjano chake: 4:32

2. Umboni wake: 4:33

3. Chuma chake: 4:32-37

B. Tchimo loyamba ndilo loononga chiyanjano: 5:1-10

1. Tchimo: 5:1-2

2. Kuonekera poyera kwa tchimo: 5:3-4

3. Mwambo wake wa tchimo: 5:5-10

C. Zotsatira za mwambo: Umboni wobala chipatso wa chiyanjano: 5:11-16

1. Malingaliro a mantha a mamembala: 5:11

2. Umodzi: 5:12

3. Zozizwa: 5:12, 15-16

4. Zomwe anthu adachita: 5:12-14

Page 32: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

32

VI. Chizunzo choyamba: 5:17-43

A. Maziko a chitsutso: 5:17

B. Zotsatira za chitsutso: 5:18

C. Chiombolo cha Mulungu: 5:19-26

1. Ntchito Zake: 5:19

2. Lamulo Lake: 5:20

3. Zomwe adachita ndi lamulo Lake: 5:21

4. Kuzindikira ntchito zake: 5:21-23

5. Zotsatira za ntchito Zake: 5:24-26

D. Kuyesedwa: 5:27-40

1. Lamulo la akuluakulu: 5:27-28

2. Chozitchinjiriza cha Petulo: 5:29-32

3. Kusanthula kwa akuluakulu: 5:33-39

4. Chisankho chosalungama cha akuluakulu: 5:40

E. Zotsatira za chizunzocho: 5:41-42

1. Chikondwerero: 5:41

2. Umodzi: Kukumana tsiku ndi tsiku limodzi: 5:42

3. Kuchitira umboni: Kuphunzitsa ndi Kulalikira: 5:42

VII. Atumiki oyamba: 6:1-7

A. Kufunikira kwa atumikiwo: 6:1

B. Atumikiwo anasankhidwa: 6:2-4

1. Maziko a kusankhidwako: 6:2

2. Cholinga cha kus: 6:2 ankhidwako

3. Chisankhocho: 6:3

4. Kufunikira kwa kusankhidwako: 6:4

C. Atumiki akhazikitsidwa: 6:5-6

1. Njira zomwe zidatsatidwa: 6:5-6

2. Amuna anasankhidwa: 6:5

3. Kuzozedwa kwao: 6:6

D. Zotsatira za atumikwo: 6:7

1. Mawu anachulukitsidwa: 6:7

2. Ophunzira anachuluka: 6:7

3. Kumvera ku chikhulupiriro: 6:7

VIII. Wophedwa woyamba kamba ka chikhulupiriro: 6:8-8:1

Page 33: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

33

A. Mmene analili Stefano: 6:3-15

1. Mmodzi wa asanu ndi awiri: 6:3,5

2. Wozazidwa ndi Mzimu Woyera: 6:5

3. Munthu wa mbiri yabwino: 6:3

4. Munthu wa chikhulupirio: 6:5

5. Munthu wa nzeru: 6:3, 10

6. Munthu wa mphmvu: 6:8

7. Mboni yadalilika: 6:9-10

B. Chizunzo cha Stefano: 6:11-15

C. Uthenga wa Stefano: 7:1-53

1. Abrahamu: 7:1-8

2. Makolo a Mchipangano chakale: 7:9-16

3. Mose: 7:17-43

a. Ku Aigupto: 7:17-28

b. Muchipululu: 7:29-43

4. Chihema: 7:44-50

a. Cha Mose: 7:44

b. Cha Yoswa: 7:45

c. Cha Davide: 7:45-46

d. Cha Solomoni: 7:47-50

e. Cha Mulungu: 7:48-50

5. Aneneri: 7:51-53

D. Umboni wa Stefano: 7:54-8:1

1. Malingaliro a akuluakulu: 7:54

2. Chilengezo cha Stefano: 7:55-56

3. Zomwe akuluakulu anachita: 7:57-59

4. Imfa ya Stefano: 7:59-8:1

Gawo Lachitatu: Umboni wa ku Yudeya ndi ku Samariya

Machitidwe 8-12

I. Kusintha: Zotsatira za imfa ya Stephano: 8:1-4

A. Chizunzo: 8:1,3

B. Kuikidwa mmanda kwa Stefano: 8:2

C. Umboni wopitirira wa mpingo: 8:4

II. Umboni wa Filipo: 8:5-40

A. Utumiki wa ku Samariya: 8:5-25

Page 34: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

34

1. Umboni wa Filipo: 8:5-13

a. Ntchito ya Filipo: 8:5-7, 12

b. Zimene a Samaliya adachita: 8:6-12

c. Simoni wa nyanga: 8:9-13

2. Ntchito ya Petulo ndi Yohane: 8:14-17

a. Kubwera kwa Petulo ndi Yohane: 8:14

b. Kubwera kea Mzimu Woyera: 8:15-17

c. Zimene Simoni adachita: 8:18-19

d. Chenjezo la Simoni: 8:20-24

B. Utumiki wa ku Aitiyopiya: 8:26-40

1. Kukonzekera: 8:26-28

2. Umboni: 8:29-35

3. Zomwe adachita: 8:36-38

C. Kusintha kupita ku Azotu: 8:39-40

III. Umboni wa Saulo: 9:1-31

A. Kusanthulika mtima kwa Saulo: 9:1-9

1. Cholinga chake: 9:1-2

2. Masomphenya ake: 9:3-9

3. Mawu ake: 9:4-7

4. Kuchita khungu: 9:8-9

B. Kutumidwa kwa Saulo kudzera kwa Hananiya: 9:10-19

1. Maitanidwe: 9:10-16

2. Kutumidwa: 9:17-19

C. Ntchito ya Saulo: 9:20-31

1. Saulo ku Damasiko: 9:20-25

a. Umboni wake: 9:20-22

b. Zimene adachita: 9:21-23

c. Kuthawa kwake: 9:23-25

2. Saulo ku Yerusalemu: 9:26-30

a. Kulandiridwa kwake: 9:26-28

b. Ntchito yake: 9:28-29

c. Kuchoka kwake: 9:29-30

D. Kusintha: Mpukulo mu mpingo: 9:31

IV. Umboni wa Petulo: 9:32-12:35

Page 35: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

35

A. Ku Luda: 9:32-35

1. Okhulupirira: 9:32

2. Munthu wodwala: 9:33

3. Kuchiritsidwa kwa munthu wodwala: 9:34

4. Zomwe adachita: 9:35

B. Ku Yopa: 9:36-43

1. Imfa ya Dorika: 9:36-37

2. Kuitanidwa kwa Petulo: 9:38-39

3. Utumiki wa Petulo: 9:40-41

4. Zotsatira za utumiki: 9:42-43

C. Ku Kaisareya: 10:1-48

1. Masomphenya a Koneriyo: 10:1-8

a. Koneriyo: 10:1-2

b. Masomphenya a Koneriyo: 10:3-6

c. Zomwe adachita Koneriyo: 10:7-8

2. Masomphenya a Petulo: 10:9-22

a. Msomphenya: 10:9-12

b. Kulankhula: 10:13-16

3. Kufika kwa otumidwa: 10:17-22

4. Kufika kunyumba ya Koneriyo: 10:23-48

a. Ulendo: 10:23

b. Kulandiridwa: 10:24-27

c. Chilongosolo: 10:27-28

d. Funso: 10:29

e. Yankho: 10:30-33

f. Ulaliki osamalizitsa: 10:34-43

(1) Mulungu opanda tsankhu: 10:34-35

(2) Kufalikira kwa Uthenga wabwino: 10:36-37

(3) Uthenga wa uthenga wabwino: 10:38-43

g. Zimene Koneriyo adachita: 8:44-48

D. Ku Yerusalemu: 11:1-12:25

1. Vuto lobwera kamba ka kusandulika kwa a mitundu: 11:1-18

a. Vuto lake: 11:1-3

b. Kulongosola ntchito ya Mulungu pakati a mitundu: 11:4-17

(1) Masomphenya: 11:4-10

(2) Alendo: 11:11

(3) Ulendo: 11:12-16

c. Chisankho: 4:18

Page 36: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

36

V. Mpingo wa ku Antiokeya ku Asuri: 11:19-30

A. Chitsitsimutso cha ku Antiokeya: 11:19-21

B. Kufika kwa Banaba: 11:22-24

C. Saulo asankhidwa ngati mbusa wophunzitsa: 11:25-26

D. Zimene Agabo anaulula: 11:27-30

VI. Chizunzo cha Herode: 12:1-25

A. Kuphedwa kwa Yakobo: 12:1-2

B. Kumangidwa kwa Petulo: 12:3-4

C. Kumasulidwa kwa Petulo 12:5-19

D. Imfa ya Herode: 12:20-23

VII. Kulalikidwa kwa Mawu: 12:24-25

Gawo Lachinayi: Umboni ku dziko lonse lapansi

Machitidwe 13-28

I. Ulendo woyamba wochita utumiki: 13:1-14:28

A. Kuitanidwa ku utumiki: 13:1-3

B. Utumiki ku Pafo wa ku Ku: 13:4-12

C. Utumiki ku Antiokeya wa Mpisidiya: 13:13-50

1. Kupita ku Pisidiya: 13:13-16

2. Uthenga: 13:17-37

a. Chipulumutso cha mu Eksodo: 13:17

b. Ulendo wa mu Chipululu: 13:18

c. Kugonjetsa Kanani: 13:19

d. Ulamuliro wa Saulo ndi Davide: 13:20-23

e. Utumiki wa Yohane Mbatizi: 13:24-25

f. Kupachikidwa ndi kuuka Kwa Yesu: 13:26-37

g. Kuitanidwa: 13:38-41

3. Mmene adayankhira kuitanako: 13:42-50

D. Utumiki ku Ikoniyo: 13:51-14:5

E. Utumikiku Lustra: 14:6-25

F. Utumiki ku Antiokeya: 14:26-28

Page 37: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

37

II. Mkumano wa akuluakulu ku Yerusalemu: 15:1-35

A. Vuto lake: 15:1-3

B. Mkumano wa akuluakulu: 15:4-21

1. Mkumano woyamba: 15:4-5

2. Mkumano wa mseli wa atumwi ndi akuluakulu: 15:6

3. Mkumano wachiwiri: 15:7-21

a. Uthenga wa Petulo: 15:7-11

b. Uthenga wa Paulo ndi Banaba: 15:12

c. Uthenga wa Yakobo: 15:13-21

C. Chisankho: 15:19-21

D. Makalata: 15:22-35

III. Ulendo wachiwiri wa utumiki: 15:36-18:22

A. Kutsutsana: 15:36-41

B. Utumiki wa ku Lustra: 16:1-5

C. Utukiwa wa ku Trowa: 16:6-10

D. Utumiki wa ku Filipo: 16:11-40

E. Utumiki wa ku Tesalonika: 17:1-9

F. Utumiki wa ku Bereya: 17:10-14

G. Utumiki wa ku Atene: 17:15-34

H. Utumiki wa ku Korinto: 18:1-18

I. Utumiki wa ku Efeso: 18:19-21

J. Yerusalemu ndi Antioki: 18:22

IV. Ulendo wachitatu wa utumiki: 18:23-21:14

A. Ku Galatiya: 18:23

B. Utumiki wa ku Efeso: 18:24-19:41

1. Apolosi: 18:24-28

2. Ophunzira a Yohane: 19:1-7

3. Sukulu ya ku Turano: 19:8-12

4. Ana a Skeva: 19:13-17

5. Kupereke otembenuka: 19:18-20

6. Chisankho: 19:21

7. Otchinjiriza Demetriyo: 19:23-41

C. Utumuki wa ku Makedoniya ndi ku Helene: 20:1-5

Page 38: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

38

D. Utumiki wa ku trowa: 20:6-12

E. Utumiki wa ku Mitilene: 20:13-38

1. Ulendo: 20:13-16

2. Mkumano ndi akuluakulu a ku Efeso: 20:17-35

a. Kuunika utumiki wake: 20:17-21

b. Kuona za kutsogolo: 20:22-24

c. Chikumbumtima cha Paulo: 20:25-27

d. Chenjezo 20:28-31

e. Kuvomerezeka kwa Mulungu: 20:32

f. Chitsanzo cha Paulo mu mtsautso: 20:33-35

3. Kusanzikana: 20:36-38

F. Utumiki wa ku Turo: 21:1-6

G. Utumiki wa ku Ptolemayi: 21:7

H. Utumiki wa ku Kaesareya: 21:8-14

V. Ulendo wotsiriza wa ku Yerusalemu ndi kwa Aroma: 21:15-28:31

A. Yerusalemu: 21:15-23:32

1. Kusintha kupita ku Yerusalemu: 21:15-17

2. Mphekesera zosutsana ndi Paulo: 21:18-30

a. Kuti anaphwanya chilamulo cha Mose: 21:18-26

b. Kuti anadetsa malo oyera: 21:27-30

3. Zimene Paulo adachita: 21:23-26

4. Kupulumuka kwa Paulo: 21:30-32

5. Zimene Paulo adayankha: 21:33-23:10

a. Khamu la Chiyuda: 22:1-23

b. Kenturiyo wa Chiroma: 22:24-26

c. Kapitao wamkuru: 22:26-30

d. Bwalo la akuru: 23:1-10

(l) Chivomerezo cha Paulo: 23:1

(2) Kukumana ndi Mkulu wansembe: 23:2-5

(3) Kugawanika kwa bwalo: 23:6-10

6. Chivumbulutso kwa Paulo: 23:11

7. Chiwembu chofuna kupha Paulo: 23:12-15

8. Kupulumuka kwa Paulo: 23:16-32

a. Chiwembu chiululika: 23:16-22

b. Kalata: 23:25-30

c. Kuthawa: 23-32

Page 39: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

39

B. Ku Kaesareya: 23:33-26:32

1. Pa maso pa Felike: 23:33-24:27

a. Chitsutso cha Tertulo: 24:1-9

b. Yankho la Paulo: 24:10-21

c. Yankho la Felike: 24:22-27

2. Pamaso pa Festo: 25:1-12

3. Felike ndi Agripa: 25:13-27

4. Pamaso pa Agripa: 26:1-32

a. Paulo adzilankhulira yekha: 26:1-23

b. Kuitanira ku chipulumutso: 26:24-29

c. Chigamulo: 26:30-32

C. Ulendo wa kwa Aroma: 27:17-28:31

1. Mafunde: 27:1-44

2. Njoka: 28:1-6

3. Machiritso: 28:7-10

4. Ulendo upitilira: 28:11-15

D. Kwa Aroma: 28:16-31

l. Mkumano ndi Ayuda: 28:16-29

2. Utumiki: 28:30-31

Page 40: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

40

CHAPUTALA CHA 3

MAFANIZO A KUCHULUKITSA

ZOLINGA:

Pakutha pa chaputachi muyenera:

Kulemba Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

Kupereka tanthauzo la mawu oti “fanizo.

Kulongosola chifukwa chimene Yesu amagwiritsa ntchito mafanizo.

Kuzindikra mfundo za kuchulukitsa mu mafanizo amene Yesu amaphunzitsa.

VESI LOTSOGOLERA:

Ndipo ndi mafanizo otere ambiri analankhula nao mau, monga anakhoza kumva;

(Marko 4:33).

MAWU OYAMBA

Phunziroli likukhazikika pa mfundo za kuchulukana molingana ndi mmene Yesu anaphunzitsira

pa utumiki wake. Fanizo ndi nkhani imene imakamba zitsanzo zochokera ku dziko limene

timakhala pofuna kuonetsera choonadi ku uzimu.

Tanthauzo lenileni la mawu oti “fanizo” ndi “kuika pambali, kufanizira.” Mu mafanizo, Yesu

amafanizira zitsanzo za kudziko ndi choonzdi cha uzimu. Fanizo ndi nkhani yochitika kudziko

imene ili ndi tanthauzo ku uzimu.

CHIFUKWA CHIYANI MAFANIZO

Ophunzira ake nthawi ina anamufunsa Yesu chifukwa chimene amagwiritsa ntchito mafanizo

pofuna kuphunzitsa choonadi cha uzimu.

Ndipo ophunzirawo anadza, nati kwa Iye, Cifukwa canji muphiphiritsira iwo

m'mafanizo? (Mateyu 13:10).

Yesu anayankha:

Ndipo Iye anayankha nati, Cifukwa kwapatsidwa kwa inu kudziwa zinsinsi za

Ufumu wa Kumwamba, koma sikunapatsidwa kwa iwo (Mateyu 13:11).

Kumvetsetsa choonadi ku uzimu chimene chaphunzitsidwa mu fanizo zinapatsidwa kwa

ophunzira chifukwa anali ndi maganizo a uzimu. Amene analibe maganizo a uzimu mkumamva

mafanizo amalephera kumvetsetsa. Choonadi chauzimu chimveka ndi maganizo a uzimu:

Page 41: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

41

Koma munthu wa cibadwidwe ca umunthu salandira za Mzimu wa Mulungu:

pakuti aziyesa zopusa; ndipo sakhoza kuzizindikira, cifukwa ziyesedwa mwauzimu

(I Akorinto 2:14).

Munthu wa maganizo a uzimu ndi amene wabadwanso mwatsopano ku uzimu. Amene ali ndi

maganizo a uzimu amamvetsa mfundo zimene zimachokera mmafanizo. Amene ndi anthupi, a

maganizo a uchimo sangamvetse.

UTHENGA WABWINO WA UFUMU

Pamene Yesu anatuma akuphunzira ake kupita kudziko lonse kukalalikira uthenga wabwino,

Anati kwa iwo…

Ndipo uthenga uwu wabwino wa Ufumu udzalalikidwa pa dziko lonse

lapansi, ukhale mboni kwa anthu a mitundu yonse; ndipo pomwepo

cidzafika cimariziro (Mateyu 24:14).

Uthenga wabwino umene mukuyenera kufalitsa kudziko lapansi ndi uthenga wabwino wa

ufumu. Ndi uthenga umene ndi wa kubadwa, moyo ndi utumiki wa Yesu. Komanso ndi uthenga

wa imfa ya machimo a anthu onse ndi kuuka kwake kuchokera ku imfa. Mukuyenera kuuza

anthu za mmene anthu za mmene angalowere mu ufumu wa Mulungu kudzera mu kubadwanso

ku uzimu ndi kuwaphunzitsa mmene angakhalire moyo watsopano wa ufumu…….

MAFANIZO A KUCHULUKANA

Yesu anaphunzitsa mafanizo ambiri okhudza ufumu wa Mulungu. Ena mwa iwo anali mafanizo

a mmene ufumu ungafalikire ku dziko lonse lapansi. Mafanizo ali mmusiwa okhudza kukula kwa

Ufumu amaululu mfundo za kuchulukana. Onani ndi kuwerenga mafanizowa Mbaibulo lanu:

Nkhosa yosochera: Mateyu 18:12-14; Luka 15:4-7

Ndalama yotaika: Luka 15:8-10

Mwana olowerera: Luka 15:11-32

Mafanizowa amaululu chidwi cha Mulungu pa otaika ndi change chowafuna kuti abwerere mu

Ufumu wa Mulungu. Sizitengera chfukwa chimene anataikira. Nkhosa zinasochera kutali.

Ndalama inataika chifukwa cha kusasamala. Mwana anasochera chifukwa cha kugalukira kwake.

Mukuyenera kuchita mmene mungathere kuti mupeze otayika mu uchimo. Pitani kumene

amapezeka, osadikiraiwo kuti akupezeni. Mulungu sakhudzidwa ndi mmene anataikira, komatu

kuti apezeke basi.

Phwando lalikulu lopanda kanthu: Luka 14:15-23

Page 42: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

42

Kuchulukana kusathe chufukwa choti ena akana atatha kuyitamidwa ku uthenga wabwino.

Mukuyenera kuwafuna iwo amene ali ndi njala ya uzimu, ndi kwabweretsa ku phwando

lokonzedwa ndi Ambuye.

Mkuyu wosabala: Luka 13:6-9

Yesu anawauza fanizo la mkuyu wosabala. Mtengo wamkuyu ndi chizindikiro chooneka cha

mtundu Israyeli. Mulungu anakweza Israyeli ngati mtundu umene kudzera mwa iye adzaululu

Ufumu wa Mulungu ku dziko. Mulungu anayetsetsa kupeza “mtengo” wa Israyeli kuti ukabale

“zipatso” pakati pa mitundu yosadziwa Mulungu pakugawana nawo chidziwitso cha Mulungu

woona. Mulungu sakondwera ndi mitengo imene sibala zipatso.

Matalente: Mateyu 25:14-30; Luka 19:11-27

Munthu wa pa ulendo wautali: Marko 13:34-37

Akapolo: Mateyu 24:43-51; Luke 12:39-46

Akapolo oyang’anira: Luka 12:36-38

Woyang’anira wokhulupirika: Mateyu 25:14-30

Mafanizo a “akapolowa” amaika chidwi pa mdindo woyang’anira wamzeru pa uthenga wa

Ufumu umene waperekedwa kwa okhulupirira. Wokhulupirira aliyense papatsidwa “matalente”

kapena kuthekera kwapaderadera koti agwiritse ntchito polalikira uthenga wabwino. Kaya

kuthekera kwanu nkochepa kapena kwakukulu, mukuyenera kuchulukitsa zimene Mulungu

wakupatsani.

Kapolo aliyense akuyenera kuchuluka. Pamene Yesu adzabwerera ku dziko lapansi, iwo amene

agwiritsa ntchito mphatso zawo moyenera adzapatsidwa mphoto (Luka 16:10-12). Iwo amene

sakuchulukana amayesedwa osakhulupirika:

Pakuti Mwana wa munthu adzabwera mu ulemerero wa Atate wace, pamodzi ndi

angelo ace; ndipo pomwepo Iye adzabwezera kwa anthu onse monga macitidwe ao

(Mateyu 16:27).

Yesu amadziwa mfundo ya muyeso pa kuchulukana:

Koma iye amene sanacidziwa, ndipo anazicita zoyenera mikwapulo,

adzakwapulidwa pang'ono. Ndipo kwa munthu ali yense adampatsa zambiri, kwa

iye adzafuna zambiri; ndipo amene anamuikizira zambiri, adzamuuza abwezere

zoposa (Luka 12:48).

Page 43: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

43

Ufumu wa Mulungu umafalikira pakugwiritsa ntchito luso la uzimu lopatsidwa ndi Mulungu.

Ngati mugwiritsa ntchito zimene Mulungu wakupatsani, luso lanu lidzachuluka. Ndipo ngati

simuligwiritsa ntchito adzkulandani.

Wofetsa: Mateyu 13:3-8; Marko 4:3-8; Luka 8:5-8

Uthenga wa Ufumu umafalikira pofesa mbewu ya Mau a Mulungu. Sipangakhale kuchulukana

popanda Mau a Mulungu. Zipatso zimatengera moyo umene uli mu mbewu (amene ndiwo Mau a

Mulungu) ndi mmene nthaka ikuchitira (ndi mmene munthu achitira akamva Mau a Mulungu).

Pamakhalamachitidwe osiyana pamene mbewu ya Mau ikufetsedwa.

Udindo wanu ndi kungofetsa. Pamene mufetsa mbewu ya Mau a Mulungu, nthaka idzakonzeka

ndi kupereka zokolola. Nthaka ina imalephera kupereka zochuluka. Ngakhale Yesu anakumana

ndi nthaka yokanika pa nthawi ya utumiki wake.

Ndipo kumeneko sanakhoza Iye kucita zamphamvu konse, koma kuti anaika manja

ace pa anthu odwala owerengeka, nawaciritsa.

Ndipo anazizwa cifukwa ca kusakhulupirira kwao (Marko 6:5-6).

Nansongole ndi Tirigu: Mateyu 13:24-30

Pamene mukuchulukitsa Ufumu wa Mulungu pa kuonjezereka kwa okhulupirira atsopano,

Satana nayenso amayesera kugonjetsa ntchitoyo. Adzadzala anthu amene adzakhala ngati

Nansongole pakati pa mbewu zabwino za Ufumu wa Mulungu.

Anthu ena amene amavomereza kukhala okhulupirira ndi kuyamba kubwera mu mpingo mu njira

yochulukitsa, nthawi zina sakhala oona mtima. Amakhala nansongole odzalidwa ndi Satana.

Yesu safuna muwononge nthawi yanu kusiyanitsa pakati pa nansongole ndi tirigu. Pitilirani

kudzala mbewu ndi kuchulukana. Pa tsiku lokolola pamene Yesu adzabwera, nansongole

adzasiyanitsidwa kuchokera ku zokololazo.

Nkhoka yoponyedwa mnyanja: Mateyu 13:47-50.

Yesu anafanizira kukula kwa Ufumu wa Mulungu ndi nkhoka yaikulu imene iponyedwa

mnyanja. Nsomba zamitundu yonse zimalowamo, koma pamene nkhoka iponyedwa kumtunda

nsombazo zimasiyanitsidwa ndi zinthu zina zimene sizabwino.

Page 44: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

44

Ufumu udzakoka anthu a mitundu yonse. Ambiri adzalowamo. Ena adzakhala oona mtima ena

ayi. Pa tsiku lomaliza la chiweruzo pamene Mulungu adzakoka nkhoka, “nsomba” zabwino ndi

zoipa zizasiyanitsidwa. Inu simunaitanidwe kusiyanitsa koma kusodza.

Mbewu ya Mpiru: Mateyu 13:31-32; Marko 4:31-32; Luka 13:19

Ufumu wa Mulungu udzachuluka ngati mbewu ya mpiru. Mbewu ya mpiri ndi yaing’ono, koma

imakula mkukhala yokhwima. Ufumu wa Mulungu padziko umakhala ndi chiyamba

chaching’ono. Pamene Yesu anabwerera kumwamba atatha utumiki padziko, anasiya gulu la

anthu lochepa kulalikira uthenga wabwino. Okhulupirira ochepawa anachulukana kufikira zikwi

la omutsatira Iye ku mitundu yonse ya anthu.

Chotupitsa Mkate: Mateyu 13:33; Luka 13:21

Monga chotupitsa mkate mu choikiramo, Ufumu wa Mulungu udzachulukitsidwa kufikira dziko

lonse. Momwemonso chotupitsa, mphamvu ya Ufumu wa Mulungu siili kunja koma ili mkati.

Mpesa ndi Nthambi zake: Yohane 15:1-16

Fanizoli limafotokoza ubale wa pakati pa Yesu ndi kubala zipatso. Yesu ndi mpesa wa uzimu

ndipo ife ndizo nthambi. Simungabale chipatso mwa inu nokha. Mungathe kuchulukana ngati

mukhala mwa olumikizika ku moyo wa wochokera ku nthambi, ndiye Yesu. Yesu akufuna

kusanza moyo wanu pochotsa chilichonse chimene sichibala chipatso ndi cholinga chakuti inu

mukabale chipatso cha uzimu chokhalitsa.

Zokolola: Mateyu 9:37-38; Luka 10:2

Mu fanizo ili, munda ukuimira dziko. Zokolola ndi khamu la anthu amene akonzeka kulandira

uthenga wabwino. Zokolola zochuluka zikudikira kuti zikololedwe ndi ogwira ntchito a

Mulungu.

MFUNDO ZINA ZA KUCHULUKITSA

Yesu anaphunzitsa mfundo zina zochulukitsa mwachidule:

Kuunika kwa Dziko: Mateyu 5:14-16; Luka 8:16

Ufumu wa Mulungu udzachuluka ngati wokhulupirira akuoneka ngati kuwala kochokera ku

mzinda umene uli pamwamba kuonekera kutali. Tikyenera kubweretsa kuunika kwa dziko

(Yesu) ku dziko limene lili mu mdima wa uzimu. Ufumu udzachuluka pamene anthu abwera ku

kuwala.

Page 45: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

45

Mchere wa dziko: Luka 14:34

Mu nthawi ya Mbaibulo, mchere umathiridwa pa nyama kuti isaonongeke. Okhulupirira ali ngati

“mchere” wothiridwa pa dziko ndi uthenga wa kuteteza (chipulumutso). Ufumu udzachuluka

anthu apulumuke ku “chivundi” (imfa ya uzimu) ya tchimo.

Chuma cha kumwamba: Mateyu 6:19-21; Luka 12:15

Okhulupirira sakuyenera kukhala ndi chidwi ndi kudzichulukitsira chuma cha dziko lapansi.

Tayitanikwa ku chichulukitso cha uzimu. Pamene mukugawana uthenga wabwino,

mumachulukitsa chuma cha chanu cha uzimu kumwamba.

Chipata chotakata: Mateyu 7:13

Simungapereke chiweruzo choyenera poyang’ana chiwerengero. Njira yak u Gehena ili yotakata

ndipo ambiri amapita kumeneko koma njira yaku moyo wosatha amapitako ndi ochepa.

Ntchito Zambiri: Mateyu 7:22

Ambiri adzachita ntchito zodabwitsa. Moti padzakhala kukula ndi kuchuluka. Komatu kuchita

zodabwitsa zambiri sikofanana ndi kuchita chifuniro ndi kukwaniritsa cholinga cha Mulungu.

Zodabwitsa za Mulungu zikuyenera kuchitidwa ndi anthu Ake mu njira Yake.

Zochepa ndi Zambiri: Mateyu 10:42; Mateyu 14:15-21

Chilichonse chochitika mu dzina la Yesu, ngakhale choneka chochepa, ndi chofunikira.

Chozizwa cha mikate ndi nsomba chimaonetsera mmene Mulungu amachulukitsira ndi

kugwiritsa ntchito zochepa zimene tingapereke.

Kukula kumafuna Kusintha: Marko 2:21-22; 7:13

Kukula kwatsopano kumafuna kusintha. Simungasunge chatsopano mu chotengera cha

makhalidwe a zakale ndi a uchimo. Kuthekera kwa mphamvu ya Mau a Mulungu

kumalepheretsedwa ndi anthu amene amakakamira makhalidwe akale ndi kukana kusintha.

Kupeza pa Kutaya: Marko 8:34-37; 10:29-30

Kulandira pa Kupereka: Luka 6:38

Mfundo za dziko lapansi zimaphunzitsa kuti mumapeza pofuna zambiri. Yesu anaphunzitsa kuti

mumapeza chilichonse pamene mutaya chilichonse. Chimene chimaoneka chotayika mu dziko

mumachipeza mu dziko la uzimu.

Imfa imabweretsa Moyo: Yohane 12:24

Page 46: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

46

Kudzera mu imfa ya Yesu, ambiri analandira moyo. Pofuna kuchulukitsa, mbewu iyenera kufa.

Kudzera mu imfa moyo unabwera. Kuti mukhale ophunzira weniweni mukuyenera kufa ku

zokhumba za thupi. Mukuyenera “kufa” ku uchimo. Mukuyenera kukaniza njira zanu potsata

Yesu.

Mpingo wa pa thanthwe: Mateyu 16:18

Ufumu wa Mulungu unakhazikika pa thanthwe Yesu Khristu. Palibe kukula popanda Iye. Yesu

anati, “Ndizamanga mpingo wanga.” Ndipo anati palibe munthu amene abwera kwa Ite ngati

Atate samuitana (Yohane 6:44).

Chitsutso chimayenera kukhalako, koma “makomo a imfa” sangakhoze kugonjetsa cholinga cha

Mulungu pofuna kukulitsa Ufumu wake.

…Ici sicitheka ndi anthu, koma zinthu zonse zitheka ndi Mulungu (Mateyu 19:26).

…Zinthu zonse zitheka ndi iye wakukhulupirira (Marko 9:23).

MFUNDO YAIKULU YA KUCHULUKITSA

Mfundo yaikulu ya kuchulukitsa imene Yesu anaphunzitsa inaperekedwa Mmau Ake otsiriza

kwa ophunzira ake. Lamulo lake linaulula cholinga chake chachikulu polalikira uthenga

wabwino ndi kuchulukitsa atsopano ndi ophunzira:

Cifukwa cace mukani, phunzitsani anthu a mitundu yonse, ndi kuwabatiza iwo

m'dzina la Atate, ndi la Mwana, ndi la Mzimu Woyera:

ndi kuwaphunzitsa, asunge zinthu zonse zimene ndinakulamulirani inu; ndipo

onani, Ine ndiri pamodzi ndi inu masiku onse, kufikira cimariziro ca nthawi ya

pansi pano (Mateyu 28:19-20).

Ndipo ananena nao, mukani ku dziko lonse lapansi, lalikirani Uthenga Wabwino

kwa olengedwa onse (Marko 16:15).

Ndipo anati kwa iwo, Kotero kwalembedwa, kuti Kristu amve zowawa, nauke kwa

akufa tsiku lacitatu;

Ndi kuti kulalikidwe m'dzina lace kulapa ndi kukhululukidwa kwa macimo kwa

mitundu yonse, kuyambira ku Yerusalemu.

Inu ndinu mboni za izi (Luka 24:46-48).

Page 47: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

47

Komatu mudzalandira mphamvu, Mzimu Woyera atadza pa inu: ndipo

mudzakhala mboni zanga m'Yerusalemu, ndi m'Yudeya lonse, ndi m'Samariya, ndi

kufikira malekezero ace a dziko (Machitidwe 1:8).

CHIDULE

Ziphunzitso za Yesu zimaonetsera kuti Iye sakondwera ndi:

-Kusodza opanga kugwira.

-Phwando lopanda kanthu.

-Kufesa opanda kulolola.

-Mtengo wosabala zipatso.

-Nkhosa yotaika imene sibwerera mnkhola.

-Ndalama yotaika imene sinapezeke.

-Mwana wolowelera amene sanapezeke.

-Kapolo wosabala zipatso.

-Nthaka ya uzimu yosachita bwino.

-Zokolola zakupsa zimene sizinakololedwe

Atate athu amene safuna kuti ngakhale mmodzi atayike, amakondwera ndi zotsatira kudzera mu

kuchulukana kwa uzimu:

Comweco siciri cifuniro ca Atate wanu wa Kumwamba kuti mmodzi wa ang'ono

awa atayike (Mateyu 18:14).

Ambuye sazengereza nalo lonjezano, monga ena aciyesa cizengerezo; komatu aleza

mtima kwa inu, wosafuna kuti ena aonongeke, koma kuti onse afike kukulapa (II

Petro 3:9).

Page 48: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

48

MAYESO ODZIYETSA NOKHA

1. Lembani Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

2. Perekani tanthauzo la mawu oti “fanizo.”

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

3. Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu amaphunzitsa ophunzira ake mu mafanizo?

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

4. Pa pepala lapadera, longosolani mwachidule mfundo za kuchulukana mu fanizo lililonse

pansipa:

Phwando la pa gome lopanda kanthu:

Mtengo wamkuyu wosabala:

Nkhosa yosochera, ndalama ndi mwana:

Mafanizo a kapolo:

Wofesa:

Nansongole ndi Tirigu:

Nkhoka:

Mbewu ya mpiru:

Chotupisa mkate:

Mpesa ndi nthambi zake:

(Mayankho a mafunsowa akupezeka kumapeto kwenikweni kwa bukuli).

Page 49: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

49

KUPITILIZA KUPHUNZIRA

1. Kuyambira zaka 12 kufikira pamene Yesu amayamba utumiki, Baibulo silimapereka

tsatanetsatane wa zimene zinachitika mmoyo wake mu nthawi imeneyi. Ndi vesi limodzi

lokha limene limaulula za kukula kwa ku uzimu mu nthawi imeneyi.

Ndipo mwanayo anakula nalimbika, nalikudzala ndi nzeru; ndi cisomo ca Mulungu

cinali pa iye (Luka 2:40).

Kuti ukhale wamphamvu, kukula kwa ku uzimu kukuyenera kubwera poyamba utumiki

usanayambe.

2. Pamene nthawi imayandikira kumapeto, Satana adzagwiritsa ntchito mfundo zake

zochulukitsa. Werengani mavesiwa:

-Aneneri onyenga adzauka: Mateyu 24:11

-Anthu ambiri adzanyengedwa: Mateyu 24:11

-Uchimo udzachuluka: Mateyu 24:12

-Ambiri adzataya choonadi cha uthenga wabwino: II Atesalonika 2:3

-Mazunzo a okhulupirira adzachuluka: Mateyu 24:9-10

-Chodetsa ndi nkhani zopanda pake zidzachuluka: II Timoteo 2:16

Page 50: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

50

CHAPUTALA CHA 4

CHIMODZI KUPHATIKIZA CHIMODZI ZIMAKHALA ZOPITILIRA ZIWIRI

ZOLINGA:

Pakutha pa chaputalachi muyenera:

Kulemba Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

Kupereka tanthauzo la mawu oti “umboni.”

Kupereka tanthauzo la mawu oti “otumikira.”

Kupereka tanthauzo la mawu oti “mkulu wampingo”

Kulongosola tanthauzo la mawu oti “maitanidwe” a otumikira.

Kuolongosola dongosolo la Mulungu lochulukitsa pofalitsa uthenga wabwino.

Kutchula anthu awiri a Mchipangano Chatsopano ngati chitsanzo cha kuchulukitsa.

Kulongosola mmene mungachulukire ku uzimu.

Kuyamba kuchulukana ku uzimu.

VESI LOTSOGOLERA:

Ndipo zimene wazimva kwa ine mwa mboni zambiri, zomwezi uikize kwa anthu

okhulupirika, amene adzadziwa kuphunzitsa enanso (II Timoteo 2:2).

MAWU OYAMBA

Kukula kwa munthu kumayamba ndi selo imodzi ya moyo. Ndipo seloyo imayamba

kuchulukana kwambiri kufikira kuti munthu amapezeka kuti wapangidwa. Atatha kubadwa,

ntchitoyo imapitilira mwa mwana. Maselo a munthu amapitilira kuchulukana ndi kuyamba

kukula. Izi zili chomwechonso ndi ndi kudziko la uzimu. Munthu aliyense amene wakumana ndi

moyo watsopano mwa Yesu ali chomwechonso ndi selo ya munthu. Wokhulupirira aliyense

ayenera kubereka ku uzimu. Uthenga wabwino umalalikidwa pamene okhulupirira amachuluka

mu njira imeneyi.

Chaputala ichi chikuulula za udindo wanu ngati munthu ku moyo wanu wa uzimu. Muphunzira

dongosolo la Mulungula kuchulukana ku uzimu limene ndi “1 kuphatikiza 1 zimakhala zoposa

ziwiri.

Page 51: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

51

ZOLEPHERETSA

Vuto limene Yesu anali nawo kwa okhulupirira linali kufikira dziko lonse lapansi ndi uthenga

wabwino (Mateyu 28:19; Machitidwe 1:8). Lero tikukhala mu dziko limene likukula. Zikwi za

anthu akubadwa tsiku ndi tsiku. Chiwerengero cha dziko chikukula kwambiri.

Pali anthu ambiri amene sanafikilidwe ndi uthenga wabwino mdzikoli ndipo ambiri sanamvepo

za Yesu. Magulu a anthu amenewa ndi ankhaninkhani amene sanafikilidwe ndi uthenga

wabwino. Midzi komanso komanso madera ambiri alibe mipingo. Maiko ambiri kulibe azibusa

ambiri ophunzitsidwa ku mipingo imene ilipo.

Kodi tingapambane bwanji ndi vutoli pamene Yesu akuti tifikire dziko lonse ndi uthenga

wabwino?

DONGOSOLO LA MULUNGU

Mulungu ali ndi dongosolo lapaderadera lofuna kufikira dziko lapansi ndi uthenga wabwino.

Mwachidule, Yesu anawauza ophunzira ake kuti…

Komatu mudzalandira mphamvu, Mzimu Woyera atadza pa inu: ndipo

mudzakhala mboni zanga m'Yerusalemu, ndi m'Yudeya lonse, ndi m'Samariya, ndi

kufikira malekezero ace a dziko (Machitidwe 1:8).

Dongosolo la Mulungu ndi ili: Mzimu Woyera ndi mphamvu ya umulungu yopezeka kuseli kwa

kuchulukana, Yesu ndiye mwini nkhani wa uthenga, ndipo dziko lonse lidzakhala lolandira

uthenga wabwino.

Ophunzira ndi mnthumwi za kuchulukana. Njira za Mulungu kwa ophunzira ndi kuchitira

“umboni” wa uthenga wabwino. Choncho kuchitira “umboni” ndiko kunena zimene waona,

wamva, kapena kukumana nazo. Mu bwalo la milandu, mboni ndiye amene amavomereza za

chinthu kapena munthu. Monga mboni, mukuyenera kuchitira umboni za Yesu ndi cholinga

chake cha chipulumutso kwa anthu onse. Pali mitundu iwiri ya maumboni opezeka mbwalo la

milandu la malamulo. Umboni woyamba ndi wolankhula zokhuza nkhani. Umboni wina ndi

otsimikizira.

Mzimu Woyera amakuthandizani kuchitira umboni kaya wolankhula kudzera mu kuonetsera

mphamvu ya Mulungu.

KUGAWANA PAKATI PA AKULU A MPINGO NDI ATUMIKI

Dongosolo la Mulungu kwa okhulupirira aliyense ndi lochitira umboni wa uthenga wabwino.

Mpingo woyamba unakula pamene amatsatira dongosololi. Wokhulupirira aliyense amagawana

uthenga wabwino ndipo anali wochitachita ku uzimu. Makomo awo amakhala malo

ochulukaniranapo. Mpingo unakula ndi kuchulukana pamene okhulupirira amachitira umboni wa

uthenga wabwino.

Page 52: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

52

Pamene mpingo ukukula, Mulungu anaitana anthu ena kuti azitumikira nthawi yawo yonse

monga abusa, alaliki, aneneri, aphunzitsi ndi atumwi. Kwa nthawi yaitali, okhulupirira anakhala

gawo limodzi la magulu awiri mu mpingo. Amakhala akulu ampingo kapena atumiki wamba.

Atumikiwa amakhala gulu limodzi la anthu wosankhidwa ndi Mulungu. Tanthauzo lake ndi

lakuti anthu onse a Mulungu. Choncho atumiki amenewa amadziwidwa ngati anhtu amene

satumikira nthawi yawo yonse mu mpingo ayi.

Kenako pali akulu a mpingo amene anaphunzira bwino pa ntchito yawo ya utumiki mu mpingo.

Awa kwa iwo utumiki umakhala ngati ntchito yawo ya nthawi yonse ku mpingo. Akhoza

kusankhidwa kapena osasankhidwa ndi mpingo.

Kwa nthawi yaitali, mu mbiri ya mpingo, kusiyana pakati pa atumiki ndi atumiki wamba

kunayamba. Moti atumiki wamva ansiya kukhala ochulukana mu mpingo. Anayamba kusiyira

ntchito yofalitsa uthenga ku dziko kwa atumiki omwe anali ndi nthawi yonse yotumikira.

Palibe mtumiki wophunzira amene akhoza kukwaniritsa ntchito yonse yonse imene mpingo

unatumidwa kuti ukachite. Ichi ndi chifukwa chimodzi chimene sitinafikire dziko lapansi ndi

uthenga wabwino. Okhulupirira apereka udindo wawo kwa atumiki. Baibulo limaphunzitsa za

kugawana kwa ntchito mu mpingo, koma munthu wina aliyense akuyenera kukangalika kufalisa

uthenga wabwino. Onani Machitidwe 6:1-6.

Pamene mpingo wa ku Yerusalemu imachulukana, zinayamba kufunikira kuti agawane ntchito

kuti afikire zosowa zonse za mu mpingo. Atsogoleri anadzipereka okha ku Mau a Mulungu ndi

kupemphero. Atumiki wamba amagwira ntchito monga kutumikira amasiye ndi ntchito zina

zotumukira. Koma ngakhale okhulupirira amatumikira mosiyanasiyana mu mpingo, onse

anakangalika kufalisa uthenga wabwino.

Stefano anali mmodzi mwa atumiki wamba amene anasankhidwa kugwira ntchito ina, koma

anachitira umboni wamphamvu wauthenga wabwino. (Machitidwe 6:8-11). Filipo anali mtumiki

wambanso amene anasankhidwa kuti atumikire zinthu zina. Anagawana uthenga wabwino ndi a

Samariya (Machitidwe 8:5-12).

Pamene chizunzo chinabwera ku Yerusalemu ndipo okhulupirira mkubalalikana mmizinda

anapitilira kukhala mboni za uthenga wabwino.

Pamenepo ndipo iwo akubalalitsidwa anapitapita nalalikira mauwo (Machitidwe

8:4).

Kwa okhulupirira enieni sipakhala kugawana pakati pa opatulika ndi a kudziko chifukwa Yesu

ndi Ambuye wa onse.

Page 53: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

53

MAITANIDWE A ATUMIKI WAMBA

Ngati mukufuna mumvetsetse maitanidwe a uzimu a mtumiki wamba, mubwerere ku

Chipangano Chakale. Dongosolo la Mulungu linali kwa mtundu wonse wa Israyeli kuti ukhale

“ansembe” kapena “atumiki.”

Ndipo ndidzakuyesani ufumu wanga wa ansembe, ndi mtundu wopatulika (Eksodo

19:6)

Monga ansembe, munthu aliyense wa Israyeli anali mboni wa Mulungu woona kwa

osakhulupirira.

Kukhazikitsidwa kwa udindo wa unsembe sikunasinthe ndondomeko ya Mulungu pa Israyeli.

Unsembe unali ngati ntchito ya “utumiki” wa utsogoleri wa masiku a lero. Koma mtundu wonse

umatumikirabe ngati atumiki a uthenga wa Mulungu mitundu yosadziwa Mulungu.

Mu Chipangano Chatsopano, okhulupirira apatsidwa maitanidwe ofanana. Akutchedwa ansembe

kapena atumiki a uthenga wabwino:

Koma inu ndinu mbadwa yosankhika, ansembe acifumu, mtundu woyera mtima,

anthu a mw ni wace, kotero kuti mukalakire zoposazo za iye amene anakuitanani

muturuke mumdima, mulowe kuunika kwace kodabwitsa (II Petro 2:9).

Kuitanidwa kwa okhulupirira ndiko kuti akachitire umboni wa Mulungu amene anawatulutsa mu

mdima wa uzimu ndi kulowa mu “kuwala” kwa Yesu Khristu (Yohane 9:5).

Okhulupirira amaudzidwa kuti “ayende moyenera molingana ndi maitanidwe awo amene alimo”

(Aefeso 4:1). Pali maitanidwe amodzi ndiwo kuchitira umboni wa uthenga wabwino. Imeneyi

ndi ntchito ya okhulupirira onse. Munthu wina aliyense adzayankhapo pa za mmene anachitira

ku maitanidwe ake.

Maitanidwe amenewa samakhazikika chifukwa cha maphunziro kapena kuthekera kwa kudziko.

Mulungu amagwiritsa ntchito anthu wamba ndi cholinga chakuti Iye yekhayo alandire

ulemerero.

Pakuti penyani maitanidwe anu, abale, kuti saitanidwa ambiri anzeru, monga mwa thupi;

ambiri amphamvu, mfulu zambiri, iai;

Koma Mulungu anasankhula zopusa za dziko lapansi, kuti akacititse manyazi anzeru;

ndipo zofoka za dziko lapansi Mulungu anazisankhula, kuti akacititse manyazi

zamphamvu;

Ndipo zopanda pace za dziko lapansi, ndi zonyozeka, anazisankhula Mulungu, ndi zinthu

zoti kulibe; kuti akathere zinthu zoti ziriko; kuti thupi liri lonse lisadzitamande pamaso pa

Mulungu (I Akorinto 1:2-29).

Page 54: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

54

MACHITIDWE A KUCHULUKANA

Dongosolo la Mulungu la kuchulukana ndi lofanana ndi la kudziko la uzimu. Paulo anamuuza

Timoteo mawu awa mwachidule:

Ndipo zimene wazimva kwa ine mwa mboni zambiri, zomwezi uikize kwa anthu

okhulupirika, amene adzadziwa kuphunzitsa enanso (II Timoteo 2:2).

Paulo anamuuza Timoteo kuti asankhe anthu okhulupirika ndi kuwapereka ku zinthu zimene

anaphunzitsidwa ndi Paulo. Anthu okhulupirika amenewa akuyenera kukhala ndi kuthekera

kophunzitsa ena. Kupyolera mu dongosolo limeneli la kuchulukana, uthenga wabwino ungafikire

ku dziko lapansi.

Pofuna kuona mmene dongosolo la Mulungu la kuchulukana mmene limagwirira ntchito,

werengani tchati mmusimu. Tchatili likuonetsa nthawi ya pachaka imene munthu

angatembenuze munthu wina ndi kumuphunzitsa kukhala mkhristu wodalilika. Mu zoona zake

zikhoza kutenga nthawi kapena ayi potengera munthu amene achitayo. Choncho sizotheka

kukhazikika pa malire a nthawi. Koma ngati mkhristu akhoza kufikira munthu mmodzi ndi

kumuphuzitsa pa chaka ndipo nayenso aphunzitsa wina pa chaka, dziko likhoza kufikilidwa ndi

uthenga wabwino.

TIYAMBE BWANJI

Chipangano chatsopano chimaulula uthenga wabwino unafalikira mmadera oyandikana.

Kutanthauza kuti mukhoza kufalisa uthenga mosavuta pogwiritsa ntchito magulu a anzanu,

achibale, ndi ogwira nawo ntchito limodzi.

Mwachitsanzo, Yesu anaitani nsodzi mmodzi wotchedwa Andreya. Iyeyi anagawana uthenga ndi

mbale wake Petro. Ndipo anagawana ndi asodzi anzawo. Posakhalitsa gulu la anthu onse la

asodzi linamtsata Yesu.

Mmoyo wathu wa tsiku ndi tsiku atumiki osaitanidwa sikuti angokhala okongoletsa mpingo

kapena kumene amakhala ayi. Iwonso ndi akazembe a Ufumu kwa anzawo, achibale komanso

ogwira nawo ntchito limodzi. Kaya ndi kusukulu, kuntchito, kubanja, mmudzi, tikhoza

kuchitanso utumiki.

Luka 16:19-31 amakmba nkhani ya mwini chuma amene anapita ku Gehena. Munthuyi

anafunitsitsa atabwerera kuti akalalkire kwa a pabanja pake koma nthawi inamuthera.

Musadikire kufikira nthawi yofalisa uthenga ndi anzanu ikuthereni.

Page 55: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

55

MPHATSO ZA MZIMU NDI KUCHULUKANA

Umboni weniweni wa ubatizo wa Mzimu Woyera ndiko kukhala wamphamvu pochitira umboni

wa uthenga wabwino. Mphamvu ya Mzimu Woyera imapangitsa akhristu kuchulukana ku uzimu

(Machitidwe 1:8).

Njira imodzi imene Mzimu Woyera amapatsa mphamvu wokhulupirira ndi kudzera mu mphatso

za uzimu. Okhulupirira aliyense anapatsidwa mphatso za uzimu zomukuonzekeretsa kuchita

utumiki kwa ena. Mphatsozi ndi ndi kuthekera kwa uzimu kopatsidwa ndi Mzimu Woyera.

Ngati simudziwa mphatso za uzimu zimene Mulungu wakupatsani, funsani a Harvestime

International Institute akupatseni phunziro la “Utumiki wa Mzimu Woyera.” Phunziroli

limakamba za mphatso za uzimu.

KUKULA KWA UFUMU

Wokhulupirira aliyense akuyenera kukhala wochitachita. Koma kuchulukana chabe kwa

okhulupirira sikukwanira. Wokhulupirira ayenera kudzipereka pa mpingo umene ali ndi cholinga

chokhala pa umodzi woona ndi okhulupirra ena. Mpingi uyeneranso kuchulukana pawokha.

Mpingo uyenera kumakula mwa okha ku uzimu ndi kupitilira kukula, mmalire, ndi makulidwe

ena. Mwaonanso udindo wanu wochukitsa ngati munthu. Mu chaputala chikubwerachi,

muphunzira za mmene mungachulukire ngati gulu pakati pa mpingo.

Page 56: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

56

MAYESO ODZIYESA NOKHA

1. Lembani Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

2. Perekani tanthauzo la mawu oti “mboni.”

___________________________________________________________________________

3. Perekani tanthauzo la mawu oti “atumiki wamba.”

___________________________________________________________________________

4. Perekani tanthauzo la mawu oti “atumiki oitanidwa.”

___________________________________________________________________________

5. Fotokoza “maitanidwe” a atumiki wamba.”

___________________________________________________________________________

6. Kodi dongosolo la Mulungu la kuchulukitsa pa kulalikita uthenga wabwino ndi chani?

___________________________________________________________________________

7. Ndi anthu ati awiri mu Chipangano Chatsopano amene anali chitsanzo cha kuchulukana

ku uzimu?

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

8. Ndi njira iti yabwino yoyamba kuchulukana ku uzimu?

___________________________________________________________________________

(Mayankho a mafunsowa akupezeka kumapeto kwenkweni kwa bukuli).

Page 57: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

57

KUPITILIZA KUPHUNZIRA

1. Mu chaputala chimene chikuthachi ndi mwaphunzira za mafanizo a kuchulukana.

Onaninso mafanizo otsatirawa kawiri. Mu fanizo lililonse aliyense anali ndi udindo

wochulukana mokhulupirika.

-Matalente: Mateyu 25:14-30; Luka 19:11-27

-Munthu wa paulendo wautali: Marko 13:34-37

-Akapolo: Mateyu 24:43-52; Luka 12:39-46

-Akapolo woyang’anira: Luka 12:36-38

-Woyang’anira wokhulupirika: Mateyu 25:14-20

2. Werengani kukambirana kwa pakati pa Yesu ndi Petro mu buku la Yohane 21:15-22. Mu

Machitidwe 10:22 werengani mawu a Yesu amene analankhula kwa Paulo pa nthawi

imene amatembenuka mtima.

Chidwi chanu chisakhale poti kaya ena akukwaniritsa udindo wawo wolalikira uthenga

kapena ayi. Simukuyenera kufunsa ngati Petro, “Kodi munthuyu adzatani?” Chidwi

chanu chikhale ngati cha Paulo, “Kodi ndidzatani Ambuye?”

Page 58: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

58

CHAPUTALA CHA 5

MAWU OYAMBA A KUKULA KWA MPINGO

ZOLINGA:

Pakutha pa chaputalachi muyenera:

Kulemba Vesi Lotsogolera kuchokra pamtima.

Kudziwa mpingo weniweni.

Kulongosola mmene mpingo unayambira.

Kulemba zitsanzo za Mpingo mu Baibulo.

Kudziwa cholinga cha Mpingo Mbaibulo.

Kudziwa mitundu inayi ya kukula kwa Mpingo.

Kulemba chidule cha utumiki wa Mzimu Woyera pa kukula kwa Mpingo.

VESI LOTSOGOLREA:

Ndiponso Ine ndinena kwa iwe, kuti iwe ndiwe Petro, ndipo pa thanthwe ili

ndidzakhazika Mpingo wanga; ndipo makomo a dziko la akufa sadzaulaka uwo

(Mateyu 16:18).

MAWU OYAMBA

Mu chaputala chomaliza mwaphunzira za udindo wa wokhulupirira aliyense wochulukana ku

uzimu pofalisa uthenga wabwino. Mulungu ali ndi dongosolo lapaderadera mwa okhulupirira

amene angofika kwa Iye. Akuyenera kukhala gawo limodzi la chiyanjano cha okhulupirira

anzawo mu Mpingo. Okhulupirira ayenera kuberekana aliyense mumpingo, pakutero mpingo

umachulukana.

Chaputala ichi chikuonetsera dongosolo la Mulungu ku Mpingo ngati malo ochulukiranapo ku

uzimu. Machaputala anayi otsatira akufotokoza za mitundu ya kukula kwa mpingo.

MPINGO

Tikamakamba za “Mpingo” sitikamba za bungwe kapena mpingo opangidwa ndi anthu.

Mawu okuti “Mpingo” amatanthauza “oitanidwa.” Tikamakamba za Mpingo, timakamba za

chiyanjano cha dziko lapansi cha iwo amene ndi okhulupirira owona amene ayitanidwa kuchoka

ku dziko lapansi kulowa mu Ufumu wa Mulungu.

Page 59: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

59

Chifukwa cha cholinga cha utumiki, chiyanjano chimenechi cha dziko lapansi cha okhulupirira

chagawidwa mmangulu awo amene amasonkhana. Maguluwa amenewa amatchedwa Mpingo.

Ena mwa magulu amenewa amakhala oyima pawokha. Pamene ena amasonkhana ndi mabungwe

monga Assemblies of God, Baptist ndi Methodist komanso ena.

Munthu sumakhala gawo la Mpingo woona pokhala limodzi ndi bungwe koma pokhala

wobadwa mwatsopano ndi kulowa mu Ufumu wa Mulungu. Izi zimachitika zimachitka

povomereza ndi kulapa machimo ndi kulandira Yesu ngati Ambuye ndi mpulumutsi wa moyo

wanu. Mutatha kukhala wokhulupirira, dongosolo la Mulngu pa moyo wanu ndilo kukhala

mmodzi wa anthu wokhulupirra mu chiyanjano chimene ndi Mpingo.

MMENE MPINGO UMAYAMBIRA

Mu Chipangano Chakale mtunda wa ana a Israyeli unasankhidwa ngati gulu la anthu limene

kudzera mwa iwo Mulungu adzadziululu yekha kwamitundi una ya anthu. Kwa nthawi yaitali

Israyeli analephera udindowu.

Mu nthawi ya Chipangano Chatsopano pamene Yesu anabwera padziko lapansi, Israyeli

anamkana ngati Mesiya. Chifukwa cha ichi, Mulungu anadzutsa gulu lina la anthu limene

anasankha kudzionetsera ku dziko. Gulu limeneli likutchedwa Mpingo.

Kutchulidwa koyamba kwa “Mpingo” ndi pamene Yesu analongosola za mmene Mpingo

ungamangidwire.

Ndiponso Ine ndinena kwa iwe, kuti iwe ndiwe Petro, ndipo pa thanthwe ili

ndidzakhazika Mpingo wanga; ndipo makomo a dziko la akufa sadzaulaka uwo

(Mateyu 16:18).

Mu ndime imeneyi Yesu anaulula kuti Petro adzakhala mmodzi wa miyala ya maziko a uzimu a

Mpingo woyamba. Izi zikutanthauza kuti adzakhala ofunika mmakulidwe ndi maumbidwe ake.

Tanthauzo la Petro ndiye kuti “thanthwe kapena mwala.”

Yesu ananena yekha kuti kwa Iye yekha, “…pa thanthwe ILI ndidzamanga Mpingo wanga.”

Amaonetsera kuti Mpingo udzakhazikika pa Iye. Adzakhala thanthwe limene Mpingo

udzmangidwa. Padzakhala miyala ina yaing’ono (anthu ngati Petro). Koma zoona zake,

okhulupirira amatchedwa “miyala yamoyo” amene ali gawo limodzi la Mpingo:

Inunso ngati miyala yamoyo mumangidwa nyumba ya uzimu, kun mukhale

ansembe oyera mtima, akupereka nsembe zauzimu, zolandiridwa ndi Mulungu

mwa Yesu Kristu (I Petro 2:5).

Maziko a “miyala ya moyo” ndi “Thanthwe.” Thanthwelo ndiye Yesu ndipo limalongosola

malire a Mpingo. Mpingo sukhala mpingo woona pokhapokha wamangidwa pa Yesu Khristu.

Page 60: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

60

Kwa zaka zambiri Minpingo yambiri yosiyana papanga zolinga za mabungwe komanso

mautumiki. Ngati ali akhazikikadi pa maziko a Yesu, ndiye kuti ali gawo limodzi la chiyanjano

cha okhulupirira cha pa dziko lapansi:

Thupi limodzi ndi Mzimu mmodzi, monganso anakuitanani m'ciyembekezo cimodzi

ca maitanidwe anu;

Ambuye mmodzi, cikhulupiriro cimodzi, ubatizo umodzi.

Mulungu mmodzi ndi Atate wa onse amene ali pamwamba pa onse, ndi mwa onse,

ndi m'kati mwa zonse (Aefeso 4:4-6).

Yesu ananena kuti “makoma a imfa” sadzaulaka mpingo woona. Izi zikutanthauza kuti Mpingo

udzakumana ndi chitsutso chachikulu cha Satana, koma sudzagonjetsedwa.

Buku la Machitidwe limakamba za chitutso choyamba cha mpingo (Machitidwe 8). Kuyambira

mu mbiri kufikra pano, mpingo wakhala ukulandira chitsutso chachikulu, koma udzakhalabe

ndipo udzapitilira kukhalapobe. Udzakwaniritsa zolinga za Mulungu.

MMENE MPINGO UMAKHALIRA

Baibulo limagwiritsa zitsanzo zambiri polongosola mpingo. Zitsanzozi zimaululu zambiri

zokhuza maziko ndi cholinga cha mpingo. Onani zitsanzo za Mbaibulo zotsatirazi zokhudza

Mpingo:

Munthu watsopano: Aefeso 2:14-15

Thupi la Khristu: Aefeso 1:22-23; 5:30; I Akorinto 12:27

Kachisi kapena nyumba ya Mulungu: Aefeso 2:21-22; I Akorinto 3:9,16: I Timoteo 3:15; I Petro

2:5

Ansembe achifumu: I Petro 2:5,9; Chibvumbulutso1:6; 5:10

Mkwati wa Khristu: II Akorinto 11:2; Mateyu 25:6; Aefeso 5:22-32

Okhala mnyumba ya Mulungu: Aefeso 2:19

Nkhosa za Mulungu: Yohane 10:1-29; I Petro 5:3-4; Ahebri 13:20; Machitidwe 20:28

Pali mpingo umodzi koma Mbaibulo ukudziwika ndi magawo ambiri. Ukutchedwa:

Mpingo wa Mulungu: Machitidwe 20:28; I Akorinto1:2; 10:32; 11:22; 15:9; I Timoteo 3:5; I

Page 61: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

61

Atesalonika 2:14

Mpingo wa Mulungu wamoyo: I Timoteo 3:15

Mpingo wa Khristu: Aroma 16:16

Mpingo wa obadwa oyamba: Ahebri 12:23

Mpingo wa oyera mtima: I Akorinto 14:33

Anthu a Mulungu: Ahebri 4:9; I Petro 2:9-10

CHOLINGA CHA MPINGO MOLINGANA NDI MALEMBA

Pali zolinga zambiri za Mpingo molingana ndi mmene Baibulo limatiuzira:

MALAMBIRO A MULUNGU:

Cholinga chachikulu chimene muntu analengedwera ndicho kulambira Mulungu. Kulambira ndi

cholinga chachikulu cha Mpingo. Onani mavesiwa:

I Petro 2:5,9; I Akorinto 14:26-27; Yohane 4:23-24; Aefeso 2:19-22.

KUTUMIKIRA MU MPINGO:

Mamembala a mu Mpingo akuyenera kutumikirana zosowa za wina ndi mzake:

-Zikhoza kukhala zosowa za kuthupi: Machitidwe 11:27-30; 6:1-6.

-Mamembala ayenera kugawana mwa ufulu zinthuzawo: Machitidwe 2:44; 4:32, 34,37.

-Mamembala ayeneranso kusamalirana pa zosowa za ku uzimu mu thupi la Khristu: Yohane

15:1-7; Aroma 15:1-15; I Akorinto 3:9; Agalatiya 6:1; Akolose 2:16-23; I Atesalonika 2:7-16.

CHIYANJANO:

-Chiyanjano cha Mpingo chakhazikika pa umodzi wa mwa Khristu: Aefeso 4:4-6

-Mpingo umakhala umodzi mwa Khristu: Aefeso 2:11-18. Membala aliyense ndi wofanana

pamoso pa Ambuye: Aefeso 2:19-20.

Page 62: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

62

-Mpingo ukuyenera kukhala gulu la chiyanjano mmawu, mpemphero, ndi mu ntchito:

Machitidwe 2:41-47; 4:24,32-33; Aefeso 2:20-22; I Yohane.

-Chiyanjano chawo chikuyenera chikhale ndi cholinga chimodzi, maganizo amodzi, moyo

umodzi ndi mtima umodzi: Machitidwe 1:14; 2:46; 4:24,32; 5:12; 15:25

Chiyanjano sikuyenera chikhale kwa mpingo umodzi wokha ayi, komanso pakati pa mipingo ina.

Werengani mavesiwa amene akuonetsera ubale umenewu pakati pa mipingo:

-Amadziwa kuti ali amodzi mwa Khristu ndipo alumikizidwa pamodzi: Machitidwe 15:1; Aroma

15:26-27

-Amalankhulana pafupipafupi ndi wina: Aroma 16:16; I Akorinto 16:19-20; Afilipi 4:23

-Amathandizana wina ndi mzake: Aroma 15:26; I Akorinto 16:1-3.

-Anathandizira ntchito ya atumwi mmadera ena: Afilipi4:15-16

-Anagawana makalata a atumwi: Akolose 4:16.

-Amatumizirana nthumwi wina ndi mzake: Machitidwe 11:22,23,27; 15:1,2; I Akorinto16:3,4

-Amalimbikizana wina ndi mzake pa chikhulupiriro: II Akorinto 1:24; 9:2; I Atesalonika 1:7-10;

2:14

-Amalumikizana pa nkhani ya ulaliki: I Atesalonika 1:8

UTUMWI:

Mpingo cholinga chake ndiko kuchita utumwi osangoti kulambira komanso chiyanjano.

Cholinga cha ana a Israyeli mu Chipangano Chakale ndi Mpingo mu Chipangano Chatsopano

kunali kuulula Mulungu ku dziko lapansi.

Mu Chipangano Chakale, Israyeli anayenera kukhala mboni ku maiko osadziwa Mulungu.

Chimene Mulungu amafuna chinali choti maikowa afike poona Mulungu ndi mphamvu yake

kwa Israyeli. Mu Chipangano Chatsopano, cholingancha Mulungu chinali china. Chollinga

chake chinali kuti mpingo upite ku maiko ngati mboni. Utumwi weniweni wa mpingo ukupezeka

mu Aefeso:

Page 63: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

63

Kuti mu Eklesia azindikiritse tsopano kwa akulu ndi maulamuliro m'zakumwamba

nzeru ya mitundu mitundu ya Mulungu,

monga mwa citsimikizo mtima ca nthawi za nthawi, cimene anacita mwa Kristu

Yesu Ambuye wathu (Aefeso 3:10-11).

Anatizindikiritsa ife cinsinsi ca cifuniro cace, monga kunamkomera ndi monga

anatsimikiza mtima kale mwa iye,

kuti tikakonzedwe a makwaniridwe a nyengozo, akasonkhanitse pamodzi zonse

mwa Kristu, za kumwamba, ndi za padziko (Aefeso 1:9-10).

Chidule cha utumwi wa mpingo ndi ichi:

1. Mpingo ukuyenera kuonetsera Yesu ku dziko lapansi ngati Ambuye ndi Mpulumutsi.

Mpingo ukuyenera kutsogolera anthu ku ubale wabwino ndi Yesu kuti athe

kukhululukidwa machimo awo ndi kuyambanso moyo watsopano.

2. Kupyolera mu chiphunzitso ndi ulaliki wa ubatizo wa mmadzi, mpingo ukuyenera

kukhazikitsa okhulupirra mu chiphunzitso, mfundo ndi makhalidwe a chikhristu.

Akuyenera kuphunzitsa anthu ongotembenuka kumene kuti “asunge zinthu zonse”

zimene analamulilidwa mmawu a Mulungu.

3. Mpingo ukuyenera kupanga dongosolo la okhulupirra atsopano kukhala ofunikira mu

chiyanjano cha mpingo.

4. Mipingo yokhazikikayi ikuyenera kubwereza ndondomekoyi kuti akhale ndi okhulupirira

ambiri ndi chiyanjano chochuluka.

Phunzirani zambiri zokhuza utumwi wa mpingo mmavesi awa:

Kufalisa uthenga wabwino kudziko lapansi: Mateyu 5:13-14; 28:18-20; Marko 16:15-16;

Luka 24:45-49; Yohane 20:19-23; Machitidwe 1:8.

Kukhala mchere ndi kuunika kwa dziko lapansi: Mateyu 5:13-16; Afilipi 2:14-16: I Yohane 4:1.

Kuphunzitsa okhulupirita atsopano: Mateyu 28:19-20; Machitidwe 20:27-28; Aefeso 4:11-16; I

Petro 5:1-3.

Page 64: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

64

MITUNDU YA KUKULA KWA MPINGO

Ngati mpingo ukukwaniritsa cholinga chake cha mmalemba, mitundu inayi yampingo

imapezeka:

KUKULA KWA MKATI:

Kukula kwa mkati ndi kukula kwa uzimu kwa anthu a mumpingo.

KUKULA KOCHULUKA:

Uku ndi kukula kwa mpingo mu chiwerengero kumene kumachitika pamene ntchito yolalikira

uthenga yachitika ndi mpingo. Okhulupirira achilendo amapezeka mkukhala gawo limodzi la

thupi la Khristu.

KUKULA MMADERA:

Mpingo umakula mmadera pamene wayambitsa mpingo wina mudera lina la anthu achikhlaidwe

chofanana.

KUKULA KOLUMIKIZANA:

Uku ndi kukula kwa mpingo pamene wayamba kugawana uthenga kupitilira malire ndi anthu a

dera lina osiyana mtundu, chikhalidwe.

MZIMU WOYERA NDI KUKULA KWA MPINGO

Mzimu Woyera ndi mphamvu ya uzimu imene imapangitsa kukula kwa konse kwa mpingo kwa

mitundu inayi:

Komatu mudzalandira mphamvu, Mzimu Woyera atadza pa inu: ndipo

mudzakhala mboni zanga m'Yerusalemu, ndi m'Yudeya lonse, ndi m'Samariya, ndi

kufikira malekezero ace a dziko. (Machitidwe 1:8).

Vesi limeneli limatiuza za mmene Mzimu Woyera amapangira:

Kukula kwa mkati: ophunzira alandira mphamvu ya Mzimu Woyera. Izi ziwapangisa iwo kuti

akachitire umboni mwamphamvu.

Kukula kochuluka: Mpingo udzachuluka ku Yerusalemu.

Page 65: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

65

Kukula mmadera: mpingo udzadzala mipingo ina kumadera a zikhalidwe zofanana.

Kukula kolumikizana: Mpingo udzalumikizitsa kusiyana kwa zikhalidwe pofuna kufikira ena

monga Samariya ndi “malekezero a dziko lapansi.”

Baibulo limaphunzitsa kuti Mzimu Woyera ali ndi mautumiki ambiri. Anali wochitachita pa

kulengedwa kwa dziko, amauzira mawu Mulungu. Analinso wochitachita mu nthawi ya utumiki

wa Yesu pansi pano, ndipo anagwira ntchito zambiri mmaalo mwa okhulupirira.

Mzimu Woyera amaulula choonadi cha uthenga wabwino ndi kuwakokera anthu kwa Mulungu

kuti apulumuke. Mzimu Woyera alinso ndi utumiki wokhudza Satana. Amaberetsa mphamvy ya

uzimu imene imaika malire pa mphamvu ya Satana (Yesaya 49:19). Mautumiki ake onse

akupezeka mu maphunziro a Harvestime International Institute otchedwa “Utumiki wa Mzimu

Woyera.”

Mzimu Woyera alinso ndi utumiki wapaderadera wokhudza kukula ndi kuumba mpingo:

MZIMU WOYERA ANAUMBA MPINGO:

Pa tsiku la pentekosite pa Machitidwe 2:1-4 Mzimu Woyera anapanga Mpingo. Baibulo

limaphunzitsa kuti Mpingo malo opezeka Mulungu omangidwa ndi Mzimu Woyera.

Pamenepo ndipo simulinso alendo ndi ogonera, komatu muli a mudzi womwewo wa

oyera mtima ndi a banja la Mulungu

omangika pa maziko a atumwi ndi aneneri, pali Kristu Yesu mwini, mwala wa

pangondya;

mwa iye cimango conse, columikizika pamodzi bwino, cikula, cikhale kacisi

wopatulika mwa Ambuye;

cimene inunso mumangidwamo pamodzi, mukhale cokhalamo Mulungu mwa

Mzimu

(Aefeso 2:19).

MZIMU AMAKHUDZA MALAMBIRO

Kulambira kwa Mpingo kukuyenera kukhudzidwa ndi Mzimu Woyera:

Page 66: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

66

Koma ikudza nthawi, ndipo tsopano iripo, imene olambira oona adzalambira Atate

mumzimu ndi m'coonadi; pakuti Atate afuna otere akhale olambira ace.

Mulungu ndiye mzimu; ndipo omlambira iye ayenera kumlambira mumzimu ndi

m'coonadi (Yohane 4:23-24).

Pakuti ife ndife mdulidwe, akutumikira popembedza ndi Mzimu wa Mulungu,

nadzitamandira mwa Yesu Kristu, osakhulupirira m'thupi (Afilipi 3:3).

MZIMU WOYERA ANATSOGOLERA NTCHITO YA UTUMWI:

Izi zikuoneka mu ntchito ya utumwi ya mpingo woyamba:

Ndipo Mzimu anati kwa Filipo, Yandikira, nudziphatike ku gareta uyu (Machitidwe

8:29).

Ndipo anapita pa dziko la Frugiya ndi Galatiya, atawaletsa Mzimu Woyera kuti

asalalikire mau m'Asiya; pamene anafika kundunji kwa Musiya,

Anayesa kunka ku Bituniya; ndipo Mzimu wa Yesu sanawaloleza

Pamene anaona masomphenyawo, pomwepo tinayesa kuturukirakunka ku

Makedoniya, poganizira kuti Mulungu anaitanira ife kulalikira Uthenga Wabwino

kwa iwo (Machitidwe 16:6,7,10).

Ndipo pa kutumikira Ambuye iwowa, ndi kusala cakudya, Mzimu Woyera anati,

Mundipatulire Ine Bamaba ndi Saulo ku nchito imene odinawaitanirako

Pamenepo iwo, otumidwa ndi Mzimu Woyera, anatsikira ku Selukeya; ndipo

pocokerapo anapita m'ngalawa ku Kupro (Machitdwe 13:2,4).

MZIMU WOYERA ANASANKHA ATUMIKI:

Mipingo ina imasankha atumiki otumikira mu mpingo. Anthu ambiri amapita ku sukulu

za koleji kapena ku seminale kukaphunzitsidwa ngati atumiki. Koma choyenereza chimene

malemba amanena ndi chakuti atumiki ayenera kuitanidwa ndi kusankhidwa ndi Mzimu

Woyera:

Page 67: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

67

Tadzicenjerani nokha, ndi gulu lonse, pamenepo Mzimu Woyera anakuikani

oyang'anira, kuti muwete Eklesia wa Mulungu, umene anaugula ndi mwazi wa iye

yekha (Machitidwe 20:28).

MZIMU AMADZODZA ALALIKI:

Paulo analemba kale: Ndipo mau anga ndi kulalikira kwanga sanakhala ndi mau

okopa a nzeru, koma m'cionetso ca Mzimu ndi ca mphamvu (I Akorinto 2:4).

MZIMU WOYERA AMATSOGOLERA ZIGANIZO:

Machitdwe chaputala cha 15 amakamba za mkumano wa atsogoleri umene amakambirana

mavuto osiyanasiyana amene mpingo umakumana nawo. Chiganizo chawo chomaliza

amatsogolera ndi Mzimu Woyera:

Pakuti cinakomer a Mzimu Woyera ndi ife, kuti tisasenzetse inu cothodwetsa

cacikuru cina coposa izi zoyenerazi (Machitidwe 15:28).

MZIMU AMABATIZA MPINGO NDI MPHAMVU:

Buku la Machitidwe limayamba ndi nkhani yaikulu kwambiri:

Ubatizo umenewu unali wamphamvu pa kukula kwa mpingo mkati, chiwerengero, mmadera,

mmalire kumene kukupezeka mbuku la Machitidwe.

Ndipo pakufika tsiku la Penteskoste, anali onse pamodzi pa malo amodzi.

Ndipo mwadzidzidzi anamveka mau ocokera Kumwamba ngati mkokomo wa

mphepo yolimba, nadzaza nyumba yonse imene analikukhalamo.

Ndipo anaonekera kwa iwo malilime ogawanikana, onga amoto; ndipo unakhala pa

iwo onse wayekha wayekha.

Ndipo anadzazidwa onse ndi Mzimu Woyera, nayamba kulankhula ndi malilime

ena, monga Mzimu anawalankhulitsa (Machitidwe 2:1-4).

Page 68: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

68

MAYESO ODZIYETSA NOKHA

1. Lembani Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

2. Kodi Mpingo woona ndi wandani?

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

3. Kodi Mpingo unayamba bwanji?

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

4. Pali zitsanzo zambiri za Mbaibulo zimene zimakamba za Mpingo. Lembani zitsanzo

zitatu zokha.

___________________________ __________________________

____________________________________

5. Tchulani zolinga zinayi za Mpingo zimene mwaphunzira mu phunziroli.

________________ _________________ _____________________

______________________

6. Tchulani ndipo longosolani mwachidule mitundu inayi ya Mpingo.

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

7. Chaputalach chakambapo za zolinga 7 za Mzimu Woyera mogwirizana ndi kukula ndi

mapangidwe a Mpingo. Kodi mungatchule zingati?

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

(Mayankho a mafunsowa akupezeka kumapeto kwenikweni kwa bukuli)

Page 69: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

69

KUPITILIZA KUPHUNZIRA

1. Izi ndi zina mwa zotitsogolera zimene tingaziwire Mpingo woona. Ndi Mpingo

umene:

-umakhala wolondola mchiphunzitso. Ziphunzitso zonse zimakhazikika mu Mau

olembedwa ndi Mulungu.

-umakhala ndi mamembala obadwa mwatsopano: miyoyo ya mamembalayo imakhala

yosinthika ndi mphamvu ya Mulungu.

-wolambira: umalambira Mulungu mmodzi woonayo Atate, Mwana ndi Mzimu

Woyera.

-olalikira. Umakhala wochitachita mu utumwi ofikira dziko lapansi ndi uthenga

wabwino.

2. Izi ndi zina zotitsogolera kudziwa Mpingo wonama. Ndi Mpingo umene:

-umakhala wonama mchiphunzitso chake: Amasindika mawu ochepa okha ochokera

Mbaibulo ndi kuchotsako ena. Samatenga Mau a Mulungu mmene alili.

Amavomereza ziphunzitso za munthu zimene zimatsutsana ndi Mau a Mulungu.

-ogawikana: amakhala ndi magawano a mu Mpingo ndipo amalakalaka kuyambitsa

kuyambitsa mipatuko mu thupi la Khristu. Onani Aroma 16:17-18; Acts 20:29,30;

Aefeso 4.

-ulamuliro: mpingo wonama umayesera kulamulira miyoyo ndi ntchito za

mamembala mu njira yowalamulira.

-umakhala ndi mamembala osabadwanso: anthu amapitilira kukhala mmakhalidwe

akale a uchimo.

Page 70: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

70

CHAPUTALA CHA 6

KUKULA KWA MKATI

ZOLINGA:

Pakutha pa chaputalachi muyenera:

Kulemba Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

Kulongosola za kukula kwa “mkati” kwa Mpingo.

Kupereka tanthauzo la “kukula mu uzimu.”

Kuzindikira zizindikiro za kukula mu uzimu.

Kulongosola utumiki wa Mzimu Woyera mogwirizana ndi kukula kwa Mpingo.

Kuzindikira nyengo za kakulidwe mu dziko lapansi molingana ndi kudziko la ku uzimu.

VESI LOTSOGOLERA:

Pakuti kunamkomera Atate kuti mwa iye cidzalo conse cikhalire (Akolose 1:19).

MAWU OYAMBA

Mu chaputala chomaliza munaphunzira kuti pali mitundi inayi ya kukula kwa dongosolo la

Mulungu pa kuchuluka kwa Mpingo. Mpingo ukuyenera kuchulukana mkati, muchiwerengero,

mmadera komanso mmalire. Phunziro ili tikhala tikukamba za kukula mkati kwa Mpingo.

KUKULA KWA MKATI

Tikamakamba za “kukula mkati” kwa Mpingo, timakamba za kukula ndi kuumbika kwa

mamembala. Mpingo umakula mu uzimu molingana ndi kukula kwa munthu kwa yekha.

Mpingo sukungoyenera kukula kokha mu chiwerengero kudzera ku mmadera, kuchuluka kwa

anthu kapena mmalire, ukuyeneranso kukula mmachitidwe. Kukula mmachitidwe ndiye kuti ndi

kukula mkati ndi kukula ku uzimu. Paulo anakamba za izi pofanizira za kukula mkati mu thupi:

Pakuti kunamkomera Atate kuti mwa iye cidzalo conse cikhalire (Akolose 1:19).

Ndiye kuti “kuchuluka kwa Mulungu” ndiye kuti ndi kukula kwa kuuzimu. Pamene mamembala

akukula mu uzimu, mpingo umakumanandi kukula kwa mkati. Moti thupi lonse la Khristu

limakula ndi kuchuluka kwa chidziwitso cha Mulungu.

Page 71: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

71

Kukula kwa ku uzimu ndi kuchuluka kwa kukhwima ku uzimu kumene kumatsatira ku kuumba

moyo wa mkhristu wa okhulupirira. Ndi kukula kwa chidziwitso cha Yesu:

Koma kulani n'cisomo ndi cizindikiritso ca Ambure wathu ndi Mpulumutsi Yesu

Khristu (II Petro 3:18)

Uku ndi kukula mwa Khristu:

Koma ndi kucita zoona mwa cikondi tikakule m'zinthu zonse, kufikira iye amene ali

mutu ndiye Kristu (Aefeso 4:15)

Kukula mu uzimu kumatanthauza kuchepetsa umwini ndi kukulitsa moyo wa Khristu mwa iwe:

Iyeyo ayenera kukula koma ine ndicepe (Yohane 3:30)

Kukula mu uzimu sikumabwera nthawi imodzi chifukwa cha kukhala nthawi yaitali ya mkhristu.

Ndi zotsatira za kukula kwa moyo wa chikhristu mwa okhulupirira.

Zizindikiro za kukula mu uzimu ndi:

1. Kuchuluka kwa chidziwitso cha uzimu

2. Kugwirtsa ntchito bwino chidziwitsocho pa moyo ndi utumiki.

3. Kukhala ndi kuya kwa zinthu za uzimu.

4. Kukhala ndi chikondi chachikulu pa Mulungu ndi anthu ena.

5. Kuumbika kwa moyo wa chikhristu mmakhalidwe a uzimu (zipatso za uzimu).

6. Kukula kwa khumbo ndi kuthekera kugawana uthenga wabwino ndi anthu ena.

7. Kukula ndi kugwiritsa ntchito mphatso za uzimu.

Kukula ndi zotsatira za moyo. Ngati pali moyo wa uzimu mu mpingo, kukula kwa mkati

kuzabweretsa kukula mu chiwerengero, mmadera, ngakhale kukula mmalire.

MZIMU WOYERA NDI KUKULA KWA MKATI

Mu chaputala chathachi munaphunzira za utumiki wa Mzimu Woyera ku mpingo. Mzimu

Woyera:

-amapanga Mpingo.

-amatakasa Mpingo.

-amatsogolera ntchito ya umishoni.

-amasankha atumiki.

-amadzodza alaliki ache.

-amatsogolera ziganizo.

Page 72: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

72

-amabatiza ndi mphamvu.

Kuonjezera zku mautumuki mu mpingo, Mzimu Woyera ali ndi ntchito zina mogwirizana ndi

makulidwe a mkati a mpingo. Izi ndi monga:

KUTSUTSA UCHIMO:

Kukula mu uzimu kumatchingidwa ndi uchimo. Motero Mzimu Woyera amatsutsa tchimo kwa

okhulupirira:

Ndipo atadza Iyeyo, adzatsutsa dziko lapansi za macimo, ndi za cilungamo, ndi za

ciweruziro;

za macimo, cifukwa sakhulupirira Ine;

za cilungamo, cifukwa ndinka kwa Atate, ndipo simundionanso;

za ciweruziro, cifukwa mkuru wa dziko ili lapansi waweruzidwa (Yohane 16:8-11).

Pamene Mzimu Woyera akutsutsa za uchimo, pamenepo ndiye kuti tikhoza kutsatira lamulo…

Ngati tibvomereza macimo athu, ali wokhulupirika ndi wolungama iye, kuti

atikhululukire macimo athu, ndi kutisambitsa kuticotsera cosalungama ciri conse (I

Yohane 1:9).

KUKONZEDWANSO:

Uku kumatanthauza “kusinthika.” Mzimu Woyera amasintha moyo wa okhulupirira. Kusintha

uku kumabweretsa kukula kwa mkati:

Zosati zocokera m'nchito za m'cilungamo, zimene tidazicita ife, komatu monga mwa

cifundo cace anatipulumutsa ife, mwa kutsuka kwa kubadwanso ndi makonzedwe a

Mzimu Woyera (Tito 3:5).

CHIYERETSO:

Chiyeretso ndi “kupatulikira Mulungu.” Kupatulikaku kumabweretsa kukula ku uzimu:

Koma tiyenera ife tiziyamika Mulungu nthawi zonse cifukwa: ca inu, abale

okondedwa ndi Ambuye, kuti Mulungu anakusankhani inu kuyambira paciyambi,

Page 73: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

73

mulandire cipulumutso mwa ciyeretso ca Mzimu ndi cikhulupiriro ca coonadi (II

Atesalonika 2:13).

KUKHALA NAYE:

Mzimu Woyera amakhala mmoyo wa wa okhulupirira. Cholinga cha chimenechi ndi

kulimbikitsa chikhalidwe chatsopano chimene chinabwera chifukwa cha chipulumutso:

Kapena simudziwa kuti thupi lanu liri kacisi wa Mzimu Woyera, amene ali mwa

inu, amene muli naye kwa Mulungu? Ndipo simukhala a inu nokha (I A korinto

6:19).

Kodi simudziwa kuti muli Kacisi wa Mulungu, ndi kuti Mzimu wa Mulungu

agonera mwa inu? (I Akorinto 3:16).

Cifukwa cace ngati munthu ali yense ali mwa Kristu ali wolengedwa watsopano;

zinthu zakale zapita, taonani, zakhala zatsopano (II Akorinto 5:17).

Koma ndinena, Muyendeyende ndi Mzimu, ndipo musafitse cilakolako ca thupi.

Pakuti thupi lilakalaka potsutsana naye Mzimu, ndi Mzimu potsutsana nalo thupi;

pakuti izi sizilingana; kuti zimene muzifuna musazicite.

Ngati Mzimu akutsogolerani, simuli omvera lamulo (Agalatiya 5:16-18).

KULIMBIKITSA:

Kulimbitsa ndi kukula zimayendera limodzi. Umakhala wamphamvu pamene ukukula.

Zimatengera mphamvu kuti munthu ukule. Kukula kwa mkati kumabwera kudzera mu

kulimbikitsidwa kwa Mzimu Woyera:

Kuti monga mwa cuma ca ulemerero wace akulimbikitseni inu ndi mphamvu mwa

Mzimu wace, m'kati mwanu (Aefeso 3:16).

UMODZI:

Umodzi umabweretsa kukula mkati kwa Mpingo:

Koma iye wophatikidwa ndi Ambuye ali mzimu umodzi (I Akorinto 6:17).

Page 74: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

74

Pakuti monga thupi liri limodzi, nilikhala nazo ziwalo zambiri; koma ziwalo zonse

za thupilo, pokhala zambiri, ziri thupi limodzi; momwemonso Kristu.

Pakutinso mwa Mzimu mmodzi ife tonse tinabatizidwa kulowa m'thupi limodzi,

ngakhale Ayuda, ngakhale Ahelene, ngakhale akapolo, ngakhale mfulu; ndipo tonse

tinamwetsedwa Mzimu mmodzi (I Akorinto 12:12-13).

KUPEMBEDZERA:

Kupembedzera kwa Mzimu Woyera kumamanga moyo wa wokhulupirira ku uzimu:

Ndipo momwemonso Mzimu athandiza kufoka kwathu; pakuti cimene tizipempha

monga ciyenera, sitidziwa; koma Mzimu mwiniatipempherera ndi zobuula

zosatheka kuneneka (Aroma 8:36).

Koma inu, okondedwa, podzimangirira nokha pa cikhulupiriro canu coyeretsetsa,

ndi 4 kupemphera mu Mzimu Woyera (Yuda 20).

Mwa pemphero lonse ndi pembedzero mupemphere nthawi yonse mwa Mzimu,

ndipo poeezera pamenepo cicezerere ndi kupembedzera oyera mtima onse (Aefeso

6:18).

CHITSOGOZO:

Mzimu Woyera amatsogoza okhulupirira ku choonadi chonse cha Mau a Mulungu chimene

chimabweretsa kukula kwa mu uzimu:

Koma atadza Iyeyo, Mzimu wa coonadi, adzatsogolera inu m'coonadi conse; pakuti

sadzalankhula za iye mwini; koma zinthu ziri zonse adzazimva, adzazilankhula;

ndipo zinthu zirinkudza adzakulalikirani (Yohane 16:13).

Pakuti onse amene atsogozedwa ndi Mzimu wa Mulungu, amenewo ali ana a

Mulungu (Aroma 16:14).

MAVUMBULUTSO:

Mzimu Woyera amavumbulutsa choonadi cha Mau a Mulungu kwa okhulupirira chimene

chimabweretsa kukula mu uzimu:

Page 75: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

75

Koma kwa ife Mulungu anati onetsera izi mwa Mzimu; pakuti Mzimu asanthula

zonse, zakuya za Mulungu zomwe (I Akorinto 2:10).

CHIKONDI:

Anthu amakulu mu uzimu pamene akuonetsera chikondi:

Ndipo ciyembekezo sicicititsa manyazi; cifukwa cikondi ca Mulungu cinatsanulidwa

m'mitima mwathu mwa Mzimu Woyera, amene wapatsidwa kwa ife (Aroma 5:5).

KUFANANA:

Mzimu Woyera amakhala pa yotifanizira ife ndi Yesu mkati mwathu:

Koma ife tonse ndi nkhope yosaphimbika popenyerera monga mwa kalirole

ulemerero wa Ambuye, tisandulika m'cithunzihunzi comweci kucokera kuulenerero

kumka kuulemerero, monga ngati kucokera kwa Ambuye Mzimu (II Akorinto

3:18).

KUPHUNZITSA:

Timakula ku uzimu pamene tikukula mu chidziwitso cha Mulungu cha Mulungu. Mzimu

Woyera ndi mphunzitsi wathu.

Ndipo inu, kudzoza kumene munalandira kucokera kwa iye, kukhala mwa inu,

ndipo simusowa kuti wina akuphunzitseni; koma 9 monga kudzoza kwace

kukuphunzitsani za zinthu zonse, ndipo kuli koona, sikuli bodza ai, ndipo monga

kudaphunzitsa inu, mukhale mwa iye (I Yohane 2:27).

CHITSIMIKIZO:

Kukaika kumatchinga kukula kwa uzimu. Mzimu Woyera amachotsa kukaika paukutipatsa

chitsimikizo cha chipulumutso:

Mzimu yekha acita umboni pamodzi ndi mzimu wathu, kuti tiri ana a Mulungu

(Aroma 8:16).

Ndipo 6 munthu amene asunga malamulo ace akhala mwa iye, ndi iye mwa

munthuyo. Ndipo 7 m'menemo tizindikira kuti akhala mwa ife, kucokera mwa

Mzimu amene anatipatsa ife (I Yohane 3:24).

Page 76: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

76

UFULU:

Zotchinga zimaika malire pa kukula. Mzimu Woyera amapatsa ufulu pa uchimo ndi

zikhulupiriro za anthu:

Pakuti cilamulo ca mzimu wa moyo mwa Kristu Yesu candimasula ine ku lamulo la

ucimo ndi la imfa (Aroma 8:2)

Koma Ambuye ndiye Mzimuyo; ndipo pamene pali Mzimu wa Ambuye pali ufulu

(II Akorinto 3:17).

KUTONTHOZA:

Nkhawa ndi kufooketsedwa kumatchinga kukula kwa moyo wa uzimu. Mzimu Woyera

amapereka chitonthozo:

…ndipo unayenda m'kuopa kwa Ambuye ndi m'citonthozo ca Mzimu Woyera,

nucuruka (Machitidwe 9:31).

Ndiye Mzimu wa coonadi; amene dziko lapansi silingathe kumlandira, pakuti

silimuona iye, kapena kumzindikira iye. Inu mumzindikira iye; cifukwa akhala ndi

inu nadzakhala mwa inu…

Koma Nkhosweyo, Mzimu Woyera, amene Atate adzamtuma m'dzina langa, Iyeyo

adzaphunzitsa Inu zonse, nadzakumbutsa inu zinthu zonse zimene ndinanena kwa

inu (Yohane 14:17,26).

KUDZUTSA:

Umodzi mwa mautumiki a Mzimu Woyera mmoyo wa Yesu unali kudzutsa Iye kwa akufa.

Koma ngati Mzimu wa iye amene adaukitsa Yesu kwa akufa akhalabe mwa inu, iye

amene adaukitsa Kristu Yesu kwa akufa adzapatsanso moyo matupi anu akufa,

mwa Mzimu wace wakukhala mwa inu (Aroma 8:11).

Ngati simukukula ku moyo wanu wa uzimu, ndiye kuti mumakhala “wakufa” ku uzimu. Kukula

kumatha. Pakuti ndi mphamvu ya Mzimu Woyera imene imadzutsa inu moyo wanu wa uzimu.

KUONETSERA MPHAMVU:

Page 77: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

77

Paulo anati:

Ndipo mau anga ndi kulalikira kwanga sanakhala ndi mau okopa a nzeru, koma

m'cionetso ca Mzimu ndi ca mphamvu;

kuti cikhulupiriro canu cisakhale m'nzeru ya anthu, koma mu mphamvu ya

Mulungu (I Akorinto 2:4-5).

Chionetsero cha mphamvu ya Mzimu Woyera chimakulitsa chikhulupiriro chanu mwa Mulungu.

MPHAMVU YA KUCHITIRA UMBONI:

Mphamvu yapadera ya kuchitira umboni ndi chizindikiro kuti munthu wabatizidwa mwa Mzimu

Woyera:

Komatu mudzalandira mphamvu, Mzimu Woyera atadza pa inu: ndipo

mudzakhala mboni zanga m'Yerusalemu, ndi m'Yudeya lonse, ndi m'Samariya, ndi

kufikira malekezero ace a dziko (Machitdwe 1:8).

Akhristu okhwima mu uzimu adzachulukana pochitira umboni wa uthenga wabwino.

KUBATIZA:

Mpingo umakula mkati kudzera mu ubatizo wa Mzimu Woyera:

Ndipo anadzazidwa onse ndi Mzimu Woyera, nayamba kulankhula ndi malilime

ena, monga Mzimu anawalankhulitsa (Machitidwe 2:4).

Ubatizo wa Mzimu Woyera kukula kwa mphatso za Mzimu ndi zipatso mmoyo wa okhulupirira.

KUPEREKA MPHATSO ZA MZIMU:

Mphatso za mzimu ndi zofunikira pa kukula kwa Mpingo chifukwa “zimalimbikitsa”

wokhulupirira. Moti “kulimbikitsa” kumatanthauza “kumanga ndi kukweza kukula kwa moyo

wa uzimu.” (Muphunzira za mphatso za mzimu muphunziro likubwerali).

KUKWEZA CHIPATSO ZA UZIMU:

Chipatso cha Mzimu ndi chikhalidwe cha Mzimu choululidwa mmoyo wa okhulupirira.

Zimenezi zimatanthauza makhalidwe a uzimu amene ndi zizindikiro mu moyo wa okhulupirira.

Page 78: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

78

Chipatso cha Mzimu ndi chizindikiro cha kukula mu uzimu. Monga chipatso cha dziko lapansi,

ndi zotsatira za makhalidwe a uzimu amene ndi zotsatira za moyowu. Monga chipatso

chimatenga nthawi kuti chikule mu dziko lapansi, chipatso cha mzimu chimatenganso nthawi

kuti chikule. Zimenezi ndi zotsatira za kukula kwa mkati kwa moyo wa okhulupirira.

Izi ndi zipatso Mzimu Woyera:

Koma cipatso ca Mzimu ndico cikondi, cimwemwe, mtendere, kuleza mtima,

cifundo, kukoma mtima, icikhulupirtro, cifatso, ciletso; pokana zimenezi palibe

lamulo (Agalatiya 5:22-23).

Mulungu amafuna inu kuti mukule mu:

Chikondi: chikondi cholama, chisamaliro, ndi kukhuzidwa

Chimwemwe: chisangalalo, kukondwa, kunyadira zimane sizimadalira zochitikaza moyo.

Mtendere: bata, chiyanjano, kudekha, kupanda nkhawa ndi madandaulo, maudani.

Kuleza mtima: kudikira-kuthekera kopilira mu nyengo yowawa, chipliro.

Kufatsa: ulemu kwa anthu ena, kupanda nkhanza, kudekha.

Ubwino: machitidwe a chiyero ndi chilungamo.

Chikhulupiriro: maganizo okhala ndi kudalira pa Mulungu.

Kudekha: kukhala ndi kuthekera koletsa mphamvu.

Kukhazikika: maganizo abwino, ntchito zabwino, kudziletsa.

ZOPANGITSA KUKULA

Mu dzikoli lapansi pali zinthu zimene zimapangitsa kukula kwa zipatso. Zinthu za chilengedwe

zimenezi zimafanana ndi za uzimu zofunika kukula kwa moyo wobereka chipatso. Izi ndi zina

zimene zimafanana:

MOYO:

Kukula mkosatheka popanda moyo. Kukula kwa chpiatso kumayamba kuchokera ku mbewu.

Pamayenera kukhala moyo mu mbewu, kupanda kutero zingakule. Pakufanizira fanizo la ofesa,

“mbewu” ndiye mau a Mulung. Kukula kumabwera kudzera mbewu ya Mau a Mulungu.

Lirani monga makanda alero mkaka woyenera, wopanda cinyengo, kuti mukakule

nao kufikira cipulumutso (I Petro 2:2).

Yesu anali ndi chionetsero cha Mau a Mulungu, mbewu, ndipo mwa Iye munali moyo:

Mwa iye munali moyo; ndi moyowu unali kuunika kwa anthu (Yohane 1:4).

Page 79: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

79

Pakuti monga Atate ali ndi moyo mwa iye yekha, momwemonso anapatsa kwa

Mwana kukhala ndi moyo mwa iye yekha (Yohane 5:26).

Yesu anadza kudzafeso mbewu ya moyo yopangitsa moyo wauzimu kukula.

Siikudza mbala, koma kuti ikabe, ndi kupha, ndi kuononga, Ndadza Ine kuti akhale

ndi moyo, ndi kukhala nao wocuruka (Yohane 10:10).

NTHAKA YABWINO:

Mbewu ya Mau a Mulungu imayenera kukhalandi nthaka yabwino kuti ikule bwinobwino.

Werengani fanizo la wofesa mu Marko 4. Mbewu yokhayo imene yagwera panthaka yabwino

imabweretsa kukula kwa ku uzimu:

Ndipo iwo ofesedwa pa nthaka yabwino ndiwo oterewa akumva mau, nawalandira,

nabala zipatso zakupindula makumi atatu, ndi makumi asanu ndi limodzi, ndi

makumi khumi (Marko 4:20).

Mukuyenera kukonzekeretsa “nthaka” ya mtima wanu ndi maganizo anu kuti mulandire Mau a

Mulungu.

MADZI:

Madzi ndi wofunika pa kukula kwa zinthu mu dzikoli. Mulungu analonjeza:

Pakuti ndidzathira madzi pa dziko limene liribe madzi, ndi mitsinje pa nthaka

youma (Yesaya 44:3).

Kutsanulira kumeneku ndi kudzodza kwa Mzimu Woyera kwa madzi amene ndi chizindikiro:

Iye wokhulupirira Ine, monga cilembo cinati, Mitsinje ya madzi amoyo idzayenda,

kuturuka m'kati mwace (Yohane 7:38).

Madzi a Mzimu Woyera amapangitsa mbewu ya Mawu a Mulungu kuzika mizu mmitima ya

anthu amene ndi okufa mu uzimu:

Pakuti akaulikha mtengo pali ciyembekezo kuti udzaphukanso,

Ndi kuti nthambi yace yanthete siidzasowa.

Ngakhale muzu wace wakalamba m'nthaka, Ndi tsinde lace likufa pansi;

Page 80: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

80

Koma pa mnunkho wa madzi udzaphuka, Nudzaswa nthambi ngati womera (Yobu

14:7-9).

KUWALA:

Uku ndi kuyankha kuwala kumene kumapangisa kukula mu dziko lapansi. Kukula ku uzimu

kumayamba polandira kuwala kwa uzimu. Kuwalaku ndi Yesu.

Mwa iye munali moyo; ndi moyowu unali kuunika kwa anthu (Yohane 1:4).

Ine ndine kuunika kwa dziko lapansi; iye wonditsata ine sadzayenda mumdima,

koma adzakhala nako kuunika kwa moyo (Yohane 8:12).

MPWEYA:

Mpweya umabwera kuchokera ku chilengedwe cha zomera mulengalenga. Mpweya ndi

wofunika pa kukula. Mu Baibulo Mzimu Woyera amafanizidwa ngati mpweya kapena mphepo.

Mphepo iomba pomwe ifuna, ndipo ukumva mau ace, komavsudziwa, kumene

icokera, ndi kumene imuka; cotero ali yense wobadwa mwa Mzimu (Yohane 3:8).

Mzimu Woyera amapumuira mmoyo wa mbewu ya Mau a Mulungu. Kukula ku uzimu ndi

zipatso zimakhala zotsatira.

MPATA:

Mu fanizo la ofesa, kulimbirana mpata kumapangisa kuti mbewu zina zife:

Ndipo iye amene afesedwa kuminga, uyu ndiye wakumva mau; ndipo kulabadira

kwa dziko lapansi, ndi cinyengo ca cuma citsamwitsa mau, ndipo akhala wopanda

cipatso (Mateyu 13:22).

Mpikisano wa zinthu za dziko zimatsamwitsa mbewu ya Mau a Mulungu ndi kulepheretsa

kukula kwa uzimu.

MPUMULO:

Nthawi ya mpumulo (yotchedwa yongokhala) imakhala nyengo yapadera ya kubwerezeka kwa

zomera mu dziko lapansi. Imeneyi ndi nthawi ya mpumulo wa zomera ndi nyengo imene ndi

Page 81: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

81

yachisanu ya kukula kwambiri. Mu nthawi yongokhala, zomera zimaoneka ngati zafa. Koma

zimakhala zisanafe. Mbewu ya moyo imakhala ili mkati.

Nthawi zina munthu kapena mpingo umatha kuoneka ngati sukukula mu uzimu. Koma ngati

mbewu ya Mau a Mulungu yadzalidwa bwino, kukula kwa mkati kudzachitika (Masalmo 1).

Monga ngati mdziko, kungokhala mu uzimu kumabwera pambuyo pa kukula kwambiri ndi

kuumbika. Dikirani modekha pa kukula kwa mkati ndi kuchuluka ku zipatso za mzimu:

Taonani, wolima munda alindira cipatso cofunikatu ca dziko, ndi kuleza mtima

naco kufikira cikalandira mvula ya myundo ndi masika (Yakobo 5:7).

MIZU YAKE:

Mizu ndi yofunikira kulimbitsa ndi kupereka zofunika ku mtengo. Masalmo 1 amatuiza za

mmene mizu ilili mmoyo wa uzimu:

Wodala munthuyo wosayenda mu uphungu wa oipawosakhala pansi pa bwalo la

onyoza.

Komatu m'cilamulo ca Yehova muli cikondwerero cace;

Ndipo m'cilamulo cace amalingima usana ndi usiku.

Ndiye akunga mtengo wooka pa mitsinje ya madzi; Wakupatsa cipatso cace pa

nyengo yace,

Tsamba lace lomwe losafota; Ndipo zonse azicita apindula nazo (Masalmo1:1-3).

IMFA:

Nthawi yonse imene mudzala mbewu kti ibereke, zingakhale ndi moyo ngati siyamba yafa kaye:

Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Ngati mbeu ya tirigu siigwa m'nthaka, nifa, ikhala

pa yokha iyo; koma ngati ifa, ibala cipatso cambiri (Yohane 12:24).

Wopusa iwe, cimene ucifesa wekha sicikhalitsidwanso camoyo, ngati sicifa (I

Akorinto 15:36).

Moyo wa uzimu umadalira kufa kwa zinthu zina za dziko lapansi. Umafuna kufa ku tchimo,

zokhumba za dziko, ndi zosangalasa. Kufa ku za dziko kumasatira kukula kwa moyo wachipatso

wofanana ndi Khristu mmoyo wanu.

Page 82: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

82

KULUMIKIZIKA KU MPESA:

Kuti mubale chipatso mu dziko lapansi nthambi iyenera kulumikizika ku mtengo. Ngati nthambi

yadulidwa ku mtengo umene umapereka moyo ndiye kuti idzafa.

Yesu ndiye mpesa ndipo ife ndi nthambi. Choncho kuti ife tikabale chipatso cha uzimu tiyenera

kusungabe ubale wathu ndi Iye:

Ine ndine mpesa weniweni, ndipo Atate wanga ndiye wam'munda.

Nthambi iri yonse ya mwa Ine yosabala cipatso, aicotsa; ndi iri y'onse yakubala

cipatso, aisadza, kuti ikabale cipatso cocuruka.

Mwakhala okonzeka tsopano inu cifukwa ca mau amene ndalankhula ndi inu,

Khalani mwa Ine, ndi Ine mwa inu. Monga nthambi siingathe kubala cipatso pa

yokha, ngati siikhala mwampesa; motere mulibe inunso ngati simukhala mwa Ine.

Ine ndine mpesa, inu ndinu nthambi zace: wakukhala mwa Ine, ndi Ine mwa iye,

ameneyo abala cipatso cambiri; pakuti kopanda Ine simungathe kucita kanthu

(Yohane 15:1-5).

KUTSAZA:

Kutsaza ndi kofunikira mu dziko lapansi ngati tikufuna kuti zomera zikhale zoberekana zipatso.

Pamene mlimi atsanza mtengo amadula nthambi zosafunika ndi cholinga chopanga mtengowo

kuti ubale zipatso zambiri. Amachotsa chilichonse chimene chimatchinga makulidwe a mtengo.

Kutsanza ndi kofunikanso ku dziko la uzimu. Kutsanza ku uzimu ndi kukonzedwa ndi Mulungu.

Baibulo limatchula kuti chilango. Pamene Mulungu “atsanza” amachotsa chilichonse chimene

chilepheretsa kukula moyo wanu wa uzimu. Machitidwewa ndi ofunika ngati mufuna kuti

mubale chipatso:

Nthambi iri yonse ya mwa Ine yosabala cipatso, aicotsa; ndi iri y'onse yakubala

cipatso, aisadza, kuti ikabale cipatso cocuruka (Yohane 15:2).

Nthawi zina simukolola zotsatira za kutsanza chifukwa mumloza chala Satana pamene ali

Mulungu kubweretsa zinthu mmoyo wanu kuti akukonzeni (kutsanza). Cholinga cha kukonza

kwa Mulungu chikupezeka pa Hoseya 6:1:

Page 83: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

83

Tiyeni, tibwerere kunka kwa Yehova; pakuti wang'amba, nadzatipoletsera; wakantha,

nadzatimanga (Hoseya 6:1).

Chilango cha kutsanza chimatsatira kubwerera kwa Mulungu. Pokhapo pamene tabwerera kwa

Iye pamenepo mudzakhala ochitachita ku uzimu ndi kubala chipatso cha Mzimu Woyera.

NYENGO:

Nyengo ndi yofunika pa kukula kwa chipatso. Mu dziko lathuli zipatso za mitundu yambiri

zimakula mu nyengo imene imatetezedwa. Zimakula mnyumba zotchedwa “nyumba zotentha”

pamene pamakhala kutentha kwapadera. Zimatetezedwa ku nyengo imene ili pa dziko.

Mukatenga “nyumba yotentha” mkudzala ndi kuchotsa, mwamsanga chidzafa chifukwa chakhala

pa nyengo yotetezedwa. Sichingalimbe ndi nyengo imene ilipo mdziko. Kulankhula ku uzimu,

simufunika “nyumba yotentha” akhristu amene amaoneka abwino mu nyengo inayake koma

amafota akapezana ndi zenizeni za dziko.

Page 84: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

84

MAYESO ODIYETSA NOKHA

1. Lembani Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

__________________________________________________________________________

2. Kodi timatanthauza chani tikamakamba za kukula kwa mkati kwa Mpingo?

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

__________________________________________________________________________

3. Kodi kukula mu uzimu ndi chiyani?

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

4. Lembani zizindikiro 7 za kukula mu uzimu.

_____________________ ______________________ ________________

___________________________

_______________________ ______________________ ________________

5. Mwaphunzira njira zambiri za mmene Mzimu Woyera amakhudzira kukula mkati kwa

mpingo. Lembani zimene mungathe:

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

__________________________________________________________________________

6. Mwaphunziranso za nyengo za kakulidwe ka moyo wa uzimu zimene ndi zofanana ndi za

mdziko lapansi. Lembani zimene mungathe.

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

(Mayankho a mafunsowa akupezeka kumapeto kwenikweni kwa bukuli)

Page 85: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

85

KUPITILIZA KUPHUNZIRA

1. Pamene mtengo wayandikira kufa mu dzikoli, umayenera kuti utsitsimudwe.

Momwemonso Mpingo ukayandikira kufa, chitsitsimutso chimafunika. Kutsitsimula

ndiye kuti “kukhala ndi moyo kawiri.” Werengani mawuwa:

Kulirira chitsitsimutso: Masalmo 85:6 Dongosolo la Mulungu la chitsitsimutso: II

Mbiri 7:14

Werengani mavesiwa amene akukamba za chitsitsimutso mu chipangano chatsopano.

Kodi ndi zinthu ziti zimene zinabweretsa chitsitsimutso? Nanga zotsatira za

chitsitsimutso zinali chiyani?

Chitsitsimutso ku Sinai: Eksodo 32:1-35; 33:1:23

Chitsitsimutso mu nthawi ya Samueli: I Samueli 7:1-17

Chitsitsimutso pa phiri la Karimeli: I Mafumu18:1-46

Chitsitsimutso ku Ninevi: Buku la Yona

Chitsitsimutso mu nthawi ya Asa: II Mbiri 15

Chitsitsimutso mu nthawi ya Hezekiya: II Mbiri 29:1-36; 30:1-27; 31:1-21

Chitsitsimutso mu nthawi ya Yosiya: II Mbiri 34:1-33; 35:1-19

Chitsitsimutso utatha ukapolo: Nehemiya 8:1-18

2. Muchaputala chomalizachi mwaphunzira kuti mpingo umafanizidwa ndi nyumba ya

uzimu yomangidwa pa maziko a Yesu Khristu. Kukula kwa mkati kwa uzimu ndi njira

yomanga pa maziko amenewa. Werengani magawowa:

KUKULA PA KUMANGA

MFUNDO ZIKULUZIKULU:

A. Kodi mukumanga chiyani ku uzimu?

1. Inu ndiye mamangidwe:

Inunso ngati miyala yamoyo mumangidwa nyumba ya uzimu… (I Petro 2:5)

2. Inu ndi mamangidwe a muyaya:

Pakuti tidziwa kuti ngati nyumba ya pansi pano ya msasa wathu ipasuka, tiri

naco cimango ca kwa Mulungu, ndiyo nyumba yosamangidwa ndi manja,

yosatha, m'Mwamba (II Akorinto 5:1)

Page 86: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

86

3. Mpingo ndi mamangidwe:

…Omangika pa maziko a atumwi ndi aneneri, pali Kristu Yesu mwini, mwala

wa pangondya; mwa iye cimango conse, columikizika pamodzi bwino, cikula,

cikhale kacisi wopatulika mwa Ambuye; cimene inunso mumangidwamo

pamodzi, mukhale cokhalamo Mulungu mwa Mzimu (Aefeso 2:20-22)

B. Pali awiri amene akutenga nawo gawo:

1. Mulungu

…Koma wodzimanga zonse ndiye Mulungu. (Ahebri 3:4).

Akapanda kumanga nyumba Yehova, Akuimanga agwiritsa nchito cabe;

Akapanda kusunga mudzi Yehoya (Masalmo 127 :1)

…Ndipo pa thanthwe ili ndidzakhazika Mpingo wanga; ndipo makomo a dziko la

akufa sadzaulaka uwo (Mateyu 16:18)

2. Munthu: Munthu, mu ubale ndi Mulungu, akuyenera kumanga:

Pakuti ife ndife anchito anzace a Mulungu; cilimo ca Mulungu, cimango ca Mulungu

ndi inu (I Akorinto 3:9)

podzimangirira nokha pa cikhulupiriro canu coyeretsetsa (Yuda 20)

Ndipo iwo amene adzakhala a iwe adzamanga malo akale abwinja; udzautsa maziko a

mibadwo yambiri; udzachedwa Wokonza pogumuka, Wakubwezera njira

zakukhalamo (Yesaya 58:12)

MUSANAYAMBE KUMANGA:

Musanaymbe kumanga muyenera:

1. Muwerengere mtengo wake:

Pakuti ndani wa inu amene akafuna kumanga nsanja yaitali, sathanga wakhala

pansi, nawerengera mtengo wace, aone ngati ali nazo zakuimariza? 29Kuti

kungacitike, pamene atakhazika pansi miyala ya ku maziko ace, osakhoza

kuimariza, anthu onse akuyang'ana adzayamba kumseka iye, 30ndi kunena kuti,

Munthu uyu anayamba kumanga, koma sanathe kumariza (Luka 14:28-30)

Page 87: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

87

2. Khalani otsimikizika:

Ndipo a Solomo anati alimangire dzina la Yehova nyumba… (II Mbiri 2:1)

3. Khalani ndi malingaliro abwino:

Taonani, nditi ndilimangire dzina la Yehova Mulungu wanga nyumba,

kumpatulira iyo, ndi kufukiza pamaso pace zonunkhira za pfungo lokoma (II

Mbiri 2:4)

4. Kukonzeka:

Pakuti Ezara adaikiratu mtima wace kucifuna cilamulo ca Yehova, ndi kucicita,

ndi kuphunzitsa m'Israyeli malemba ndi maweruzo… (Ezara 7:10)

Ndipo 4 kapolo uyo, wodziwa cifuniro ca mbuye wace, ndipo sanakonza, ndi

kusacita zonga za cifuniro caceco, (Luka 12:47)

TIMANGE BWANJI:

1. Mangani pa maziko abwino:

Munthu wamzeru amamanga pa maziko a Mau a Mulungu…amene simagwa

chifukwa imakhala pa thanthwe (Mateyu 7:24-27)

Maziko abwino ndiye Yesu ndi Mau ake:

omangika pa maziko a atumwi ndi aneneri, pali Kristu Yesu mwini, mwala wa

pangondya (Aefeso 2:20)

Ozika mizu ndi omangirika mwa iye, ndi okhazikika m'cikhulupiriro, monga

munaphunzitsidwa, ndi kucurukitsa ciiyamiko (Akolose 2:7)

Musamalitse mmene mukumangirapa mazikowa:

Monga mwa cisomo ca Mulungu cidapatsidwa kwa ine, ngati mwini mamangidwe

waluso, ndinaika maziko, koma wina amangapo. Koma yense ayang'anire umo

amangira pamenepo. 11Pakuti palibe munthu akhoza kuika maziko ena, koma

amene aikidwako, ndiwo Yesu Kristu.

Page 88: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

88

Koma ngati wina amanga pa mazikowo, golidi, siliva, miyala va mtengo wace,

mtengo, maudzu, dziputu,

nchito ya yense idzaonetsedwa; pakuti tsikulo lidzaisonyeza, cifukwa kuti

yabvumbuluka m'moto; ndipo mota wokha udzayesera nchito ya yense ikhala

yotani (I Akorinto 3:10-13)

2. Mangani molingana ndi dongosolo:

Mamangidwe ena aliwonse a Mbaibulo, pamakhala dongosolo la Mulungu. Onani Genesis 6:

Eksodo 25:1 Mbiri 22. Anthu anamvera dongosolo la Mulungu:

Cotero anacita Nowa, monga mwa zonse anamlamulira iye Mulungu,

momwemo anacita (Genesis 6:22)

Dongosolo linali losiyana, koma chomwechonso zinali ndi Mose, Davide, Solomoni, Ezarandi

Nehemiya molingana ndi mmene Ambuye anawalamulira.

Conseci, anati Davide, anandidziwitsa ndi kucilemba kucokera kwa dzanja la

Yehova; ndizo nchito zonse za cifaniziro ici (I Mbiri 28:19)

Ngati simukusatira dongosolo la Mulungu la moyo wanu pa Mau a Mulungu, simudzapambana:

Pakuti sasamala nchito za Yehova, Kapena macitidwe a manja ace,

Adzawapasula, osawamanganso (Masalmo 28:5)

3. Mangani molingana ndi kuthekera kwanu:

Pa zokhudza mamangidwe mu nthawi ya Chipangano Chakale, anthu anapereka molingana ndi

kutherekera kwawo:

Monga momwe anakhoza anapereka ku Cuma… (Ezara 2:69)

4. Mangani mofuna:

Funani kukula mu uzimu:

Anapereka caufulu kwa nyumba ya Mulungu cakulimika pakuzika pace (Ezara

2:68).

Page 89: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

89

5. Mangani mu mphamvu za Ambuye:

…Motero ndinalimbika mtima, monga umo dzanja la Yehova Mulungu

wanga linakhala pa ine (Ezara 7:28)

6. Mangani mu Umodzi:

…Popeza mitima ya anthu inalunjika kunchito (Nehemiya 4:6)

7. Mangani Mwanzeru:

Nzeru imangitsa nyumba; Luntha liikhazikitsa (Miyambo 24:3)

Mkazi yense wanzeru amanga banja lace; Koma wopusa alipasula ndi manja ace

(Miyambo 14:1)

Nzeru yamanga nyumba yace, Yasema zoimiritsa zace zisanu ndi ziwiri (Miyambo

9:1)

Mulungu adzakupatsa luntha:

Ndipo ndamdzaza nd mzimu wa Mulungu, ndi luso, ndi nzeru, ndi cidziwitso, ndi

m'nchito ziri zonse (Eksodo 31:3,6)

Nampatsa mfumu Davide mwana waluso, wodziwa nzeru ndi waluntha, ammangire

Yehova nyumba, ndiponso nyumba ya ufumu wace (II Mbiri 2:12)

Mwini luntha ndi Mulungu:

Koma wina wa inu ikamsowa nzeru, apemphe kwa Mulungu, amene apatsa kwa

onse modzala manja, niwosatonza; ndipo adzampatsa iye (Yakobo 1:5)

Page 90: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

90

CHAPUTALA CHA 7

KUKULA MU CHIWERENGERO

ZOLINGA:

Pakutha pa chaputalachi muyenera:

Kulemba Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

Kulongosola tanthauzo la kukula mu chiwerengero.

Kulemba chidule cha kukula mu chiwerengero kwa mpingo woyamba wa ku

Yerusalemu.

Lembani chidule cha njira za kukula kwa mpingo mu chipangano chatsopano.

VESI LOTSOGOLERA

Ndipo mau a Mulungu anakula; ndipo ciwerengero ca akuphunzira cidacurukatu

ku Yerusalemu (Machitidwe 6:7)

MAWU OYAMBA

Mu thupi lathuli, ziwalo zambiri zalumikizika ndi mutu. Ntchito zonse za thupi zimabwera

chifukwa zimachokera ku mutu. Yesu ndi mutu amene amapereka chitsogozo cha thupi lake la

uzimu, ndiye mpingo. Yesu anati, “ndizamanga mpingo wanga” (Mateyu 16:18). Mu Baibulo,

njira zake zofuna kukwaniritsa cholinga chake zaululika.

Njira zochulukitsa mpingo zikuyenera kuti zikhazikike pa zimene zinaphunzitsidwa ndi

kuonetsedwa Mmau a Mulungu. Ngati ziwalo za thupi la Khristu, okhulupirira akuyenera

kuchitapo kanthu pa zitsogozo zimene zimachokera ku mutu, ndiye Ambuye Yesu. Chaputala

ichi ndi chimodzi mwa machaputala atatu amene amaika chidwi pa kukula kwa mamembala mu

mpingo. Phunziro ili likukamba zambiri za kukula mu chiwerengero.

KUKULA MU CHIWERENGERO

Kukula mu chiwerengero kumachitika pamene okhulupirira atembenuza munthu kupita kwa

Khristu ndikumutengera ki chiyanjano cha mpingo. Zotsatira za izi ndi kukula kwa mpingo mu

chiwerengero. Kukula mu chiwerengero kukuyenera kuloza ku kuchulukitsa Ufumu wa

Mulungu.

Ngati mpingo wachiwiri unaonjezeka ndi anthu 100 kuchokera ku mpingo wina pa ma thiransifa,

pamenepo kukula mu chiwerengero sikunachitike. Pakhala pali kuchuluka kwa mamembala ku

Page 91: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

91

mpingo wachiwiri koma chiwerengero mu ufumu sichinachitike. Kukula kwa ufumu

kumachitika pamene membala watsopano akutengedwera kwa Yesu ndi kuphunzitsidwa kukhala

membala odalilika mu thupi la Khristu.

ZIMENE CHIPANGANO CHATSOPANO CHIMANENA

Buku la Machitidwe limakamba za kukula kwa mpingo woyamba ku Yerusalemu mu

chiwerengero. Izi ndi chidule cha mmene zinakhalira:

KAKULIDWE KAKE:

Ndipo m'masiku awa anaimirira Petro pakati pa abale, nati (gulu la anthu

losonkhana pamalo pomwe ndilo ngati zana limodzi ndi makumi awiri)

(Machitidwe 1:15)

Mpingo unayamba mu chipinda cha pamwamba ndi gulu lochepa la ophunzira okwana 120. Pa

tsiku la Pentekosite, anthu okwanira 3,000 anaonjezereka ku mpingo:

Pamenepo iwo amene analandira mau ace anabatizidwa; ndipo anaonjezedwa tsiku

lomwelo anthu ngati zikwi zitatu (Machitidwe 2:41).

Itatha Pentekosite, kukula mu chiwerengero kumachitika tsiku ndi tsiku:

Chiwerengero cha anthu ku Yerusalemu chinakwera mkufika 5,000. Chiwerengerochi panalibe

akazi ndi ana amene analinso gawo limodzi la mpingo:

Koma ambiri a iwo amene adamva mau anakhulupira; ndipo ciwerengero ca

amuna cinali ngati zikwi zisanu (Machitidwe 4:4)

Kumapeto kwake, khamu la athu linaonjezereka:

Ndipo makamaka anaonjezedwa kwa Ambuye okhulupirira ambiri, ndiwo amuna

ndi akazi (Machitidwe 5:14)

Ngakhale iwo amene amatsutsa mpingo anazizwa ndi kukulaku:

Koma m'mene anamva mau awa mdindo wa Kacisi ndi ansembe akulu anathedwa

nzeru ndi iwo aja, kuti ici cidzatani (Machitidwe 5:24)

Page 92: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

92

Mawu oti anaonjezeredwa anagwiritsidwa ntchito polongosola kukula ku chiwerengero cha

mpingo. Mwamsanga kukula kuja kunakhala kwakukulu moti mawu oti kukuchuka anagwira

ntchito.

Ndipo mau a Mulungu anakula; ndipo ciwerengero ca akuphunzira cidacurukatu

ku Yerusalemu (Machitidwe 6:7)

Kuchokera pa nthawi imeneyi, buku la Machitidwe limatsindika za kuchuluka kwa mipingo

komanso mamembala a mpingo wa ku Yerusalemu. Mipingo yatsopano inadzalidwa mmalo onse

a anthu a mitundu amene ndi odziwika mdziko osachepera za 40. Mwachitsanzo, ku Samariya…

Koma pamene anakhulupirira Filipo wakulalikira Uthenga Wabwinowa Ufumu wa

Mulungu ndi dzina la Yesu Kristu, anabatizidwa, amuna ndi akazi (Machitidwe

8:12)

Mipingo yaku Yudeya, Galileya, Ludda, Sarona ndi Yopa inakula mu chiwerengero cha anthu:

Pamenepo ndipo Mpingo wa m'Yudeya Ionse ndi Galileya ndi Samariya unali nao

mtendere, nukhazikika; ndipo unayenda m'kuopa kwa Ambuye ndi m'citonthozo ca

Mzimu Woyera, nucuruka (Machitidwe 9:31)

Ndipo anamuona iye onse akukhala ku Luda ndi ku Sarona, natembenukira kwa

Ambuye amenewa (Machitidwe 9:35,42)

Anthu “ambiri anaonjezereka” ku mpingo kudzera mu utumiki wa Myuda mmodzi

wotembenuka:

Cifukwa anali munthu wabwino, ndi wodzala ndi Mzimu Woyera ndi cikhulupiriro:

ndipo khamu lalikuru lidaonjezeka kwa Ambuye (Machitidwe 11:24)

Mavesi atatu akukamba za chiwerenero chachikulu chimene chinaonjezereka ku Antioki:

Ndipo dzanja la Ambuye linali nao; ndi unyinji wakukhulupira unatembenukira

kwa Ambuye.

ndipo m'mene anampeza, anadza naye ku Antiokeya. Ndipo kunali, kuti caka conse

anasonkhana pamodzi mu Mpingo, naphunzitsa anthu aunyinji; ndipo ophunzira

anayamba kuchedwa Akristu ku Antiokeya (Machitidwe 11:21, 24,26).

Pamene Mau a Ambuye amapitilira kulalikidwa ndi kuchuluka, okhulupirira atsopano

amaonjezereka ku mpingo:

Page 93: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

93

Koma mau a Mulungu anakula, nacurukitsa (Machitidwe 12:24)

KUCHULUKA KUPITILIRA:

Ndime zotsatirazi ndi chidule chabe cha kukula kwa mpingo kumadera ena:

Ndipo mau a Ambuye anabukitsidwa m'dziko lonse. Koma Ayuda anakakamiza

akazi opembedza ndi omveka, ndi akulu a mudziwo (Machitidwe 13:49-50)

Cotero mau a Ambuye anacuruka mwamphamvu nalakika (Machitidwe 19:20)

KUKULA KU IKONIYO

Ndipo kunali pa Ikoniyo kuti analowa pamodzi m'sunagoge wa Ayuda, nalankhula

kotero, kuti khamu lalikuru la Ayuda ndi Ahelene anakhulupira (Machitidwe 14:1)

KUKULA KU DEBE

Ku Debe, ophunzira anatsimikizidwa, kulimbikitsidwa ndi kukhala pamodzi ndi Paulo (Onani

Machitidwe 14:20-21)

KUKULA KU AGALATIYA:

Kotero Mipingoyo inalimbikitsidwa m'cikhulupiriro, nacuruka m'ciwerengo cao

tsiku ndi tsiku (Machitidwe 16:5)

KUKULA KU FILIPO:

Ndipo anatimva mkazi wina dzina lace Lidiya, wakugulitsa cibakuwa, wa ku mudzi

wa Tiyatira, amene anapembedza Mulungu; mtima wace Ambuye anatsegula, kuti

amvere zimene anazinena Paulo (Machitidwe 16:14)

KUKULA KU ATESALONIKA:

Ndipo ena a iwo anakopedwa, nadziphatika kwa Paulo ndi Sila; ndi Ahelene

akupembedza aunyinji ndithu, ndi akazi akuru osati owerengeka (Machitidwe 17:4)

Page 94: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

94

KUKULA KU BEREYA:

Ndipo ambiri a iwo anakhulupira; ndi akazi a Cihelene omveka, ndi amuna, osati

owerengeka (Machitidwe 17:12)

KUKULA KU AKORINTO:

Ambuye anati “Ndili ndi anthu ambiri mu mzindawu” (Onani Machitidwe 18:8-11). Buku la

Machitidwe limatha ndi Paulo akadali kukulitsabe mpingo, ngakhale anali wa mndende kwa

Aroma:

Ndipo anakhala zaka ziwiri zamphumphu m'nyumba yace yobwereka, nalandira

onse akufika kwa iye,

ndi kulalikira Ufumu wa Mulungu, ndi kuphunzitsa za Ambuye Yesu Kristu ndi

kulimbika konse, wosamletsa munthu (Machitidwe 28:30-31)

Paulo nalemba kuti zikwi za Ayuda ambiri anabwera kwa Yesu nakhala gawo la

mipingo:

Ndipo pamene anazimva, analemekeza Mulungu; nati kwa iye, Uona, mbale, kuti

ambirimbiri mwa Ayuda akhulupira; ndipo ali naco cangu onsewa, ca pa cilamulo

(Machitidwe 21:20)

MMENE MPINGO UMAKULIRA

Pali njira zambiri zimene mpingo oyamba unakulira:

MASOMPHENYA A UZIMU:

Popanda masomphenya anthu amatayika. (Miyambo 29:18)

Popanda masomphenya a uzimu, anthu amafa ku uzimu. Mpingo woyamba unali ndi

masomphenya a uzimu. Anali masomphenya amene Yesu anapereka kwa ophunzira ake pamene

anawauza kuti….

Onani ndinena kwa inu, Kwezani maso anu, nimuyang'ane m'minda, kuti mwayera

kale kufikira kumweta (Yohane 4:35)

Page 95: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

95

Masomphenya a uzimu amalumikiza anthu pa cholinga. Masomphenya amatsogolera anthu

kuchitukuko cha machitidwe. Machitidwe monga kumvetsa cholinga, ndi kuwaniritsa

cholingacho komanso njira za kauniuni poonetsetsa kuti cholinga chikukwaniritsidwa.

Masomphenya amatsogolera kukhudzikwa. Pamene Yesu anaona khamu la anthu anakhudzika.

Chinali chikatundu cholemera molingana ndi chidziwitso cha chosowa chawo. Masomphenya

ndi kutukula kwa maonedwe a zinthu molingana ndi Baibulo, kumaliwona dziko molingana ndi

mmene Mulungu amalionera ndi kuvomereza pa zimenezo.

Mpingo woyamba unatenga masomphenya ochulukitsa mpingo kuchokera ku Yerusalemu kupita

ku Yudeya, Samariya ndi malekedzero onse a dziko lapansi. Anali masomphenya ophunzitsidwa

ndi atsogolera awo (Machitidwe 1:8). Pamene anthu ali ndi masomphenya a uzimu

chiyembekezo chimachotsa ulesi ndi umodzi wawo umachotsa mpikisano.

MALO NDI NTHAWI ZOLANDILIKA:

Yesu anaphunzitsa kuti malo ena adzalandilidwa kuposa ena:

Awa amene, khumi ndi awiriwa, Yesu anawatumiza, nawalangiza ndi kuti,

Musapite ku njira ya kwa anthu akunja, ndi m'mudzi wa Asamariya

musamalowamo:

koma makamaka mupite ku nkhosa zosokera za banja la Israyeli

Ndipo yemwe sadzakulandirani inu, kapena kusamva mau anu, pamene

mulikuturuka m'nyumbayo, kapena m'mudzimo, sansani pfumbi m'mapazi anu

(Mateyu 10:5-6,14)

Madera ena komanso magulu ena amalandira uthenga mu nthawi zina kuposa ena. Mpingo

woyamba unagwira ntchito pa zokolola za uzimu zimene zimalandira uthengawo. Pamene Paulo

anakanidwa ku Sunagoge, anaphunzitsa kwina (Machitidwe 9:20-31). Pamene amafuna kupita

ku M’ Asiya mu nthawi yoyamba, Mzimu Woyera anamuletsa (Machitidwe 16:6). Anadzapita

nthawi ina imene analandira uthenga.

Kukula ku chiwerengero kumachitika pamene taika chidwi pa zokolola za mmunda mu nyengo

yake. Izi sizitanthauza kuti mumasiya minda imene sinakonzeke ayi. Mumapitilizabe kufesa mau

a Mulungu, kudikira, kupemphera kuti Mulungu awapangise kulandira uthenga.

NDONDOMEKO YA “PITANI OSATI “BWERANI”

Page 96: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

96

Mpingo woyamba umagwiritsa ntchito njira “yopita” osati njira “yobwera” ya Chipangano

Chakale mu nthawi ya Israyeli.

Mu nthawi ya Chipangano Chakale mitundu ya anthu imayenera kubwera kwa Israyeli

kudzalandira vumbulutso la Mulungu. Koma mu Chipangano Chatsopano lamulo ndi lakuti

“pitani kudziko lonse lapansi.” Mu Chipangano Chatsopano okhulupirira amatsatira njira

imeneyi. samangokhala pansi kudikirira anthu kuti awapeza kumene iwo akukhala.

WOKHULUPIRIRA ALIYENSE ACHULUKITSE”

Wokhulupirira aliyense wa mpingo woyamba amachuluka pobweretsa okhulupirira atsopano:

Pamenepo ndipo iwo akubalalitsidwa anapitapita nalalikira mauwo (Machitidwe

8:4)

Mpingo ukuyenera kutumiza anthu (MUN ndi akazi) mmagawo onse a moyo. Anthu amene

amakhala ndi mwa chikhulupiriro osti kumangoyankhula. Anthu amene miyoyo yawo inasintha

ndi uthenga wabwino. Msilikali sapambana ku nkhondo pamene wangokhala ku malo

amaphunziro. Wokolola sangokhala mu nkhokwe ndipo nsodzi sangokhala kumtunda

kumadikira.

MAUBALE A ANTHU:

Mu nthawi ya Chipangano Chatsopano uthenga wabwino unafala mwamsanga mmalo amene

anthu anali pa ubale wa mbanja, ndi anzawo. Mwachitsanzo, Yesu anaitana Andreya kuti

amtsate. Mwamsanga Andreya anayamba kugawana uthenga wabwino kwa apabanja ake. Ndipo

anambweretsera Petro kwa Yesu.

Werengani ndimezi zimene zikuonetsera za mmene uthenga unafalikira pakati pa maubale a

anthu:

-Zakeyu ndi banja lake: Luka19

-Banja la mkulu wa ku Kapanawo: Yohane 4:53

-Abale ndi abwenzi a Koneliyo: Machitdwe 10:24,44

-Anthu awiri mnyumba ya Filipo: Machitdwe 16:15 ndi 27-34

-Banja la atsogoleri a Sunagoge: Machitidwe18:8

-Stefano ndi a mnyumba mwake: I Akorinto 1:16

-Amnyumba mwa of Aristobulo ndi Nakiso: Romans 16:10-11

-Onesifolo ndi banja lake: II Timoteo 1:16

-Filemoni ndi banja lake: Filemoni l

NJIRA ZA YESU

Page 97: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

97

Mu buku lonse la Machitidwe, mpingo woyamba unagwiritsa ntchito njira zimene Yesu

anaphunzitsa ndi kuonetsera. Analalikira uthenga, kuphunzitsa mau, kubatiza atsopano, ndi

kuphunzitsa ophunzira (Mateyu 28:19-20).

Pemphero ndi kuwerenga Mau zinali zofunika kwambiri pa kukula kwa mpingo mu

chiwerengero (Machitidwe 6:4).

Kuphatikiza Mau a Mulungu ndi kuonetsera mphamvu zinachulukitsanso mpingo. Pamene anthu

amachiritsidwa, zozizwa zimachitikanso, ziwanda zimathawa ndipo ambiri amabwera kwa

Ambuye.

(Kuonetsera mphamvu kunali kofunika moti a Harvestime International Institute ali ndi phunziro

lotchedwa “Mfundo Zamphamvu”).

MAGULU A CHIPANGANO CHATSOPANO:

Magulu anali ofunika mu Chipangano Chatsopano pa kukula mu chiwerengero. Mu Machitidwe

6:1-7 pamene vuto labwera, gulu lapadera linapangidwa kuthetsa vutoli. Paulo anaphunzitsa

zagulu lapadera la ophunzira pa sukulu ya mdera (Machitidwe 19:9). Mwanthawi, Paulo

amaphunzitsa gulu lapadera la Ayuda ndi a mitundu (Machitidwe 13:42). Magulu ochepa

amakumana mnyumba (Machitidwe 12).

Mipingo yambiri yapanga dongosolo la anthu amumpingo mwawo kuhkala magulu a ang’ono

kuti akwaniritse cholinga chimene sichingakwaniritsidwe ndi bwino ndi mikumano yaikulu ya

mpingo wonse. Magulu ang’ono amakhala pa ubale, oyendayenda ndi omasuka kutumikira

zosowa za anthu.

UTUMIKI WA MZIMU WOYERA:

Mzimu Woyera ndi mphamvu imene imatsutsa anthu ochimwa ndi kuwakopa kuti alandire

uthenga wabwino. Zotsatira za izi ndi kukhala ndi okhulupirira atsopano amene amakulitsa

mpingo.

Ndipo atadza Iyeyo, adzatsutsa dziko lapansi za macimo, ndi za cilungamo, ndi za

ciweruziro;

za macimo, cifukwa sakhulupirira Ine;

za cilungamo, cifukwa ndinka kwa Atate, ndipo simundionanso; 11za ciweruziro,

cifukwa mkuru wa dziko ili lapansi waweruzidwa (Yohane 16:8-11).

Page 98: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

98

MPHATSO ZA MZIMU:

Kukula kwa munthu kumafuna kukula kwa gawo lolimba pofuna kulimbitsa ndi kuthandiza

kuchulukana nkwa ma selo. Kuti thupi la Khristu likule, gawolinso ndi lofunika. Yesu ananena

kuti zokolola zapsa, koma ogwira ntchito ochepa. Ngati ogwira ntchito achepa, ndiye kuti

tigwirizane kuti tikolole zokolola.

Pa cholinga ichi, Mzimu Woyera amapereka mphatso ndi mautumiki osiyana mu mpingo ndi

cholinga chogwira ntchito ya utumiki. Mphatso za Mzimu ndi kuthekera kwa uzimu kopatsidwa

ndi Mzimu Woyera kopangitsa ntchito ya utumiki. Mukhoza kuwerenga mavesi awa:

Aroma 12:1-8, I Akorinto 12:1-31, Aefeso 4:1-16, I Petro 4:7-11

Mulungu ali ndi malo mu mpingo amene ali wokhulupirira:

Koma tsopano, Mulungu anaika ziwalo zonsezo m'thupi, monga anafuna (I

Akorinto 12:18)

Membala aliyense ali ndi malo amene Mulungu anamusankhira. Amapatsidwa mphamvu kuti

akwaniritse cholinga mu mpingo kudzera mu mphatso za Mzimu Woyera. Pamene okhulupirira

akupezeka pa malo amene Mulungu wamusankhira ndi kuyamba kugwiritsa mphatso yake,

mpingo umayamba kuyenda bwino. Mulungu amaufanizira ngati mmene thupi la munthu

limagwirira ntchito pamene chiwalo chilichonse chimachita ntchito yake. (I Akorinto 12:1-31).

Munthu aliyense ndi wofunika pa ntchito ya utumiki, monganso mmene lilili thupi lathu:

Ndipo dise silingathe kunena kwa dzanja, Sindikufuna iwe, kapenanso mutu kwa mapazi,

Sindikufunani inu. 22Koma makamakatu ziwalozo zoyesedwa zofoka m'thupi, zifunika (I

Akorinto 12:21-22).

Harvestime International Institute mu phunziro lawo amalitcha “Utumiki wa Mzimu Woyera”

limapereka tsatanetsatane wa mphatso za uzimu. Pa chifukwa ichi, chidule chokha

chaperekedwa:

Mphatso zapadera za utsogoleri:

Pali ma udindo a utsogoleri amene Mulungu amawaika ndi kuwasankha ena mu mpingo:

Ndipo Iye anapatsa ena akhale atumwi; ndi enaaneneri; ndi ena alaliki; ndi ena

abusa, ndi ena aphunzitsi (Aefeso 4:11)

Atsogoleri apadera operekedwa ndi Mulungu ndi monga:

Atumwi:

Page 99: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

99

Mtumwi ndi amene ali ndi kuthekera kwapadera kutukula mpingo watsopano mmadera komanso

mu zikhalidwe osiyanasiyana ndipo amayang’anira mipingo ngati woyang’anira. Mtumwi ndiye

kuti “wotumidwa” amene watumidwa ndi mphamvu yonse komanso ulamuliro wochita mmalo

mwa wina.” Mtumwi ali ndi ulamuliro wapadera kapena kuthekera kofalisa uthenga wabwino

kumadera ambiri ku dziko lapansi popanga okhulupirira. Masiku ano mpingo ukuwatchula

atumwi ngati wodzala mipingo.

Aneneri:

Pali magawo awiri a uneneri. Loyamba ndi mphatso yapadera yokhala mneneri. Ina ndi mphatso

yolankhula uneneri. Mwachidule, uneneri ndi kulankhula pansi pa kuuzilidwa ndi Mulungu. Ndi

kuthekera kwapadera kolandira ndi kulankhula uthenga wa Mulungu kwa anthu ake. Munthu

amene ali mneneri ali ndi mphatso ya utsogoleri yapadera ya uneneri komanso mphatso

yolankhula uneneri.

Alaliki:

Mlaliki ali ndi kuthekera kwa kogawana ndi uthenga wabwino ndi anthu osakhulupirira ndi

cholinga kuti anthuwa akhale mu thupi la Yesu. Tanthauzo la “mlaliki” ndi amene amagawa

uthenga wabwino.

Abusa:

Abusa ndi atsogoleri amene amakhala nthawi yaitali yoyamg’anira moyo wa uzimu wa gulu la

okhulupirira.

Aphunzitsi:

Aphunzitsi ali ndi kuthekera kolankhula Mau a Mulungu cholinga choti adziwitse anthu ndi

kugwiritsa ntchito zimene aphunzirazo. Mphunzitsi ndi amene ali ndi mphatso yophunzitsa

komanso amakhala atsogoleri a mu mpingo.

Mphatso zisanu za utsogolerizi zimagwira ntchito pamodzi ndi cholinga chokulitsa mpingo.

Atumwi amakulitsa mpingo polalikira uthenga wabwino ku madera osiyanasiyana ndi kukhala

ndi okhulupirira atsopano. Mulungu amachita zozizwa ndi zodabwitsa pofuna kuthandiza kukula

kwa uthenga wabwino. Atumwi amapereka utsogoleri wapadera ku mpingo umene awudzutsa.

Udindo wenweni wa iwo amene ali ndi mphatso ndi kuthandiza okhulupirira ena kuzindikira ndi

kugwiritsa ntchito mphatso zawo za uzimu (Aefeso 4:11-16). Ntchito ya utumiki imafuna

kuchitachita kwa onse. Pamene thupi la Khristu siligwira ntchito moyenera, mamembala ofooka

amatengedwa ndi mosavuta ndi ziphunzitso zonama (Aefeso 4:14).

Ichi ndi chidule cha mphatso za uzimu zopatsidwa kwa okhulupirira:

Mphatso zolankhula:

Page 100: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

100

Mphatso izi zimatchedwa “zolankhula” chifukwa zimakhudza kulankhula momveka (mokweza).

Mphatsozi ndi monga uneneri, kuphunzitsa, chilimbikitso, mawu a nzeru (kuthekera kolandira

chidziwitso cha mmene zinthu zikhalire), mawu a chidziwitso (kuthekera komvetsa zinthu

zimene ena sadziwa ndipo sangamvetse ngakhale kutha kugawira kwa ena.

Mphatso zotumikira:

Mphatso izi zimatumikira mpingo pothandiza ndondomeko, dongosolo ndi chithandizo cha ku

uzimu kapena kuthupi.

Kutumira: kuthekera kogwira ntchito ya Ambuye, kumasula ena ndi zina.

Thandizo: kuthandiza ena mu ntchito za Ambuye powachulukitsa kuti azichita bwino.

Utsogoleri: kuthekera kokhala ndi zolinga zogwirizana ndi Mulungu ndi kuuza ena za izi.

Munthu amene ali ndi mphatso imeneyi amalimbiktsa ndi kutsogolera ena kuwaniritsa cholinga

cha Mulungu ku ulemerero wa dzina lake.

Dongosolo: mphatsoyi imatchedwa “maboma” Mbaibulo. Munthu amene ali ndi mphatsoyi

amakhala ndi kuthekera kotsogolera, kulongosola, ndi kupanga ziganizo mmalo mwa ena.

Kupereka: kuthekera kwapadera kopereka zinthu, ndalama, nthawi, mphamvu ndi luso ku ntchito

ya Mulungu.

Kuonetsa chifundo: chifundo chapadera ndi kuthekera kothandiza iwo akuvutika.

Kuzindikira mizimi: kuthekera kokhalandi kawuniwuni wa anthu, ziphunzitso ndi nyengo ndi

kutsimikiza ngati zikuchokera kwa Mulungu kapena Satana.

Chikhulupiriro: munthu wa chikhulupiriro amakhala ndi kuthekera kokhulupirira zinthu pa

kulimba mtima ndi kudalira Mulungu mu nyengo zovuta.

Kuchereza alendo: kuthekera kopereka chakudya ndi malo ndi zinthu zina kwa iwo amene ali ndi

zosowa.

Mphatso za zozizwa:

Izi ndi zozizwa za umulungu za mphamvu ya Mulungu kudzera mwa okhulupirira pofuna

kuwaniritsa Mau a Mulungu.

Malilime: kuthekera kolandira ndi kulankhula uthenga wa Mulungu kupita kwa anthu mwa

ziyankhulo zachilendo.

Kumasulira: kuthekera kodziwitsa uthenga mu chilankhulo chomveka cha amene alankhula ndi

malilime ena.

Page 101: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

101

Zozizwa: kudzera mwa munthu amene ali ndi mphatso ya kuchita zodabwitsa za Mulungu

amachita mwamphamvu ya Mulungu kuposa ya chilengedwe.

Machiritso: munthu ameneyi amakhala ndi kuthekera kolola mphamvu ya Mulungu kuwombola

moyo posagwiritsa ntchito njira zachilengedwe.

MAUTSOGOLERI ENA A MBAIBULO

Okhulupirira amene ali ndi mphatso zapadera si omwewa amene ali ndi utsogoleri mu Mbaibulo

kuti atumikire mu mpingo. Palinso ma udindi ena monga akulu a mpingo, oyanga’anira amene

akupezeka mu Chipangano Chatsopano. Maudindo amenewa ndi ofunikiranso pa kukula kwa

mpingo.

Maudindo amenewa ndi osiyana ndi mphatso za utsogoleri zimene mwaphunzira. Awa ndi

maudindo apadera amene anakhazikitsidwa ndi mpingo wakale othandizira kukula kwa mpingo

mu chiwerengero. Mukhoza kuwerenga Machitidwe 6:1-7 za mmene analili mu mpingo

woyamba.

Zimene mpingo wakale umachita zinali cholinga cha Mulungu kuti zikhale chitsanzo chathu.

Maudindowa akhoza kugwiranso ntchito lero lino. Cholinga cha maudindo amenewa ndi

kuthandiza iwo amene ali ndi mautumiki a mphatso zapadera monga za atumwi, aneneri, alaliki,

abusa ndi aphunzitsi.

Dziwani: mawu oti “akulu a mpingo” anayamba kugwiritsidwa ntchito mu Eksodo 3:16 pofuna

kunena za Israyeli. Pali mavesi ambiri amakamba za akulu a Israyeli mu Baibulo. Akuluwa ndi

osiyana ndi amene anali ndi utsogoleri wa mpingo woyamba.

ZOWAYENEREZA A BISHOPO NDI AKULU A MPINGO

Werengani mavesi ndipo phunzirani zina mwa zinthu zimene atumiki akuyenera kukhala:

I Timoteo 3:2-12, Tito 1:6-9 ndi Aroma 16:2

Page 102: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

102

MAYESO ODZIYETSA NOKHA

1. Lembani Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

__________________________________________________________________________

2. Kodi chimachitika ndi chiyani pamene mpingo ukukula mu chiwerengero?

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

__________________________________________________________________________

3. Lembani chidule cha mmene mpingo woyamba unakulira ku Yerusalemu.

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

4. Pansipa pali njira za kukula kwa mpingo mu Chipangano Chatsopano. Lembani

mwachidule pa pepala lina za mmene zinagwirira ntchito kuti mpingo ukule ku

Yerusalemu.

-Masomphenya a uzimu

-Nthawi ndi malo amene uthenga wabwino umalandilidwa

-"Pitani" osati "bwerani" ngati njira

-Okhulupirira aliyense achulukane

-Maubale

-Njira za Yesu

-Magulu

-Khomo lililonse

-Utumiki wa Mzimu Woyera

-Mphatso ndi maudindo a uzimu

(Mayankho a mafunsowa akupezeka kumapeto kwenikweni kwa bukuli).

Page 103: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

103

KUPITILIZA KUPHUNZIRA

1. Pa nkhani ya kukula kwa mpingo mu chiwerengero pali zinthu zitatu zofunika. Mzimu

wa Mulungu (Machitidwe 1-11, Mau a Mulungu (Machitidwe 12:20) ndi munthu wa

Mulungu (Machitidwe 21-28).

2. Magulu a padera a uthumi anali amodzi amene amene anabweretsa kukula kwa mpingo

wakale. Awa ndi ena mwa magulu a padera a utumuki amene mukhoza

kumawapempherera mu mpingo mwanu:

-Kuphunzitsa obadwa mwatsopano

-Akazi atsopano ndi oyembekezera

-Ana

-Achinyamata

-Achikulire

-Mabanja atsopano

-Osakwatiwa / osakwatira

-Utumiki wa iwo amene ali mu msinga za mowa, fodya, mankhwala ozunguza bongo.

-Utumiki wa abambo

-Utumiki wa amayi

-Amasiye, osiidwa banja

-Olumala

3. Magulu onse amene ali mu mpingo amafuna mtsogoleri. Onetsetsani kuti mtsogoleri

amene akutsogolera ali ndi zomuyenereza kukhala mtsogoleri molingana ndi Baibulo.

4. Kafukufuku wa kukula kwa mpingo anachitika ku Amerika ndipo anapeza zinthu zimene

zimakuluitsa mpingo mu chiwerengero. Zina mwa izo ndi izi:

Utsogoleri wa uzimu wamphamvu

Ulaliki wa kathithi

Kuonetsera mphamvu za Mzimu woyera

Maziko a chuma amphamvu

Mphatso ndi zipatso za Mzimu

Pemphero

Mautumiki osiyanasiyana

Kugwiritsa ntchito Baibulo

Kukamba za Yesu yekha basi.

Page 104: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

104

CHAPUTALA CHA 8

KUKULA MMADERA

ZOLINGA:

Pakutha pa chaputalachi muyenera:

Kulemba Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

Kupereka tanthauzo la “kukula mmadera”

Kupereka tanthauzo la “kudzala mpingo”

Kuomba mkota pa kukula mmadera kwa mpingo wa chipangano chatsopano.

Longosolani za mmene mpingo umachulukira kudzera mmadera.

Kudziwa njira zinayi zimene mpingo ungayambire

Kudziwa mitundu itatu ya kukula mmadera kwa mpingo.

Lembani zimene Baibulo limafuna posankha madera amene mungadzaleko mipingo

Longosolani uthenga umene ungayambitse mpingo.

VESI LOTSOGOLERA:

Kotero Mipingoyo inalimbikitsidwa m'cikhulupiriro, nacuruka m'ciwerengo cao

tsiku ndi tsiku (Machitidwe 16:5)

MAWU OYAMBA

Ophunzira analamulidwa ndi Yesu kuti akhale mboni ku Yerusalemu, Yudeya, Samariya ndi

malekedzero a dziko lapansi (Machitidwe 1:8).

Monga mwaphunzira chaputala changothachi, mpingo wa ku Yerusalemu unachuluka kwambiri.

Gawo lina mu dongosolo la Mulungu linali kukulitsa mmadera. Mpingo wa ku Yerusalemu

unayenera kuyambitsa mipingo ina mu mizinda ya Ayuda.

KUKULA MMADERA

Kukula mmadera kumayamba pamene mpingo wayambitsa mpingo wina mu dera la anthu a

chikhalidwe chofanana. Mpingo watsopanowo umakhala wina wochokera ku mpingo “waukulu”

monga ngati mwana akakhala ndi makolo ake mdzikoli.

Ngati mpingo “waukuluwo” uli wokhwima mu uzimu, mpingo watsopanowo udzakulanso

momwemo. Ngati pali mavuto mu mpingo “waukulu” mpingo watsopanowo udzakhalanso ndi

ndi mavutowo. Izi ndi chifukwa chake mkofunika kwa mpingo kuti uyambe wakula mkati

usanayambe kuganiza zoyambitsa mpingo kwina.

Mawu oti “Kudzala mpingo” ndi mawu amene timagwiritsa nchito pokamba za kukula mmadera

ndi kubweretsa kukula kwa mpingo. Mawuwa amagwiritsidwa ntchito chifukwa mmodzi

Page 105: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

105

“amadzala” mpingo watsopano ngati mlimi adzala mbewu munthaka. Mu dothi la nthaka,

mbewu idzakula ngati yatsopano monga ngati “makolo” amene mbewuyo inachokera.

Mawu oti “kudzala” amafunika chifukwa sizikwanira pa “kulongosola” mpingo umene suyenera

mu chikhalidwe cha anthu. Sizikwanira “kungoyambitsa” mpingo mkuwusiya kuti uzivutika.

Umayenera “kudzalidwa” zimene zikutanthauza kuti umaikizidwa, kukulitsidwa ndi kupitilira

moyo wa uzimu.

KUKULA KWA MPINGO MMADERA MCHIPANGANO CHATSOPANO

Kuchuluka kumachitika pogawana. Ndipo kugawana ndi njira yoyamba yofunika imene

Mulungu amachulukitsira. Ngati mwadala sitikusankha kugawana ndi kuchulukana, Mulungu

adzalola zinthu zina zipangise. Machitidwe 8 amakamba za chizunzo chachikulu pa okhulupirira

ku Yerusalemu. Chizunzochi chinabweretsa kugawana ku mpingo wa ku Yerusalemu pakuti

anthu anathawa kupita ku mizinda ina.

Pamene anthu amathawa ku Yerusalemu, “kumene amapitako amalalikira Mau” (Machitidwe

8:4). Obadwa mwatsopano amapezeka ndipo mipingo yatsopano imadzalidwa. Mipingo imrneyi

imakulitsa mpingo “waukulu” wa ku Yerusalemu.

Mpingo wa Chipangano Chatsopano sunakule mmadera podzala mipingo ina yokha ayi,

komanso unalumikiza danga loyambitsa mipingo yambiri mu madera ena. Muphunzira izi mu

phunziro la “kukula kwa mpingo kolumikiza maiko” mu chaputala chikubwerachi.

Mbiri ya kukula kwa mpingo mmadera mu buku la Machitidwe inayamba ku Yerusalemu,

Yudeya, Galileya, Ludda, Sarone ndi Ku Yopa. Awa anali madera a chikhalidwe cha Ayuda. Si

munthu wokhulupirira payekha amene akachuluka ku uzimu, koma mipingo inachulukanso mu

chiwerengero pamene mpingo wa ku Yerusalemu umakula pochitira umboni

mderalo...Machitidwe 16:5

MMENE MIPINGO INAKULIRA MMADERA

Pali njira zimene mpingo watsopano umayambira:

1. Mpingo wina umayambitsa mpingo umzake.

2. Mipingo kugwirizana kuyambitsa mpingo wina.

3. Mpingo waukulu kugawana kupanga mipingo iwiri kapena yoposera apo.

4. Wokhulupirira mmodzi akhoza kukuyambitsa mpingo. Amene ali ndi mphatso ya uzimu

ya utumwi angatero mosavuta. Munthu ameneyi nthawi zina amatchedwa “wodzala

mpingo.”

Muzonse izi, kuchulukana kumachitika kudzera mu kufalisa uthenga pokhala ndi

okhulupirira atsopano.

MITUNDU YA KUKULA KWA MPINGO MMADERA

Mipingo yatsopano imakhala ndi makulidwe osiyana a mmadera:

Page 106: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

106

1. MIPINGO KUMATUMIKIRA KU MADERA:

Iyi ndi mipingo yokhazikitsidwa ndi cholinga chotumikira ku madera, mmidzi, kapena mu

mzinda. Izi zikhoza kukhala zotsatira za ulaliki umene waitana gulu la anthu okhulupirira mdera.

Ikhoza kukhazikitsidwa kuti itumikire anthu amene sanafikilidwe ndi uthenga kapena ku malo

kumene uthenga sulandilidwa.

2. MIPINGO YOTUMIKIRA KU MAGULU A MITUNDU YA ANTHU:

Chiyanjano cha mautumiki awa amtumikira ku magulu a anthu amene ali ndi zikhalidwe,

ziyankhulo komanso mitundu yofanana. Mwachitsanzo mpingo ukhoza kuyamba kwa anthu

amene amalankhula Spanishi koma sangamve chingerezi ngati “chiyankhulo” chawo choyamba.

3. MIPINGO YOKHALA NDI CHOLINGA CHAPADERADERA:

Mpingo ukhoza kukhazikitsidwa ndi cholinga chapedera: Mwachitsanzo, mpingo ukhoza

kudzalidwe kufupi ndi malo amene ophunzira amachitirako maphunziro kuti azitumikira

ophunzira.

ZOFUNIKA TIKAMAYAMBA KUKULITSA MPINGO MMADERA

Baibulo limaphunzitsa zinthu zimene ndi zofunikira pokulitsa mpingo polalikira uthenga

wabwino pamene tikufuna kukhazikitsa mipingo. Zofunikirazo ndi izi:

OSAFIKILIDWA:

Chinthu choyambirira ndi anthu osafikilidwa. Paulo anati:

Pakuti, amene ali yense adzaitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.

Ndipo iwo adzaitana bwanji pa iye amene sanamkhulupirira? ndipo

adzakhulupirira bwanji iye amene sanamva za iye? ndipo adzamva bwanji

wopanda wolalikira (Aroma 10:13-14)

Kumalo kumene kulibe umboni wa uthenga wabwino kukuyeneran kukhala koyamba.

Werengani fanizo la nkhosa mu Luka 15:3-7. Chinthu choyamba chinali pa nkhosa yotaika, osati

pa zomwe zinali nkhola.

OLANDIRA:

Mwaphunzira mu phunziro lotsiriza za kufumikira kwa kulalikira kwa munda wa uzimu umene

uthenga umalandirika. Yesu anaphunzitsa mu Mateyu 10:13-15; Luka 8:5-15) ndi Paulo

analankhulanso (Machitidwe 13:42-51). Yesu ndi Paulo sanakane za malo osalandilika.

Anapitilira kulalikira uthenga kwa iwo ndikuchenjeza za chiwereuzo cha Mulungu. Koma

anayambirira kwa anthu amene amalandira uthenga.

Page 107: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

107

KUYAMBA MIZINDA, KENAKO MADERA A KUMUDZI:

Iyi inali njira imene Paulo anagwiritsa ntchito imene muphunzira zambiri mukafika mu chaputala

chikubwerachi. Mizindi ili ndi chiwerengero chambiri cha anthu. Anthu ambiri amapita ku

kukachita malonda ku mizinda. Anapitilira kulalikira uthenga ndi kuchenjeza za chiwereuzo cha

Mulungu. Pamene mukufikira anthu ambiri mi mizinda, iwowa amabwerera ku midzi

kumakagawira anthu uthenga wabwino ndi kudzala mipingo yatsopano.

Kaya ndi zokhuza za kusintha kwa zikhalidwe, machitidwe a moyo, malamulo, kusintha

kumeneku kumayamba ku mizinda kenako kumudzi. Pamene mwafikira mizinda ndi uthenga

wabwino, umafalikira kumalo konse kwa deralo mpakana ku midzi.

UTHENGA

Uthenga wa iwo amene amadzala mipingo ndi wakuti:

UTHENGA WA MBAIBULO:

Mipingo yatsopano inabadwa chifukwa cha iwo amene sanatembenuke mtima atatha kumva

uthenga wabwino ndi kulandira Yesu kukhala Mbuye ndi mpulumutsi wa moyo wawo. Pamene

kulalikira kuli kochokera Mbaibulo, kumakhala ndi ulamuliro wa Mulungu. Omvera amadziwa

ndi kuchitapo kanthu pa za mphamvu ya Mau a Mulungu.

WOKAMBA ZA MKRISTU:

Yesu ndiye mwini wa uthenga umene umachulukitsa mipingo. Anthu akuyenera kudziwa Yesu

ndi ndani, kufunikira kwa utumuki wake wa padziko lapansi, imfa yake, ndi kuuka kwake kwa

akufa. Akuyenera kuphunzitsaidwa za mmene angachitire ndi kulandira uthenga wabwino wa

chipulumutso ndi moyo wosatha.

UTHENGA WOKHAZIKIKA PA CHOSOWA:

Anthu amachitapo kanthu pa uthenga umene ukukumana ndi chosowa chawo. Chitsanzo cha ichi

ndi Yesu ndi mkazi pa chitsime (Yohane 4). Uthenga wake ukhakhazikika pa pa chosowa chake

pa madzi akumwa.

MMENE TIGZDZALIRE MPINGO WATSOPANO:

Maphunziro ambiri a Harvestime International Institute amakamba zambiri za mmene

tingadzalire mpingo watsopano. Ngati mukuphunzira phunziroli la Harvestime Institute mu

ndondomeko yawo, phunziro limene mukuphunzirali lili gawo limodzi la mapgunziro a Mfundo

za Baibulo za kuchulukitsa.

Pofuna kudzala ndi kulongosola mipingo, mukuyenera kuphunzira maphunzirowa. Pakadali pano

yambani kupemphera chitsogozo cha Mulungu cha kumene akufuna iye kuti mukule. Ngati muli

Page 108: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

108

mbusa wa mpingo, musadwabwe pa nkhani yoti muchulukane. Mwaphunzira kale kuti

kuchuluka ndi chifuniro cha Mulungu.

Pemphero lanu likhale pa kumene mukufuna kudzala mpingo watsopano ndi nthawi imene

muchite chifukwa nthawi ndi malo ndi zofunika pa zokolola za uzimu. Mukuyenera kuchulukana

ku malo oyenera komanso pa nthawi yabwino.

MIPINGO YATSOPANO IKUYENERA KUKULA

Monga mwana akabadwa mdzikoli, mpingo watsopano ukuyenera kudalira “kholo” la mpingo pa

kukula kwake. Koma pamene mpingo watsopano ukukula, ukuyenera kukhala osiyana, thupi la

okhulupirira lochitachita, ndi kuthekera kwa kuchulukana ku uzimu pa kuberekana. Ichi ndi

chitsanzo cha mipingo imene Paulo anadzala.

Mpingo wadera ukuyenera kukula kuchokera mu mfundo za Mmalemba zimene zimakamba za

“Kukula kwa Mpingo mu chiwerengero.” Kuti ukule bwino mpingo uliwonse watsopano

ukuyenera:

1. KUMVETSA CHOLINGA CHAKE:

Madongosolo onse a mu mpingo akuyenera kugwirizana ndi zolinga za Mpingo.

Harvestime International Institute ali ndi phunziro la “Dongosolo pa Zolinga” limene

limalongosola izi mwatsatane.

2. KUMVETSA MFUNDO ZA MMBAIBULO ZA DONGOSOLO:

Izi ndi monga mphatso za uzim ndi mautumiki a mumpingo ndi mpaphunziro a

okhulupirira atsopano kuti akhala atsogoleri a ku uzimu otha kugwiritsa ntchito mphatso

zawo. Harvestime International Institute ali ndi phunziro la “Dongosolo la Mfundo za

Mbaibulo” ndi “Dongosolo pa Zolinga” amene adzakuthandizani pophunzira.

3. KUMETSA ZOMUYENEREZA MTSOGOLERI ZA MBAIBULO:

Harvestime International Institute ali ndi phunziro la “Dongosolo la Mfundo za

Mbaibulo” limene lingakuthandizeni pa maphunziro anu.

4. KUPHUNZITSIDWA MAZIKO A CHIKHULUPIRIRO:

Maphunziro a Harvestime mu bukhu la “Kukhala Wachiwiri” a Harvestime International

Institute azakuthandizani kukwaniritsa zolinga zanu.

5. KHAZIKIKANI PA MAFUNSO ENIENI:

Mafunsowa ali ndi zinthu monga:

Page 109: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

109

-Kupanga chiphunzitso chimene alendo adzadziwa zikhulipiriro zanu za mpingo za

Mbaibulo.

-Malamulo amene boma limafuna pa za mpingo watsopano.

-Dongosolo la mpingo lokhuza utsogoleri, mautumiki, ndi ndondomeko za chuma cha

mpingo.

-Malo ndi umwini wake wa katundu wa mpingo.

-Ubale wake wa “likulu” la mpingo ndi mipingo yatsopano.

Page 110: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

110

MAYESO ODZIYETSA NOKHA

1. Lembaini Vesi Lotsogera kuchokera pamtima.

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

2. Kodi kukula kwa mpingo “mmadera ndi chiyani?

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

3. Kodi “kudzala mpingo” kumatanthauza chiyani?

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

4. Lembani chidule cha kukula kwa mpingo woyamba mmadera ku Yerusalemu.

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

5. Lembani njira zinayi zimene mpingo watsopano ungayambire.

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

6. Lembani mitundu itatu ya kukula mmadera kwa mpingo.

____________________________________ ____________________________

________________________________________________________

7. Ndi mfundo ziti zoyamba zimene Baibulo limanena posankha madera oyambitsako

mipingo?

______________________________________________________________________________

________________________________________________________________________

8. Kodi ndi mtundu uti wa uthenga umene umayambitsa mpingo watsopano?

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

(Mayankho a mafunsowa akupezeka kumapeto kwenikweni kwa bukuli)

Page 111: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

111

KUPITILIZA KUPHUNZIRA

Popitiliza kuphunzira za mmene mungadzalire mpingo onani maphunziro awa a Harvestime

International Institute:

Dongosolo la mpingo la Mbaibulo lidzakutsogolerani posankha ndi kupanga atsogoleri a

mpingo.

Kusanthula Malo lidzakuthandizani kudziwa malo amene uthenga wabwino ungafikeko ndi

kudzalako mpingo.

Dongosolo la Zolinga lidzakuphunzitsani kukhazikitsa cholinga, kupanda zochita ndi

kulongosola mpingo.

Ndondomeko Zolimbikitsa zidzkuthandizani kulimbikitsa chiyanjano cha mpingo pa ulaliki.

Chotupisa ngati Ulaliki lidzabweretsa okhulupirira atsopano pa mpingo.

Page 112: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

112

CHAPUTALA CHA 9

KUKULA POLUMIKIZA

ZOLINGA:

Pakutha pa chaputalachi muyenera:

Kulemba Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

Kulongosola tanthauza la “kukula polumikiza” mipingo.

Kupereka Vesi la Mbaibulo la dongosolo ma Mulungu la “kukula polumikiza”

mpingo.

Kudziwa Vesi Lotsogolera la mtsogoleri wa mu Chipangano Chatsopano pa nkhani

ya “kukula polumikiza”

Kulemba chidule cha njira zimene Paulo anagwiritsa ntchito pokulitsa uthenga

wabwino mmadera a zikhalidwe zina.

VESI LOTSOGOLERA:

… Kukawatsegulira maso ao, kuti atembenuke kucokera kumdima, kulinga

kukuunika, ndi kucokera ulamuliro wa Satana kulinga kwa Mulungu, kuti

alandire iwo cikhululukiro ca macimo, ndi colowa mwa iwo akuyeretsedwa

ndi cikhulupiriro ca mwa Ine (Machitidwe 26:18)

MAWU OTSOGOLERA

Chaputala chomwe mwamalizirachi chikukamba za kukula kwa mpingo mmadera kumene

kumachitika podzala mipingo yatsopano mu madera ofanana chikhalidwe. Zikuyenera kukhala

limodzi ndi phunziro la kukula kwa mpingo polumikiza.

Mfundo zomwezo zofunikira pa kukula kwa mpingo mmadera zikugwiranso ntchito pa kukula

kwa mpingo polumikiza. Izi zikutanthauza kuti chilichonse chakambidwa mu phunziro lathali,

ndi chofunikanso mu phunziro lino. Koma kukulitsa polumikiza kumafuna njira zina zimene ndi

za chaputalachi basi.

KUKULA POLUMIKIZA

Kukula polumikiza kumachitika pamene mpingo uzikulitsa mmadera a dziko, chiyankhulo,

malire a mitundu podzala mpingo watsopano mu zikhalidwe zatsopano za anthu. Mawu oti

“kulumikiza” akugwiritsidwa ntchito chifukwa pamene ntchito ikuchitika “mlato” umaikidwa

kuchokera ku chikhalidwe china kupita ku chikhalidwe china polafalitsa uthenga. Njira

zatsopano za mayendedwe ndi zolumikizana zatukula kwambiri machitidwe a mpingo okula

polumikiza ngakhale ku malo akutali.

Page 113: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

113

KUKULA KOLUMIKIZA MCHIPANGANO CHATSOPANO

Kukula kolumikiza madera kunali gawo limodzi la dongosolo la Ambuye Yesu pofuna kufalitsa

uthenga wabwino mdziko lonse lapansi. Ophunzira amayenera kuyamba kuchitira umboni

mmadera a zikhalidwe zawo ku Yerusalemu keneko kukula popita ku madera ena ofanana nawo

zikhalidwe kukudzala mipingo.

Kenako, ophunzira amayenera kulumikiza maiko, zilankhulo ndi malire pofalisa uthenga

wabwino mu zikhalidwe zosiyana ndi zawo monga Samariya ndi “malekezero onse a dziko

lapansi” (Machitidwe 1:8). Ophunzira mwachangu anakwaniritsa lamuloli pochulukana pakati pa

anthu a zikhalidwe zawo (Machitidwe 2).

Kukula ku madera ena a zikhalidwe zawo kunabwera chifukwa cha chizunzo:

… Koma pamene atumwi a ku Yerusalemu anamva kuti Samariya adalandira mau

a Mulungu, anawatumizira Petro ndi Yohane; (Machitidwe 8:14).

Filipo koyamba analumikiza kusiyana kwa zikhalidwe pa chitsitsimutso cha ku Samariya pa

Machitidwe 8. Petro ndi Yohane anapitiliza utumiki mu dera lomwelo.

Mtumwi Petro anali ndi vuto polandira ntchito yotumidwa wa anthu osiyana zikhalidwe. Anali

mu Yuda wachipembedzo ndipo mwa kanthawi anali ndi malire polumikizana ndi Amitundu

(anthu amene sanali Ayuda). Mulungu analankhula kwa Petro mmasomphenya pa Machitidwe

10 ndipo Petro anatengera uthenga wabwino kwa amitundu ku Kaesareya.

Kukula kolumikiza mu Chipangano Chatsopano kukuonetsedwa bwino ndi utumiki wa mtumwi

Paulo. Mulungu akuitana Paulo ku utumuki umenewu. Paulo anali mu Yuda, koma Mulungu

anamuuza kuti anali:

Koma Ambuye anat kwa iye, Pita; pakuti iye ndiye cotengera canga cosankhika,

cakunyamula dzina langa pamaso pa amitundu ndi mafumu ndi ana a Israyeli

(Machitidwe 9:15).

Chifukwa Paulo anaitanidwa ndi Mulungu pa utumiki wopita kwa anthu a zikhalidwe zina, njira

zake ndi zofunika pofuna kumvetsetsa kukula kwa mpingo polumikiza. Werengani nkhani ya

kutembenuka mtima kwa Paulo mu Machitidwe 9. Zina zonse za buku la Machitidwe ndi nkhani

ya ntchito ya umishoni kwa mitundu ya dziko. Ambiri mwa mabuku a Chipangano chatsopano

ndi makalata otsatira kwa mipingo imene anadzala mmadera osiyanasiyana (Aroma ndi Aheleni).

NJIRA ZA MTUMWI PAULO

Paulo anasankhidwa ndi Mulungu ngati chitsanzo chathu:

Komatu mwa ici anandicitira cifundo, kuti mwa ine, woyamba, Yesu Kristu

akaonetsere kuleza mtima kwace konse kukhale citsanzo ca kwa iwo

adzakhulupirira pa iye m'tsogolo kufikira moyo wosatha (I Timoteo 1:16).

Page 114: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

114

Ichi ndi chifukwa njira za Paulo zikhoza kukhala ngati chitsanzo pa kukula kwa mpingo

polumikiza. Izi ndi zina mwa mfundo za kukula polumikiza mu utumiki wa Paulo:

CHOLINGA CHABWINO:

Paulo amalimbikitsidwa ndi nyengo za amitundu zopanda Yesu (Amitundu ndiye kuti mitundu

yonse imene si Israyeli).

Momwemo kumbukirani, kuti kale inu amitundu m'thupi, ochedwa kusadulidwa

ndi iwo ochedwa mdulidwe m'thupi, umene udacitika ndi manja; 12kuti nthawi ija

munali opanda Kristu, alendo a padera ndi mbumba ya Israyeli, ndi alendo alibe

kanthu ndi mapangano a malonjezano, opanda ciyembekezo, ndi opanda Mulungu

m'dziko lapansi (Aefeso 2:11-12).

Amaumilizidwa ndi chidwi cha lamulo:

Ine ndiri wamangawa wa Ahelene ndi wa akunja, wa anzeru ndi wa opusa.

15Cotero, momwe ndingakhoze ine, ndirikufuna kulalikira Uthenga Wabwino kwa

inunso a ku Roma (Aroma 1:14-15).

Paulo amalimbikitsidwa ndi khumbo lomvera masomphenya opatsidwa ndi Mulungu:

Potero, Mfumu Agripa, sindinakhala ine wosamvera masomphenya a Kumwamba

(Machitidwe 26:16)

Amalimbikitsidwa ndi changu ndi katundu wa pa Mulungu:

Pamene Paulo analindira iwo pa Atene, anabvutidwa mtima pamene anaona mudzi

wonse wadzala ndi mafano (Machitidwe 17:16)

Amalimbikitsidwa ndi chikondi choyera:

Koma m'zonse tidzitsimikfzira ife tokha monga atumiki a Mulungu, m'kupirira

kwambiri, m'zisautso, m'zikakamizo, m'zopsinja

M'mayeredwe, m'cidziwitso, m'cilekerero, m'kukoma mtima, mwa Mzimu Woyera,

m'cikondi cosanyenga (II Akorinto 6:4,6)

ZOFUKIKA KOYAMBIRIRA:

Paulo anali ndi zinthu zofunikira. Zinthu zimene zinali phindu kwa iye…maphunziro, katundu,

chuma, maudindo, ndi zina…anaziyesa zopanda kanthu ku uzimu. Chokhacho chimene

chinampindulira kwa Yesu chinali choyambirira:

Page 115: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

115

Komatu zonse zimene zinandipindulira, zomwezo ndinaziyesa citayiko cifukwa ca

Kristu.

Komatu zeni zeninso ndiyesa zonse zikhale citayiko cifukwa ca mapambanidwe a

cizindikiritso ca Kristu Yesu Ambuye wanga, cifukwa ca Iyeyu ndinatayikitsa

zinthu zonse, ndipo ndiziyesa zapadzala, kuti ndikadzionjezere Kristu (Afilipi 3:7-8)

Zinthu zanu zofunikira zikuyenera kukhala:

1. Ubale wanu ndi Mulungu.

2. Ubale wanu ku thupi la Khristu (kuphatikizapo banja lanu ngati gawo la thupilo).

3. Utumiki wanu kwa Mulungu.

Ubale umabwera pambuyo pa utumiki pa zifukwa ziwiri:

1. Simungatumikire pamene ubale wanu siuli bwino ndi Mulungu.

2. Simungatumikire pamene ubale wanu siuli bwino ndi anthu ena. Ziwalo za thupi la

Khristu (kuphatikizapo banja lanu) sizingalandire utumiki wanu pamene ubale wanu ndi

ena siuli bwino.

MAWU A MULUNGU:

Utumiki wa Paulo unakhazikika pa Mau a Mulungu. Pamene Mau a Mulungu amafalikira ku

zikhalidwe za anthu ena, mipingo imafalikira:

Koma mau a Mulungu anakula, nacurukitsa (Machitidwe 12:24)

Cotero mau a Ambuye anacuruka mwamphamvu nalakika (Machitidwe 19:20)

Kotero Mipingoyo inalimbikitsidwa m'cikhulupiriro, nacuruka m'ciwerengo cao

tsiku ndi tsiku (Machitidwe 16:5)

UTHENGA WA UTHENGA WABWINO:

Uthenga wabwino wa Ufumu wa Mulungu wa Paulo. Sanasemphanitse ndi ntchito za za

umishoni kwa maiko osowa ndi mphamvu ya kulalikira uthenga wabwino. Sanagwiritse ntchito

machitidwe ake kuti akope anthu ambiri. Anthu amakhuzidwa ndi mphamvu ya Mulungu.

Pakuti Uthenga Wabwino sundicititsa manyazi; pakuti uti mphamvu ya Mulungu

yakupulumutsa munthu ali yense wakukhulupira; kuyambira Myuda, ndiponso

Mhelene (Aroma 1:16).

PEMPHERO:

Page 116: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

116

Paulo anapempherera chitsogozo cha Mulungu polalikira uthenga wabwino kwa anthu a

zikhalidwe zina:

Ndipo pa kutumikira Ambuye iwowa, ndi kusala cakudya, Mzimu Woyera anati,

Mundipatulire Ine Bamaba ndi Saulo ku nchito imene odinawaitanirako.

Pamenepo, m'mene adasala cakudya ndi kupemphera ndi kuika manja pa iwo,

anawatumiza amuke (Machitidwe 13:2-3)

MZIMU WOYERA:

Mzimu Woyera anali mtsogoleri wa utumwi wa Paulo. Mwachitsanzo, mu nyengo ina…

… atawaletsa Mzimu Woyera kuti asalalikire mau m'Asiya (Machitidwe 16:6)

ULALIKI, CHIPHUNZITSO, KUCHITIRA UMBONI:

Paulo anatsata malangizo a kutumwa kwakukulu kolalikira, kuphunzitsa ndi kuchitira umboni wa

uthenga wabwino.

Ndipo tsiku loyamba la sabata, posonkhana ife kunyema mkate, Paulo

anawafotokozera mau, popeza anati acoke m'mawa mwace; ndipo ananena cinenere

kufikira pakati pa usiku… (Machitidwe 20:7)

Kuti sindinakubisirani zinthu zopindulira, osazilalikira kwa inu, ndi

kukuphunzitsani inu pabwalo ndi m'nyumba m'nyumba, ndi kucitira umboni

Ayuda ndi Ahelene wa kutembenuza mtima kulinga kwa Mulungu, ndi

cikhulupiriro colinga kwa Ambuye wathu Yesu Kristu (Machitidwe 20:20-21).

Sizokwanira kulumikizana mu uthenga wabwino okha. Unthenga ukuyenera kuperekedwa mu

njira imene ingamveke kwa anthu omvera. Mawu, chilankhulo, machitidwe ena ofalisira

akuyenera kusinthidwa ndi cholinga chakuti uthenga umveke. Paulo anazindikira ndi kuchita izi

(onani Machitidwe 21:37-40 ndi 22:2). Ndipo 26:18 amapereka njira imene kulumikizana

kwamphamvu kungachitikire palalikira uthenga wabwino kw anthu ndi zikhalidwe zina.

Mulungu anatuma Paulo kwa amitundu…

…Kukawatsegulira maso ao, kuti atembenuke kucokera kumdima, kulinga

kukuunika, ndi kucokera ulamuliro wa Satana kulinga kwa Mulungu, kuti alandire

iwo cikhululukiro ca macimo, ndi colowa mwa iwo akuyeretsedwa ndi cikhulupiriro

ca mwa Ine (Machitidwe 26:18).

Uthenga ukuyenera kuperekedwa mu njira yotha:

1. Kutsekula maso a anthu.

Page 117: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

117

2. Kuti atuluke mu mdima wa uzimu kulowa mu kuunika.

3. Kuti achoke ku mphamvu ya Satana mkupita kwa Mulungu.

4. Kuti alandire chikhululukiro cha machimo awo polandira chipulumutso.

5. Kuti alandire cholowa cha uzimu mwa chiyeretso cha chikhulupiriro.

Chikhalidwe chimene munthu wakhalamo chimalosera zinthu zisanu mmadera awa:

Chilankhulo chake: mmene amalankhulira ndi kulumikizana maganizo ake.

Maonedwe ake a dziko: mmene amalionera ndi kulimvetsa dzikoli.

Zikhulupiriro zake: chipembedzo mu za mphamvu za uzimu, njira ndi maganizo ake.

Zimene amayendera: makhalidwe ake ndi anthu ena, zilimbikitso ndi njira za mmene

amapangira ziganizo.

Makhalidwe ake: mmene amachitira, amakhalira, makhalidwe a zikhalidwe zawo

zoyenera.

Machitidwe 26:18 amakambapo za izi, mukhoza kuwerenga. Pali nkhani ya chiyankhulo,

maonedwe a dziko, zikhulupiriro ndi kusintha kwa makhalidwe.

KUONETSERA MPHAMVU

Paulo sanangolankhula za uthenga wabwino ayi, komanso amaonetsera mphamvu ya Mulungu:

Mu mphamvu ya zizindikilo ndi zozizwitsa, mu mphamvu ya Mzimu Woyera;

kotero kuti ine kuyambira ku Yerusalemu ndi kuzungulirako kufikira ku Iluriko,

ndinakwanitsa Uthenga Wabwino wa Kristu (Aroma 15:19)

KUDZALA MIPINGO:

Paulo sanangofalitsa uthenga wabwino keneko ndi kuwasiya okha obadwa mwatsopano.

Amapanga gulu la okhulupirira amene otembenuka mtima amakhala nawo. Amadzala mipingo

mmadera.

1. Ogwira ntchito atumidwa: Machitidwe 13:1-4; 15:39-40

Ogwira ntchito amaphunzitsaidwa ndi kutumidwa kukafika mmadera ena. Okhulupirira a

mmipingo ya pakhomo amathandiza, kutuma, ndi kuyanjana ndi iwo amene Mulungu

anawapatulira ku ntchito.

2. Anthu analumikizana: Machitidwe 13:14-16; 14:1; 16:13-15

Mmadera ambiri, Paulo anayetsetsa kulumikizana ndi atsogoleri a mu sunagoge. Anayesera

kukhala ndi chidziwitso ndi thandizo la atsogoleri a pamalo. Magulu komanso anthu anatsata

zolinga zokhala ndi gulu la anthu ambiri omvera uthenga wabwino.

3. Uthenga unaperekedwa: Machitidwe 13:17; 16:31

Page 118: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

118

Uthenga unaperekedwa mu ulaliki, chiphunzitso, kuchitira umboni ndi kuonetsera mphamvu ya

Mulungu. Njira zosiyana zinagwira ntchito molingana ndi mmene zinalili pofuna kulupereka

uthenga kwa anthu. Mmadera ena amalalikira mu sunagoge (Machitidwe 14:1). Pomwe ena,

anthu amene amalandira amaikidwa mmagulu ena apadera (Machitidwe 19:9). Mautumiki

osiyana kwa anthu amachitika mmadera ena (Machitidwe 13:42) ndipo chilankhulo

chimasinthidwa ponetsetsa kuti uthenga ukuperekedwa moyenera (Machitidwe 22:2).

4. Omvera amatembenuka: Machitidwe 13:48; 16:14-15

Kulumikizana bwino kwa uthenga wabwino kunachokera mu kutembenuka, ndi anthu amene

amalandira uthenga wa chipulumutso ndi kulapa kwa machimo awo.

5. Okhulupirira anasonkhana: Machitidwe 13:43

Paulo sanasite ulaliki ndi kutembenuza anthu. Amawasonkhanitsa okhulupirira kukhala pa

mpingo wad era. Okhulupirirawa amakhala mu thupi la chiyanjano ndi mwambo wa mpingo.

Nthawi komanso malo zimayikidwa zoti azisonkhana pamodzi ngati mpingo.

6. Chikhulupiriro chitsimikizidwa: Machitidwe 14:21, 22; 15:41

Monga zaonetsedwa pa kutuma kwakukulu mu Machitidwe 28:19-20, chiphunzitso chimatsatira

kutembenuka mtima. Chiphunzitso ichi, molingana ndi mpingo chinaumba okhulupirirawa pa

maziko a moyo wawo wa chikhristu mu ufumu wa Mulungu. Zokhuza “chitsimikizo cha

chikhulupiriro” zimalimbikitsa kukula mmoyo wauzimu, ndi kuthandiza okhulupirira kuzindikira

mphatso zawo za uzimu ndi kukhala ziwalo zamphamvu mu thupi la Khristu.

7. Atsogoleri apatulidwa: Machitidwe 14:23

Ngati okhulupirira okhwima, atsogoleri omwe akulitsidwa ndi Mulungu amayenerezedwa pa

utumiki wotsogolera mu mpingo. Akukuakulu anasankhidwa ku mpingo womwe amasonkhana

osti kutumizidwa kuchokra ku mpingo wina kapena ku dziko lina. Mpingo uliwonse umakhala

ndi madongosolo a kayendetsedwe ka mpingo kochokera Mbaibulo, kabwino ndi koyenera.

8. Mpingo unayamikiridwa: Machitidwe 14:23; 16:40

Pamene atsogoleri ali pamalo ndi kuyamba kugwira ntchito moyenera, kudalira “odzala mpingo”

kumatha. Pakuti kusintha koyenera kunachitika kuchokera ku likulu la mpingo kupita ku mpingo

watsopano. Mpingo “unayamikidwa” pochita bwino kwawo ngati thupi lokhulupirira.

9. Maubale anapitilira: Machitidwe 15:36; 18:23

Ubale unapitilira pakati pa okhulupirira ndi odzala mpingo (Paulo) ndi likulu la mpingo

(Yerusalemu). Maubalewa amakhazikikanso pakati pa chiyanjano chatsopano cha iwo ndi

mipingo ina mmadera ndi cholinga chofuna kufalitsa uthenga.

MASOMPHENYA A DZIKO LONSE:

Page 119: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

119

Paulo anali ndi dongosolo la lenileni la machitidwe ake. Baibulo limaulula kuti anali ndi chidwi

ku mAsiya, Galatiya, Makedoniya ndi ena amene anali ndi mmadera amenewo nthawi imeneyo:

Filipo: (Machitidwe 16) uwu unali mzinda wotsogolera ku Makedoniya.

Tesalonika: (Machitidwe17:1-10) uwu unali waukulu ndi wachumua.

Akorinto: (Machitidwe18:1-11) wa chuma wa Metulopolisi ku Helene.

Aefeso: (Machitidwe 19:1-10) kumene misewu yaikulu ya ufumu wa Chiroma unadutsa

kummawa. Madoko komanso malo a malonda.

Paulo anadziwa kutiangathe kufikira anthu ambiri mu mizinda. Anadziwanso kuti kusintha

kumayamba mu mzinda kenako ku malo akumudzi.

Mizinda ya malondayi ndi malo okopa alendo inali ndi anthu ambiri amalonda ndi zolinga zina.

Moti alendo amamva nawo uthenga wabwino pamene amapita kwawo. Paulo anayendera

mizinda mkukhazikitsa ntchito ua umishoni. Pamene amachoka ku Yerusalemu, anapita kudera

lina ku Tarisi ndi Antiokeya. Werengani mavesi awa: Machitidwe 11:25-30; 13:1-3; 19:1-20;

16:8; 19:21; 23:11; 28:14-31. Aroma 1:9-15; 15:24, 28).

MALO OLANDILIKA:

Njira za Paulo zokulitsa mpingo zinachitika chifukwa cha anthu amene amalandira uthenga wa

Paulo. Ku Mateyu 10, Yesu anawauza ophunzira ake kuti asapite ku Samariya kapena kwa anthu

a mitundu koma kwa Israyeli. Nthawiyi inali ya bwino koma kwa ana a Israyeli. Magulu ena a

anthu sinali nthawi yawo yolandira uthenga.

Ngakhale pakati pa Ayuda, ophunzira amayenera kulalikira kwa iwo amene akanalandira

uthenga. Amayenera kugawira iwo amene amalandira ndi kuchitabe choncho ngakhale

amakumana ndi osalandira uthenga. Amayenera apereke mphamvu zawo kwa madera amene

amalandira uthenga.

Paulo anatsata ndithu njira imeneyi. pamene ayuda amakana uthenga wabwino, Paulo amapita

kwa amitundu (Machitidwe 13:42-51). Pamene Atene sanakonzeke, Paulo amapita Kwa

Akorinto. Ndipo ku Akorinto Paulo anachoka kwa ayuda ndi amitundu. A Helene amene

amalandira uthenga anakondwera ndikubatizidwa atakhulupirira (Machitidwe 18:5-11). Mulungu

anavomereza ntchito ya Paulo mmasomphenya pomuuza kuti akhalebe ku Akorinto opanda

mantha ndi kulalikira Khristu (Machitidwe 18:5-11). Pamene mikumano ikuchitika

mmasunagoge mkuamamukana iye, Paulo anayamba mipingo imene imalandira mauthenga ake.

Pamene chizunzo chimamutulutsa kunja, amapita ku madera ena.

ANTHU AKE:

Paulo amaika chidwi pofikira anthu a mtundu wake ndi uthenga wabwino:

Page 120: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

120

Abale, kufunitsa kwa mtima wanga ndi pemphero langa limene ndiwapempherera

kwa Mulungu, ndilo, kuti apulumuke (Aroma 10:1).

ANTHU OSAFIKILIDWA:

Paulo anasankha madera amene uthenga wa Khristu sunafikeko:

Ndipo cotero ndinaciyesa cinthu caulemu kulalikira Uthenga Wabwino, pa malopo

Kristu asanachulldwe kale, kuti ndisamange nyumba pa maziko a munthu wina.

Koma monga kwalembedwa; Iwo amene uthenga wace sunawafikire, adzaona,

Ndipo iwo amene sanamve, adzadziwitsa (Aroma 15:20-21)

MAGULU A ANTHU

Paulo anagwira ntchito ndi magulu a anthu mkati mzinda ndi madera. Mwachitsanzo, analalikira

kwa Ahelene ndi ayuda ku Antiyokeya (Machitidwe 13:42). Gulu la anthu linali la mtundu wa

chikhalidwe, chiyankhulo chofanana. Ndi kofunikira kumaona mudzi kapena mzinda mu magulu

a zikhalidwe zawo ndi kupanga dongosolo la kukulitsa mu kulumikiza.

Mwachitsanzo, mzinda umodzi ku Amerika muli anthu ambiri olankhula chi spanishi, chingerezi

ndi chimwenye. Kukula pa kulumikiza kumanga mipingo mu mizinda imeneyi muyenera kuona

magulu onse a anthuwa. Kudala mipingo mkati mwa anthu a magulu osiyana kumapititsa

uthenga wabwino patsogolo. Pakuti anthu a maguluwa amalnkhula zilankhulo zosiyana ndipo

ndi a zikhalidwe zosiyananso. Choncho palibe chimene chingatchinge uthenga wabwino kaya

zilankhulo kapena zikhalidwe. Mu phunziro latha mwaphunzira kuti anthu amene amakhala

limodzi, amalamkhula zilankhulo zofanana ndipo ali ndi zikhalidwe zofanana.

Anthu amene ali ngati ife, akhoza kugawidwa mkukhala mmagulu a ang’ono ndi cholinga

chofalitsa uthenga. Mwachitsanzo, mumachita izi pokhala ndi magulu a maphunziro a sunde

sukulu molingana ndi zaka zawo. Mukhonzanso kuchita izi pamene mukufuna kufikira anthu

amabiri a mmagulu.

Harvestime international Institute ali ndi phunziro la “Kuzindikira Malo” limene limathandiza

kudziwa malo ofunika pa utumuki. Taganiza kuti mukhale ndi phunziroli pa kudzala mpingo.

Phunziroli likuthandizani mmalo:

1. Kudziwa anthu amene mukawafikire. Ndi anthu amagulu ati osiyana amene

mukawafikire mmizinda kapena mmadera. Ndi ndani amene mukufuna kukafikra?

Zipembedzo zawo, zikhalidwe ndi zilankhulo zawo.

2. Kudzindikira zosowa zawo za ku uzimu. Mwachitsanzo, kodi mkofunika kudzala mpingo

pakati pa anthu a chilankhulo cha chisena. Mwina zosowa zawo zikutumikiridwa koma

amene amalankhula zilankhulo zina sakuthandizidwa.

Page 121: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

121

3. Kudziwa kulandilidwa kwa uthenga wabwino:

4. Kudziwa njira zimene mukagwiritse ntchito pofikira anthu onse. Kodi afikilidwa bwanji?

Nanga ndi ndani amene afikire? Mukuyenera kuwafikira monse mmene angamvere ndi

kumvetsetsa mwa zikhalidwe zawo. Mwachtsanzo, ngati gulu lina silingawerenge,

kulalikira kowapatsa zowerenga sikungawathandize powafikira ndi uthenga.

KUFUNA KUSINTHA MALINGANA NDI ZIKHALIDWE:

Paulo anafunitsitsa kusintha kwa anthu osiyana zikhalidwe ndi muteso mmadera (onani I

Akorinto 9:16-23). Munthu amasunthika ndi chikhalidwe chimene wakulilamo. Anthu a

zikhalidwe zosiyana amasiyananso mu zochita.

KUSIYANA KWA ZIKHALIDWE

Paulo sanagofuna kusintha pa zikhalidwe zokha ayi, koma sanalole kuti uthenga wabwino

utchingidwe ndi zikhalidwe.

Ku maiko a aluya, ngati wokhulupirira watsopano afuna kusiya mpingo wa pabanja lake

chifukwa cha chikhulupiriro chake, amakhala limodzi ndi anthu ofanana naye chikhulupiriro mu

mpingo. Onse amalankhula chiyankhulo chimodzi ndi kukhala ndi makhalidwe amodzi. Koma

ku maiko ena kumene chikhristu chimati munthu ayenera kusiya chikhalidwe chake ndi kuyamba

kukhala ndi achikhulupiriro chimodzi, uthenga wabwino umafalikira mochedwa. Zikhalidwe

zina zimalemekezedwa kuposa za anthu ena. Mitundu, zikhalidwe zonsezi ndi zofunikira

kwambiri.

Mu Chipangano Chatsopano, pamene munthu wakhala khristu sizimatanthauza kuti wasiya

kukhala mu wosatira chi Yuda. Ngakhale wamitundu sayenera kulandira mdulidwe wa chiyuda.

Komayambiriro kunali mavuto pa ayuda amene amaika lamulo pa amitundu polalola kuti

azidulidwa ngati atembenuka mtima. Koma Paulo ananena kuti ameneyu anali katundu

wosayenera kusenza. Mukhoza kuwerenga za izi pa Machitidwe 15.

(Chidziwitso: tikamakamba za “chikhalidwe” timakamba za makhalalidwe osiyana potengera

zikhalidwe za anthu ndi mtundu zimene sizimaphwanya malamulo a Mulungu. Machitidwe a

uchimo samaloledwa.

NTHAWI:

Paulo amasinthanso nthawi imene amakhala nawo mu zikhalidwe za anthu malingana ndi

zosowa zawo. Mmalo ena amakhalamo masiku ochepa. Onani Machitidwe 21:4. Ndipo malo ena

amakhalako nthawi yaitali, onani Machitidwe 14:28. Anali woyendayenda ndipo dongosolo lake

limatsogozedwa ndi Mzimu Woyera.

KULANKHULA KWA ANTHU AMBIRI:

Page 122: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

122

Paulo amalankhula uthenga wake kwa anthu ambiri. Anagwiritsa ntchito mwayi wolankhula kwa

anthu ambiri:

Ndipo kunali pa Ikoniyo kuti analowa pamodzi m'sunagoge wa Ayuda, nalankhula

kotero, kuti khamu lalikuru la Ayuda ndi Ahelene anakhulupira (Machitidwe 14:1)

KUKHALA WOPHUNZIRA:

Paulo analalikira ku khamu la anthu komanso amadziwa kufunika kopereka moyo wake kwa

anthu ochepa amene anli ofunika okhala ndi kuthekera kophunzitsa ena. Timoteo anali mmodzi

wa anthuwa komanso Tito ndi Yohane Marko, amene nthawi ina anakanidwa pa maphunziro a

kukhala wophunzira (Machitidwe 15:36-40). Anali Paulo amene Mzimu Woyera anamuulira

zolinga za Mulungu pa wokhulupirira onse kuti achulukane mu uzimu (II Timoteo 2:2).

Kugwira ntchito limodzi ndi okhulupirira ena monga Banabasi ndi Sila, ndi ophunzira ena amene

anawaphunzitsa, kunachulukitsa utumiki wa Paulo mtumwi. Pa ulendo wake wachiwiri ndi

wachitatu, Paulo anlemba za thandizo la amene anagwira nawo ntchito limodzi amene anli mzika

za madera awo kumene anakonza kuti agwireko ntchito.

Iyi ndi mfundo yaikulu. Anthu a ku afilika akhoza kufikira anzawo a ku Afilika momwenso

anthu a mitundu ina. Chifukwa amalankhula chilankhulo chofanana, komanso zikhalidwe zawo

zofanana.

MIPINGO YOIMA PAWOKHA:

Paulo anadzala mipingo yoima pawokha. Ngakhale inali pa ubale ndi likulu la mpingowo

kumbali ya chiyanjano chawo ndi utsogoleri, simadalira mpingo waukulu. Paulo samatenga

thandizo la umishoni kapena iwo kuonetsa kuti Paulo antengako thandizo lopita ku mipingo ina

ya zikhalidwe zina. Amapeza yekha thandizo la mipingo imene amadzala imene inalinso

yokonzeka kuima payokha posadalira thandizo la kwina.

Nkhani zonse za chuma zothandizira kukula kwa mpingo zikuyenera kupanga anthu kuti

azizilamulira okha. Ngati mpingo ulandira thandizo kuchokera ku mipingo ina, ndiye kuti

mpingowo ukudalira amenewo. Ngati mpingo wothandizawo walephera, ndiye kuti mpingo

umene ukudalirawo udzalepheranso. Ngati ubale wa maiko suli bwino, mpingo udzakumana ndi

mavuto ngati thandizo lasiya kubwera.

Ambuye yemweyo amene anasandutsa madzi kukhala vinyo ndi kuchulukitsa mkate ndi nsomba

zimene anadyetsa khamu la anthu ndi wokuthanso kubweretsa chuma chofunikira kufalisira

uthenga.

Ulamuliro wogwiritsa ntchito mphatso za mzimu ukyenera kupatsidwa ku mpingo watsopano

kamodzi ndi utsogoleri umene ulipo pa mpingo watsopano. Pamene Paulo anasankha akulu a

mpingo, anasankhidwa kuchokera pakati pa anthu osati kuchokera kwina kwake.

Page 123: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

123

Cifukwa ca ici ndinakusiya iwe m'Krete, kuti ukalongosole zosowa, nukaike akuru

m'midzi yonse, monga ndinakulamulira (Tito 1:5)

Paulo anagwiritsa ntchito mipingo yatsopano mmadera onse amene amapita monga pemphero,

kupereka, ndi ngati ogwira ntchito limodzi okulitsa mpingo mchiwerengero, ndi polumikiza ndi

anthu ena. Onani Machitidwe 20:4, Aefeso 6:19 ndi Afilipi 1:5,7; 4:14-16.

Mpingo uliwonse umene Paulo anadzala unali likulu latsopano la kuchulukana ku uzimu.

Pakuti kuturuka kwa inu kudamveka mau a Ambuye, osati m'Makedoniya ndi

Akaya mokha, komatu m'malo monse cikhulupiriro canu ca kwa Mulungu

cidaturuka; kotero kuti sikufunika kwa ife kulankhula kanthu (I Atesalonika 1:8)

Paulo anadzala mipingo yambiri pa Mau a Mulungu ndi thanthwe, Yesu Khristu. Sanaikhazikitse

pa bungwe kapena mpingo kapena umunthu wake. Kubweretsa kudalira sikumaphunzitsa kuima

pawekha.

Page 124: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

124

MAYESO ODZIYETSA NOKHA

1. Lembani Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

2. Lembani tanthauzo la mawu oti “kukula kwa mpingo kolumikiza”

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

__________________________________________________________________________

3. Tchulani vesi imene imakamba za dongosolo la Khristu la “kukulitsa mpingo

polumikiza”

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

4. Ndi ndani amene anali mtsogoleri mu Chipangano Chatsopano pa “kukulitsa mpingo

polumikiza” kwa amitundu?

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

5. Lembani chidule cha njira zimene Paulo angwiritsa ntchito pofalitsa uthenga wabwino

kwa anthu a zikhalidwe zina.

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

(Mayankho a mafunsowa akupezeka kumapeto kwenikweni kwa bukuli)

Page 125: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

125

KUPITILIZA KUPHUNZIRA

1. Mpingo wa ku Antiokeya unadzalidwa ndi mpingo wa ku Yerusalemu. Chitatha chizunzo

cha Stefano, okhulupirira ambiri anathawa ku Yerusalemu. Ena anabwera ku mzinda wa

Antiokeya ku Siriya, mzinda waukulu ku ufumu wa Chiroma. Kumeneko anakakhazikitsa

mpingo (Machitidwe 11:19-21).

Ophunzira kwa nthawi yoyamba anatchedwa akhristu ku Antiokeya. Uwu unali mpingo

woyamba kwa anthu amene sanali ayuda koma anli pd chiyanjano chabwino. Aheleni

amitundu ndiwo amene anali mu mpingowo. Antiokeya unakhalano mzinda waukulu wa

mipingo ya Chipangano Chatsopano. Utumiki umene tili nawo pano umachokera ku

Antiokeya, osati ku Yerusalemu kumene anthu ake anali a chikhalidwe cha chiyuda basi.

2. Kufala kwa uthenga wabwino kwa Paulo mu zikhalidwe za anthu ena chidule chake ndi

ichi mu maulendo wake wachitatu wa umishoni:

Ulendo woyamba: Machitidwe 13:1-14:28

Ulendo wachiwiri: Machitidwe 15:36-18:22

Ulendo wachitatu: Machitidwe 18:23-21:14

3. Werengani umboni wa Paulo mu Machitidwe 22:

Asanatembenukire kwa Khristu: Machitidwe 22:3-5

Kutembenuka mtima: Machitidwe 22:6-11

Utumiki wake: Machitidwe 22:12-16

Ntchito yake ya umishoni: Machitidwe 22:17-21

4. Werengani zambiri zokhuza Paulo mmene anayendera ulendo wake ku Aefeso:

Anthu anakumana: Machitidwe 18:19; 19:1,8,9

Uthenga wabwino unaperekedwa: Machitidwe 19:4,9,10

Omvera anatembenuka: Machitidwe 19:5,18

Okhulupirira anasonhkana: Machitidwe 19:9-10

Chikhulupiriro chinatsimikizidwa: Machitidwe 20:20, 27

Atsogoleri anapatulidwa: Machitidwe 20:17,28: I Timoteo 1:3,4;

Mpingo unayamikidwa: Machitidwe 20:17; Aefeso 1:1-3,15,16

5. Kodi kukula kwa mpingo polumikiza mu chipangano chatsopano kumachita bwino?

Onetsetsani izi:

… Ndipo panakhala cimwemwe cacikuru m'mudzimo (Samariya): Machitidwe 8:8

… Ndipo anamuona iye onse akukhala ku Luda ndi ku Sarona, natembenukira kwa

Ambuye amenewa: Machitidwe 9:35

… Koma mau a Mulungu anakula, nacurukitsa (Machitidwe 12:24).

Page 126: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

126

… Ndipo mau a Ambuye anabukitsidwa m'dziko lonse (Machitidwe 13:49)

… Kotero Mipingoyo inalimbikitsidwa m'cikhulupiriro, nacuruka m'ciwerengo cao tsiku

ndi tsiku (Machitidwe 16:5)

… Ndipo anacita comweco zaka ziwiri; kotero kuti onseakukhala m'Asiya anamva mau a

Ambuye, Ayuda ndi Ahelene (Machitidwe 19:10)

…Cotero mau a Ambuye anacuruka mwamphamvu nalakika (Machitidwe 19:20)

…mu mphamvu ya zizindikilo ndi zozizwitsa, mu mphamvu ya Mzimu Woyera; kotero

kuti ine kuyambira ku Yerusalemu ndi kuzungulirako kufikira ku Iluriko, ndinakwanitsa

Uthenga Wabwino wa Kristu; ndipo cotero ndinaciyesa cinthu caulemu kulalikira

Uthenga Wabwino, pa malopo Kristu asanachulldwe kale, kuti ndisamange nyumba pa

maziko a munthu wina (Aroma 15:19)

6. Muyeso wa anthu ndi malo a anthu amene anatembenuka mtima amaonetsera za mmene

mpingo wa chipangano chatsopano unalumikizana mmagulu, muzikhalidwe, ndi

mmadera ndi uthenga wabwino.

Page 127: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

127

CHAPUTALA CHA 10

ZISANKHO KAPENA OPHUNZIRA?

ZOLINGA:

Pakutha pa chaputalachi muyenera:

Kulemba Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

Kupereka tanthauza la “kutembenuka.”

Kupereka tanthauzo la “wophunzira.”

Kulemba zinthu zitatu zofunika pa kukhala wophunzira.

Kudziwa mfundo 9 za kukhala wophunzira zimene zikuonetseredwa pa Yesu ndi

ophunzira ake.

Kulemba zinthu 9 za kukhala wophunzira weniweni.

Longosolani yesero lenileni la wophunzira.

VESI LOTSOGOLERA:

Pomwepo Yesu anati kwa ophunzira ace, Ngati munthu afuna kudza pambuyo

panga, adzikane yekha, natenge mtanda wace, nanditsate Ine (Mateyu 16:24)

MAWU OYAMBA

Mwamvapo zambiri za nkhani ya “Kutuma Kwakukulu” kwa Yesu, koma kodi mumamvetsa

zenizeni za umishoni umene Yesu anapatsa ophunzira ake? Kodi lamulo linali longokhala ndi

anthu atsopano? Kodi anawatsimikizira kuti atha kupanga maulendo mmizinda ndi kumanga

mipingo yaikulu? Kodi anawauza za zinthu zofunikira monga chakudya ndi zovala za a

umphawi?

Tiyeni tiwerengenso malangizowa kachiwiri:

Cifukwa cace mukani, phunzitsani anthu a mitundu yonse, ndi kuwabatiza iwo

m'dzina la Atate, ndi la Mwana, ndi la Mzimu Woyera:

ndi kuwaphunzitsa, asunge zinthu zonse zimene ndinakulamulirani inu; ndipo

onani, Ine ndiri pamodzi ndi inu masiku onse, kufikira cimariziro ca nthawi ya

pansi pano (Mateyu 28:19-20)

koyambirira kupita kunali kwa amitundu yonse, kuwaphunzitsa uthenga wabwino ndi

kuwabatiza ndi kukhala nawo pa ziphunzitso a zimene Yesu analamulira.

Page 128: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

128

Ichi chinali choyamba ndi chofunikira. Mukhoza kukhala moyo wanu mu njira zambiri.

Mukhoza kuchita ntchito zabwino ngati kuthandiza a umphawi. Mukhoza kumanga mipingo

yaikulu. Mukhoza kupanga misonkhano yaikulu ya chipembedzo.

Koma mukuyenera kuchita chinthu chimodzi ngati mukufuna kuwaniritsa zimene Yesu

amanena: Mukuyenera kuchita nawo pofikira dziko lapansi ndi uthenga wabwino. Zinthu zonse

ngati kutumikira osauka, kumanga mipingo ndi zina, ndi zofunika pakuti zingothandizira ku

chofunika chachikulu.

Koma kufikira anthu a mitundu yonse ndi kuposa kulumikiza anthu ku malo a chitsankho cha

Yesu. Pofuna kukwaniritsa kutuma kwakukuluku mukuyenera kupita chitsogolo kupitilira

kukhala wophunzira.

CHISANKHO KAPENA WOPHUNZIRA?

Mitundu iwiri ya ziphunzitso ikupezeka pa kutuma kwakukula kwa Yesu:

KOYAMBA: KUPHUNZITSA ANTHU KUTI APULUMUTSIDWE

Anthu akuyenera kumva Mau a Mulungu ndi cholinga choti achitepo kanthu, kulapa ku machimo

ndi kubadwa mwatsopano. Chipunzitso chimenechi ndi “uvangeli”:

Cifukwa cace mukani, phunzitsani anthu a mitundu yonse, ndi kuwabatiza iwo

m'dzina la Atate, ndi la Mwana, ndi la Mzimu Woyera (Mateyu 28:19).

Okhulupirira atsopano nthawi zina amatchedwa “otembenuka mtima.” Munthu wotembenuka ndi

wokhulupirira mwa Yesu amene wabadwa mwatsopano mwa chikhulupiriro ndi kukhala gawo

limodzi la Ufumu wa Mulungu. (Harvestime International Institute ali ndi phunziro lotchedwa

“Chotupitsa ngati Ulaliki” limene limapereka maphunziro a ulaliki kwa anthu amene ndi

atsopano mu chikhulupiriro.

CHACHIWIRI: CHIPHUNZITSO PAMBUYO PA KUTEMBENUKA:

Mutatha kupnzitsidwa za Uthnega Wabwino ndipo mwabwera kwa Yesu, mukuyenera

kuphunzira za mmene mungamutsatire Iye.

Ndi kuwaphunzitsa, asunge zinthu zonse zimene ndinakulamulirani inu; ndipo

onani, Ine ndiri pamodzi ndi inu masiku onse, kufikira cimariziro ca nthawi ya

pansi pano (Mateyu 28:19-20)

Kutumwa kwa Yesu kumaulula kuti chiphunzitso chopitilira chimayenera kubwera munthu

atatha kutembenuka ndi kubatizidwa. Obadwa mwatsopano akuyenera kulangizidwa mmene

Yesu anaphunzitsira. Ntchito imeneyi imatchedwa “kuyendera anthu” kapena “kudyetsa nkhosa”

kapena “kupanga ophunzira.”

Page 129: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

129

TANTHAUZO LA KUPANGA OPHUNZIRA

Dongosolo la Yesu ndi lokuti mutsogolere otembenuka mtima kukhala ophunzira.

Wophunzirandiye amene watembenuka ndi kukhazikika pa maziko a chikhulupiriro cha

chikhristu ndi kuthekera kupanganso ophunzira ena ndi kuwatsogolera. Mawu oti “wophunzira”

ndiye kuti mwana, amene ali ku sukulu, amene amaphunzira potsatira. Zikuposa mzeru za

mmutu. Uku ndi kuphunzira kumene kumasintha makhalidwe a munthu.

CHISANKHO CHA WOPHUNZIRA

Chisankho ndi gawo lokhalo loyamba pa kukhala wophunzire woona. Otembenuka mtima

ayenera kupita chitsogolo pa chisankho chawo chokhala ziwalo za thupi la Yesu zokonzeka

kupanganso ophunzira ena. Kupeza ophunzira ena ndi zofunikira, koma kuwaphunzitsa kutsatira

ndi kukhala okhwima ku uzimu ndiye zofunikanso. Aliyense amene mukumphunzitsa,

mumpange kuti akhalale wophunzira weniweni kuti nayenso aphunzitse ena.

Ili ndi dongosolo la Mbaibulo la kukhala wophunzira molingana ndi mmene Yesu

anaphunzitsira. Anasankha ophunzira khumi ndi awiri, nawaphunzitsa kuti nawonso aphunzitse

ena. Pamene mukuphunzira chaputala cha 4 cha phunziro ili, dongosolo loti “aliyense

aphunzitse” limabweretsa kukulukana kwa okhulupirira, mipingo komanso zipembedzo.

Koma nthawi zonse dziwani zolinga zanu bwino. Sikuti mukuphunzitsa ndi cholinga chopanga

utumiki wanu kapena mpingo wanu. Cholinga ndi chakuti mufikire anthu a mitundu yonse

molingana ndi Yesu. Kukwaniritsa kutuma kwakukulu sikukutengera mzeru kapena luso

lapadera, komano pa kuumba ndi kudzipereka kwa ophunzira.

Ulaliki umabweretsa anthu kutembenuka mtima. Kupereka mwambo kumapanga ophunzira

amene akhoza kulalikira, ndi kutembenuza anthu ndi kuwapanga kukhala ophunzira. Ndipo izi

zimapitilira chonchi.

KUKHALA WOPHUNZIRA

Werengani Luka 9:57-62 mu Baibulo lanu. Mu ndimeyi anthu atatu anampeza Yesu ndi khumbo

lofuna kukhala ophunzira. Kwa yense, Yesu anaulula machitidwe osiyana okhala wophunzira

kuti amafuna:

1. KUWERENGERA MTENGO: Luka 9:57-58

Munthu woyamba akanamtsata Yesu opandapo kudikira kuti ayitanidwe. Anayesera kukhala

wophunzira mwakufuna kwa iye yekha. Koma Yesu anamuchenjeza kuti samvetsa bwino

tanthauzo la kukhala wophunzira. Kukhala wophunzira sikuti munthu umangozifunitsa kwa

Mulungu ayi, koma ndi maitanidwe a kwa Mulungu. Yesu anaati, “ukanditsata ine, izi ndi

zimene udzakumana nazo.” Analongosola kuti kukhala wophunzira umalipira mtengo wake.

Sizingakwaniritsidwe ndi kuchita mwa iwe wekha.

Page 130: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

130

2. KUCHITA ZOYENERA: Luka 9:59-60

Munthu wachiwiri amene anaitanidwa ndi Yesu kuti “amutsate.” Ku “mutsata” ndiye kuti

kubwera pambuyo pa wina amene ali patsogolo, kutsatira chitsanzo. Zimakhuza zomwe

umakhulupirira ndi kumvera. Pamene Yesu anaitana ophunzira ake 12, anawapempha kuti

amutsatire ndi kumutsata. Sanalongosole za mmene njira yake inalili. Sanawapatse tsatanetsatane

wa dongosolo la moyo.

Ophunzira akuyenera kusiya moyo wakale mbuyo chifukwa cha maitanidwe okha basi.

Zosankho ndi nsembe zimene izi zimatengera sizidziwika. Wotsatirayo amasiya moyo

wachitetezo ndi kukhala moyo wonga ngati wopanda chitetezo mmaso a dziko. Sikukhala

kudzipereka ku dongosolo koma kwa munthuyo. Munthuyo ndiye Yesu Khristu.

Mu ndime ya Luka, mmene munthuyu anayankhira ku maitanidwe omtsata Yesu anali “uyambe

wavutikira ine kaye…” amafuna kumutsata Yesu, koma sichinali chinthu choyamba pa moyo

wake. Yesu sanaganizirepo kuti wotsatira wa iye adzakana zosowa za makolo ake (onani Yohane

19:25-27). Ndi nkhani ya zinthu zoyamba zimene ndi zofunika mu nkhaniyi. Munthuyi amafuna

kukaika makolo ake koyamba. Mu nthawi yofunikira iyi ndi pamene Yesu anamuitana kuti

amutsatire iye, pasapezeke chinachake chotchinga maitanidwe usanayankhe.

Mu ndime ina Yesu analongosola mwachindunji pa nkhani ya “kutsatira” imene imafuna:

Pomwepo Yesu anati kwa ophunzira ace, Ngati munthu afuna kudza pambuyo

panga, adzikane yekha, natenge mtanda wace, nanditsate Ine (Mateyu 16:24).

Kudzikana wekha kukuyenera kukhala koyamba usanayambe kunyamula mtanda. Makhalidwe

akale ndi a uchimo akanidwe. (werengani Aroma 7-8 mmene Paulo anavutikira ndi moyo wake).

Keneko motha kutenga mtanda. Mtanda ndi chizindikiro cha nsembe, kuwawa, kukanidwa,

mavuto, chitonzo pochita chifuniro cha Mulungu. Mtanda ukhoza kukhalanso maitanidwe a kufa

chifukwa cha dzina la Khristu.

“kusenza mtanda sizimakamba za zomelera za moyo. Izi ndi za kwa anthu onse. Pakuti ndi

ziphinjo, mayesero, kukhumudwa, kuwawadwa chifukwa cha moyo wochimwa wa mdziko.

Wokhulupirira sanaikidwe kunja kwa zowawazi. Nayenso amamva kuwawa, amadwala,

kukumana ndi ngozi, moto, zopsa za dziko chifukwa cha uchimo. Koma zowawazi sizimatenga

mtanda. Kunyamula mtanda ndi kuchokera mu kufuna kwa munthu osti zokakamizidwa ndi

zophinja za dziko ayi. Ndipo ndi zopitilira (tsiku ndi tsiku) kusankha kudzikana ku zokhuma za

thupi ndi cholinga chomvera Mulungu.

Kunyamula mtanda ndi kofunikira pa kukhala wophunzira. Yesu anati, “Aliyense amene

sanyamula mtanda ndi kunditsata sayenera ine.” Kunyamula mtanda sikosangalasa chifukwa ndi

nkhani yodzikaniza. Koma ikuyenera kuchitika mwa ufulu chifukwa cha Yesu ndi cholinga

chofuna kukhala wophunzira. Kunyamula mtanda, kukupangiseni kusiya zonse za dziko lapansi.

Ngati mtima wanu uli pa ndalama ndi zinthu zina, ndiye kuti mwachulukidwa kuti

simungatengenso mtanda. Ngati nthawi yanu imatha ndi zinthu za dziko lapansi ndi za thupi,

ndiye kuti manja anu alemedwa sangatengenso mtanda. Mutatha kudzikana nokha ndi kutenga

Page 131: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

131

mtanda, chotstira ndiko kumutsata. Mukuyenera kusiya zonse za moyo wakale ndi maubale a

kale a uchimo.

Izi sizitanthauza kuti wophunzira aliyense asiye ntchito yake ayi mdi nymba yake. Koma

akutanthauza kusintha kwa makhalidwe a munthu. Mwa njira ina zikhoza kutanthauza kusiya

nyumba, ntchito kapena okondedwa chifukwa cha uthenga wabwino. Mukuyenera kutsatira

kumene Yesu akutsogolera. Kukhala wophunzira kukuyenera kukhala koyambirira.

ZOLINGA CHENICHENI: Luka 9:61-62

Munthu wachitatu mu buku la Luka 9:757-62 amafuna kumutsata Yesu, koma amafuna kutero

mu njira yake. Kupita kukatsanzika banja lake chinali chodziwika koma Yesu anamiutana kuti

amutsate. Kodi cholinga chenicheni chinali chani mmoyo wake? Kukhala wophunzira kapena

kuchita zinthu zake? Cholinga cha munthuyi chinali chosakhazikika. Amabwerera mbuyo ndi

zomwe amachita kale ndi zatsopano zimene Yesu anamuitanira.

NJIRA NDI UTHENGA WA OPHUNZIRA

Kuitanidwa kukhala wophunzira kumakhuza kutumidwa kuphunzitsa mitundu yonse. Njira ya

ophunzira inali yochitira umboni. Yesu anati, “mudzakhala mboni zanga” Machitidwe 1:8.

Kutsindika sikunali kwambiri pa zimene akadachita mkukhala. Koma zimene zikadakula mu

zimene akanakhala. Kumapeto, otsatira Yesu anadzitenga okha kukhala mboni. Kumapeto a

moyo wake, Paulo anati:

Pamenepo pothandizidwa ndi Mulungu, ndiimirira kufikira lero lino, ndi

kuwacitira umboni ang'ono ndi akuru, posanena kanthu kena koma zimene aneneri

ndi Mose ananenazidzafika; 23kuti Kristu akamve zowawa, kuti iye, woyamba mwa

kuuka kwa akufa, adzalalikira kuunika kwa anthu ndi kwa amitundu (Machitidwe

26:22-23)

Kuchitira umboni kwa ophunzira kunali kulalikira, kuphunzitsa ndi kuonetsera mphamvu ya

Mulungu mwa zozizwa ndi machiritso. Uthenga wa umboni wawo unali uthenga wabwino wa

ufumu wa Mulungu:

Ndipo uthenga uwu wabwino wa Ufumu udzalalikidwa pa dziko lonse lapansi,

ukhale mboni kwa anthu h mitundu yonse; ndipo pomwepo cidzafika cimariziro

(Mateyu 24:14).

Pakuti ndinapereka kwa inu poyamba, cimenenso ndinalandira, kuti Kristuanafera

zoipa zathu, mongamwa malembo; 4ndi kuti anaikidwa; ndi kutianaukitsidwa tsiku

lacitatu, monga mwa malembo (I Akorinto 15:3-4)

Izi ndi zimene Paulo anazitcha kuti “choonadi cha uthenga wabwino” (Agalatiya 2:5). Uthenga

wina unali wosaloledwa (Agalatiya 1:8).

YESU NDI OPHUNZIRA

Page 132: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

132

Yesu anali ndi ophunzira ake kwa zaka zitatu ndi theka za utumiki wa ntchito imene Mulungu

anamutumira kuti akachite. Imeneyi inali ntchito yapamwamba kwambiri. Amakwanitsa

kuyendera malo ochepa mu nthawinso yochepayo ndi kufikira anthu ochepa.

Kufuna kutsimikiza mathero a ntchito yake, Yesu anapanga ophunzira ngati chofunikira

kwambiri. Amadziwa kuti ophunzira ake adzapanga ophunzira ena ndi kufikira anthu ambir ku

midzi ndi mizinda imene Yesu sanakhale ndi mwayi ofikako.

Yesu akanakhala ndi nthawi yonse yodyetsa ndi kuveka osauka. Akanamanga mpingo waukulu

ku Yerusalemu. Panali njira zambiri zimene akanatha kugwiritsa ntchito ntchito. Koma Yesu

anasankha mafungulo aakulu a kuchulukana ku uzimu. Anadziwa kuti kuika moyo wake mwa

okhulupirika ochepa ulendo wochulukitsa umene sudzatha uyamba. Chidwi chake sichinali

kufikira khamu, koma pa anthu amene anali ndi kuthekera kufikira makamu a anthu.

Sizitengera kuti mukukhala dera liti, khaya muli ku mzinda waukulu, kaya ku midzi yakytali,

munamva uthenga wabwino chifukwa cha kukhulupirika kwa ophunzira a Yesu. Titati tibwerere

mbuyo ku mbiri ya uthenga wabwino, unafalikira mpaka utakupezani, njirayo ndiye kuti

ikanabwerera kumene kunali ophunzira ake.

Yesu ndiye chitsanzo cha ophunzira. Ngati mutsata chitsanzo chake, mudzazindikira kuti

ophunzira woberekana sachokera ku maphunziro a atsogoleri. Yesu anaona kufunikira kwa

kupereka mwambo.

Powerenga ubale wa pakati pa Yesu ndi akuphunzira ake, mfundo zambiri za kukhala ophunzira

zimaonekera. Izi ndi zofunika pa nkhani ya kukhala ophunzira:

1. KUSANKHA:

Kusankhidwa kwa ophunzira 12 kukupezeka pa Mateyu 5:1; 10:2-4; Marko 3:13-19 ndi Luka

6:12-16. Kusankhidwa kwa 70 aja kukupezeka ku Luka 10:1-16. Kusankhaku chinali chinthu

choyamba mu dongosolo lopanga ophunzira. Pamene Yesu anasankha ophunzira, anaitana ngati

anthu wamba. Ena anali osaphunzira ndipo anali ndi zolakwika ndi zolephera.

Zakhala zikunenedwa kuti ngati ophunzira 12 aja anayamba awonedwa kaye ndi mpingo wa

utumwi mu nthawi yathu ino, sakapatsidwa ntchito yotumikira. Koma Yesu anakhazikika pa

kuthekera kwawo osati zoooka zawo. Sanawasankhe chifukwa cha mmene analili koma

chifukwa cha chimene akanakhala. Anayang’ana kutsogolo kupitilira mavuto awo.

Wokhulupirira aliyense ayenera kupatsidwa mwambo ndi wina wake, simungakwanitse kupanga

ophunzira wina aliyense. Ndinu munthu mmodzi yekha ndipo muli ndi malire ku chiwerengero

cha anthu ophunzira amene mungawapange mu nthawi imodzi. Ichi ndi chifukwa chake kupanga

ophunzira kukuyenera kuchitika mmalo amene mpingo wanu ulili. Mbusa aliyense amakhala ndi

chitsimikizo kuti wotembenuka mtima aliyense amaphunzitsidwa ndi okhulupirira okhwima mu

uzimu.

Kodi Yesu anasankha bwanji ophunzira:

Page 133: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

133

Koyamba, podalira ndi Mulungu:

Sindikhoza kucita kanthu kwa Ine ndekha; monga momwe ndimva ndiweruza;

ndipo maweruzidwe anga ali olungama; cifukwa kuti sinditsata cifuniro canga,

koma cifuniro ca Iye ondituma Ine (Yohane 5:30)

Kachiwiri, anapemphera, Luka 6:12-13 amakamba kuti Yesu anapereka nthawi yake yonse usiku

kupemphera asanasankhe ophunzira amene amawafuna.

Kachitatu, Yesu anayamba kuwaitana ophunzira ake. Anthu sadzabera kwa inu kuti mukhale

ophunzira wa Yesu. Mukuyenera kuchitapo kanthu powayitana. Mwa mphamvu ya Mulungu

mukuyenera “kupanga” ophunzira.

Kachinayi, Yesu analongosola za mmene kukhala ophunzira kumakhalira. Monga mwaphunzira,

ophunzira akuyenera awerengere mtengo wake, kuika zoyambirira, ndi kuipanga ntchitoyi

kukhala cholinga chenicheni pa moyo.

Kukhala wophunziranso kumafuna okhulupirika ndi kutha kuphunzitsa ena. Paulo anamuuza

Timoteo kuti asankhe anthu okhulupirika ndi odzipereka ku zinthu zimene anaphunzitsidwa.

Anthu amenewa akuyenera kukhala ndi kuthekera kophunzitsa ena. Zinthu ziwiri izi ndi

zofunika pa kuchulukitsa. Ngati munthu Sali okhulupirika, sangathe kukwaniritsa udindo

wochulukana ku uzimu. Ngati ali wokhulupirira koma sakwanitsa kuphunzitsa, ndiye kuti

adzalephera.

Paulo analankhula za okhulupirira amene akadali ndi kuthekera kophunzitsa ena koma

osakhwima ku uzimu kuti atha kutero. Anthuwa ndiye kuti sanakonzeke kukhala ophunzira

enieni. Akuyenera kulangizidwa mu maziko a chikhulupirio. Kukhala ophunzira kumafuna

“anthu okhulupirika” otha kuphunzitsa enanso.

Anthu okhulupirika sikuti amakhala opanda vuto. Musasokoneze kukhala ophunzira ndi

ungwiro. Musakhazikike pa mavuto a munthu amene akufuna kukhala ophunzira. Muyang’ane

kuthekera kwawo. Kukhala ophunzira kumatenga nthawi kuti munthu akhale “wangwiro” monga

mmene zilili pa Aefeso 4. Ngakhale anthu okhulupirika amakhalanso ndi zofooka zoti athane

nazo monga mmene analili oyamba aja.

Dziko limatenga anthu aluso mkuwapatsa zochita. Amakhazikika pa luko lawo la ntchito.

Mulungu anati kutenga okhulupirika a makhalidwe abwino ndipo amawapatsa maluso a uzimu

ndi kuthekera. Anthu okhulupirika amapezeka kuti akwaniritse cholinga cha Mulungu. Pamene

Yesu anaitana Simoni ndi Andreya, mwachangu anasiya maukonde awo. Mawu oti “mwachangu

amatanthauza kuoezeka kwawo.

Pamene mwasankha anthu oti akhale ophunzira ayenera kupezeka. Amayenera kufuna kupanga

ophunzira ndikukhala choyamba ku moyo wawo. Anthu okhulupirikawa amakhala

olimbikitsidwa ndi masomphenya a uzimu. Pamene Yesu anampatsa Petro ndi Andreya

masomphenya osodza anthu, zinawalimbikitsa kusiya maukonde awo. Anthu okhulupirika

Page 134: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

134

amakhala ndi njala ya Mau a Mulungu, ngati mmene Yesu anachitira ndi ophunzira ake. Mitima

yawo inatekeseka ndi iwo pamene amawagawira Malemba (Luka 24:32,45). Amafuna ndi

kukhumba kuphunzitsidwa.

2. MAGULU:

Pamene Yesu anaitana ophunzira ake, anwaitana kuti akhale ndi Iye. Amakhalira limodzi,

mmautumiki onse komanso mu nyengo zonse. Kukhala ophunzira sikubwera chifukwa cha

misonkhano kapena maphunziro tsiku lolambira. Mukuyenera kukhala pa ubale ndi iwo amene

ndi ophunziranso. Muyenera mugawane nawo moyo wanu ndi iwo.

3. KUDZIPATULA

Kuchokera mu chiyanjano chimene anali nacho ndi Yesu, kudzipatula kunayamba. Yesu

anaitana ophunzira ake kuti adzipatule ku umuthu osati ku mpingo kapena bungwe.

Kudzipatulira kwa Mulungu kumafuna kumvera kwatunthu ku Mau ndi cholinga chake. Onani

Yohane 4:34; 5:30; 15:10; 17:4; and Luka 22:42).

4. MASOMPHENYA:

Yesu anawalimbikitsa ophunzira ake pa kuwapatsa masomphenya a uzimu. Anawaitianira ku

ntchito yaikulu kwambiri kuposa imene iwo amaidziwa mmoyo wawo wa tsiku ndi tsiku.

Anawaitana ophunzira ake kukhala asodzi a anthu (Mateyu 4:19). Anawapatsa masomphenya a

dziko lonse pa zokolola za uzimu (Yohane 4:35). Anawatsimikizira ndi mavumbulutso a ufumu

wa Mulungu (Mateyu 13).

5. MALANGIZO:

Malangizo amene Yesu amawapatsa amagwirizana ndi masomphenya a uzimu. Ngati

wophuznira wa Yesu amayenera kuphunzitsa zimene Yesu anaphunzitsa. Ili ndi gawo limodzi la

kutuma kwakukulu kopezeka pa Mateyu 28:20. Chidwi chikuyenera kukhala pa chiphunzitso cha

Yesu ndipo zimene zimaululika pa ziphunzitsozi zikhale zimene mpingo uyenera kumachita.

Maphunziro a Harvestime International Institute amapereka maphunziro a kukhala wophunzira.

Ndipo ndi chaputala chomalizira pa phunziroli. Komanso ali ndi phunziro limene limatchedwa

“Luso pa Kaphunzitsidwe” limene limakuphunzitsani inu kuti muthenso kuphunzitsa anthu ena

monga mmene Yesu anaphunzitsira.

Pamene mukuphunzitsa zimene Yesu anaphunzitsa, mumaphunzitsa zonse zimene zili mu Mau a

Mulungu chifukwa choti zakhazikika pa Chipangano Chatsopano monga Yesu anati:

Ndipo anati kwa iwo, Awa ndi mauwo ndinalankhula nanu, paja ndinakhala ndi

inu, kuti ziyenera kukwanitsidwa zonse zolembedwa za Ine m'cilamulo ca Mose, ndi

aneneri, ndi masalmo…

Page 135: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

135

ndipo anati kwa iwo, Kotero kwalembedwa, kuti Kristu amve zowawa, nauke kwa

akufa tsiku lacitatu;

ndi kuti kulalikidwe m'dzina lace kulapa ndi kukhululukidwa kwa macimo kwa

mitundu yonse, kuyambira ku Yerusalemu (Luka 24:44, 46-47)

6. KUONETSERA:

Yesu sanaphunzitse kuchokera pa zolankhula zokha ayi. Amaonetseranso zimene amaphunzitsa

u machiritso kwa odwala. Anali ndi mphamvu yotulutsa ziwanda ndi ulamuliro pa Satana.

Anaika chidwi pa osauka nawapatsa chakudya. Ophunzira sanali ophunzira okha, komanso anali

mboni pa zimene Yesu amachita ndi mphamvu ya Mulungu. “Cimene cinaliko kuyambira

paciyambi, cimene tidacimva, cimene tidaciona m'maso mwathu, cimene tidacipenyerera, ndipo

manja athu adacigwira ca Mau a moyo (I Yohane 1:1).

Yesu anaphunzitsa nakhala chitsanzo. Anaonetsera zimene anaphunzitsa ndi mmene anakhalira

ndi kutumikira. Ndipo anati:

Pakuti ndakupatsani inu citsanzo, kuti, monga Ine ndakucitirani inu, inunso mucite

(Yohane 13:15)

Kuonetsera kwa mphamvu kumapangitsa anthu kuti akhale ndi chidwi ku uthenga:

Ndipo makamuwo ndi mtima umodzi anasamalira zonenedwa ndi Filipo, pamene

anamva, napenya zizindikilo zimene anazicita (Machitdwe 8:6)

Paulo sanalankhule za choonadi cha uthenga wokha (Agalatiya 2:5) komanso za mphamvu ya

uthenga wabwino (Aroma 1:16). Analengeza ndi kuonetsera uthenga (I Akorinto 2:1,4).

Chifukwa cha kufunika kwa kuonetsera mphamvu mu kuchulukitsa, Harvestime International

Institute ali ndi phunziro lotchedwa “Mfundo za Mphamvu” ku maphunziro amenewa.

7. KUTENGA NAWO MBALI:

Chidziwitso chokhal sichipindula. Kuti uchite bwino, chidziwitso chiyenera chigwire ntchito.

Keneko imafika nthawi yoti muchitepo kanthu. Ophunzira samangomvetsera ndi kuonera

ziphunzitso za Yesu ndi chionetsero cha mphamvu koma amtenga nawonso mbali. Kuphunzitsi

chithu sizikwanira kuti utha kuphunzira. Kuphunzitsa kokha kuli ngati kuyera opareshoni ya mu

ubongo powerenga mabuku.

Ophunzira akuyenera kukhala ndi luso kapena mzeru za kachitidwe ka zinthu ka zimene

akuphunzira. Akuyenera kudziwa za mmene angalalikire uthenga, kupempherera odwala, ndi

kutulutsa ziwanda. Yesu amapereka mwayi umenewu kwa ophunzira ake. Werengani pa Marko

6:7-13 ndi Luka 9:1-6. Yesu anawatuma ophunzra ake kuti akayesere zimene anawaphunzitsa.

Onetsetsani kuti ophunzira anu ali ochita mawu osati ongomva kokha.

8. KUYANG’ANIRA

Page 136: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

136

Pamene ophunzira a Yesu anabwerera ku utumiki umene Yesu anawatuma, Yesu anasanthula

ntchito yawo (Luka 9:10). Mu maphunziro onse amen anachita nawo Yesu amawayng’anira

ophunzira ake. Samawasiya wokha kuti azilimbana nazo zinthu. Amakhala nawo kuti awakonze,

kuwadzudzula ndi kuwalimbikitsa.

Simungayerekeze kuti ntchitoyi mukhoza kuichita chifukwa mwamuonetsera wogwira ntchito

machitidwe ake, ndi kutuma ndi chiyembekezo chonse. Mukuyenera kumuyang’anira. Monga

ophunzira amakumana ndi zokhumudwitsa ndi zoletsa, mukuyenera kuwaphunzitsa za mmene

angakumaire ndi zimenezi. Kuyang’anira nthawi zina kumatchedwa “kulondola.” Paulo

amayang’anira komanso “kulondola” ophunzira ake:

Atakhala kumeneko nthawi, anacoka, napita pa dziko la Galatiya ndi Frugiya

m'dziko m'dziko, nakhazikitsaakuphunzira onse (Machitidwe 18:23)

nalimbikitsa mitima ya akuphunzira, nadandauliraiwo kuti akhalebe

m'cikhulupiriro, ndi kuti tiyenera kulowa m'ufumu wa Mulungu ndi zisautso

zambiri (Machitdwe 14:22)

KUPATSA ENA NTCHITO:

Gawo lomaliza la kukhala wophunzira linali pamene Yesu amapatsa ophunzira ake chochita pa

kukhala anthu opanga ophunzira ena. Anawapatsa ntchito ya kuchulukitsa ku uzimu kudziko

lonse lapansi.

MAKHALIDWE A WOPHUNZIRA WENIWENI

Ophunzira ayesu akuyenera kukhala okhulupirira okhwima ndi kuonetsa chipatso cha Mzimu

Woyera ngati chizindikiro mmoyo wawo komanso mphatso za mzimu zikhale zochitachita

mmautumiki awo.

Pali makhalidwe ambiri a kukhala wophunzira weniweni wa Yesu pamene mukuona zimene

Mau a Mulungu akufotokozera, koma Yesu anakhazikika pa makhalidwe 9. Wophunzira ndiye

amene:

1. AMASIYA ZINTHU ZONSE:

Amasiya zonse ndi kuyamba kumutsata Yesu.

Cifukwa cace tsono, yense wa inu amene sakaniza zonse ali nazo, sakhoza kukhala

wophunzira wanga (Luka 14:33)

2. KUDZIKANA WEKHA:

Wophunzira woona ayenera kudzikaniza yekha ndi kunyamula mtanda mwaufulu:

Page 137: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

137

Pomwepo Yesu anati kwa ophunzira ace, Ngati munthu afuna kudza pambuyo

panga, adzikane yekha, natenge mtanda wace, nanditsate Ine (Mateyu 16:24)

Ndipo amene ali yense sasenza mtanda wace wa mwini yekha, ndi kudza pambuyo

panga, sakhoza kukhala wophunzira wanga (Mateyu 14:27)

3. KUTSATIRA YESU:

Pomwepo Yesu anati kwa ophunzira ace, Ngati munthu afuna kudza pambuyo

panga, adzikane yekha, natenge mtanda wace, nanditsate Ine (Mateyu 16:24)

4. KUPANGA UFUMU WA MULUNGU KUKHALA WOYAMBA:

Cifukwa cace musadere nkhawa, ndi kuti, Tidzadya ciani? kapena, Tidzamwa

ciani? kapena, Tidzabvala ciani

Koma muthange mwafuna Ufumu wace ndi cilungamo cace, ndipo zonse zimenezo

zidzaonjezedwa kwa inu (Mateyu 6:31,33)

5. KUONETSERA CHIKONDI CHA MULUNGU:

Ndikupatsani inu lamulo latsopano, kuti mukondane wina ndi mnzace; monga

ndakonda Inu, kuti inunso mukondane wina ndi mnzace. 351 Mwa ici adzazindikira

onse kuti muli akuphunzira anga, ngati muli naco cikondano wina ndi mnzace

(Yohane 13:34-35)

6. KUKHAMA MMAWU:

…Ngati mukhala inu m'mau anga, muli akuphunzira anga ndithu (Yohane 8:31)

Mawu oti “kukhala” amatanthauza kuti kupitilira. Wophunzira amakhala akuphunzira mopitilira

ndi kugwiritsa ntchito Mau a Mulungu.

7. NDI OMVERA:

Kukhala mu Mau kumaposa kuphunzira. Uku ndi kuchita zimene mwaphunzira. Ndiye kumvera.

Sizikwanira kuwerenga, kuphunzira kapena kuloweza Mau. Amayenera apange chikhalidwe cha

munthu. Kukhala mu Mau kumaphtikizapo kumvera.

8. NDI OTUMIKIRA:

Kumkwanira wophunzira kuti akhale monga mphunzitsi wace, ndi kapolo monga

mbuye (Mateyu 10:25)

Sikudzakhala comweco kwa inu ai; koma amene ali yense akafuna kukhala wamkuru

mwa inu, adzakhala mtumiki wanu;

Page 138: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

138

Ndipo amene ali yense akafuna kukhala woyamba mwa inu, adzakhala kapolo wanu

Monga Mwana wa munthu sanadza kutumikiridwa koma kutumikira, ndi kupereka

moyo wace dipo la anthu ambiri (Mateyu 20:26-28)

9. KULEMEKEZA MULUNGU MWA KUBEREKA ZIPATSO:

Wophunzira ayenera kulemekeza Mulungu pobereka zipatso:

Mwa ici alemekezedwa Atate wanga, kuti mubale cipatso cambiri; ndipo

mudzakhala akuphunzira anga (Yohane 15:8)

Pamene mubala chipatso cha ku uzimu, mumakuza chipatso cha Mzimu Woyera mu moyo wanu

(Agalatiya 5:20-23). Mumabala chipatso poberekana ku uzimu (Yohane 15:1-16)

YESERO LENILENI LA WOPHUNZIRA

Yesero lenileni la wophunzira ndi zimene zimzchitika pamene simukupezeka ndi iwo amene

munawaphunzitsa. Kodi mumakhalabe okhulupirika ku zimene munaphunzitsidwa? Kodi

mumaphunzitsa ena amene ali ndi kuthekera kochulukana? Ngati ndi choncho ndiye kuti kukhala

wophunzira kwanu kuli kopambana:

Wophunzira saposa mphunzitsi wace; koma yense, m'mene atakonzedwa mtima,

adzafanana ndi mphunzitsi wace (Luka 6:40)

Mu maphunziro anu ndi ena, yembekezerani mavuto monga mmene Yesu anakumana nawo…

-Munthawi ina yake, Petro, Yakobo ndi Yohane anawonetsa maganizo a udani popempha

moto kuchokera kumwamba kuti uwononge mudzi wa Samariya umene sumalandira

uthenga (Luka 9:51-55).

-Petro anamkana Yesu katatu (Luka 22:54-62).

-Onse atatu amagona mmunda wa Getsemane pamene anauzidwa kuti apemphere (Luka

22:45-46).

Koma anthu ochepawa anali oyenera kupereka nthawi yawo ku utumiki wa Yesu. Yesu

anatsimikira kukhala anthu okhulupirika, posatengera zofooka ndi zolephera zawo. Panthawi

imene Yesu sanali ndi iwo anakhalabe ophunzira ochulukitsa ku maiko onse a dziko lapansi.

Yesu anati:

Zotuta zicurukadi koma anchito ali owerengeka (Mateyu 9:37)

Page 139: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

139

Anthu otuta zokolola oyenera kututa zokolola za uzimu ndi ochepa. Kodi mwakonzeka kupereka

moyo wanu kukhala gawo limodzi la ochepawa?

Page 140: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

140

MAYESO ODZIYETSA NOKHA

1. Lembani Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

2. Kodi mawu oti “kutembenuka” akutanthauza chiyani?

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

3. Perekani tanthauzo la mawu oti “wophunzira.”

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

_

4. Lembani mfundo zitatu zachidule cha maitanidwe a kukhala wophunzira

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

____________________________________

5. Lembani mfundo 9 zimene ndi zofunika kukhala wophunzira zimene mwaphunzira

zokhuza Yesu ndi ophunzira ake.

________________________________________________________________________

________________________________________________________________________

________________________________________________________________________

________________________________________________________________________

________________________________________________________________________

________________________________________________________________________

6. Lembani makhalidwe 9 a kukhala wophunzira weniweni.

________________________________________________________________________

________________________________________________________________________

________________________________________________________________________

________________________________________________________________________

________________________________________________________________________

7. Kodi yesero lenileni la wophunzira ndi liti?

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

__________________________________________________________________________

(Mayankho a mafunsowa akupezeka kumapeto kwenikweni kwa bukuli)

Page 141: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

141

Page 142: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

142

KUPITILIZA KUPHUNZIRA

1. Kupereka mwambo kuli ngatinso “kudyetsa nkhosa” mawu amene amaonetsedwa

Mbaibulo za mmene mbusa angasamalire nkhosa zake.

Mulungu ali ngati mbusa: Ahebri 13:20; Masalmo 80:1-2 ndi Ezekieli 34:11

Yesu ali ngati mbusa wa nkhosa: Yohane 10:11-18

Mbusa ndi wotsogolera, woyang’anira kapena mlonda wa nkhosa. Amazipulumutsa ku

choipa, namanga mabala, kuzikonda ndi kudzidyetsa. Werengani Mateyu 9:36-38; Marko

3:14- 15; Yohane 21:15-17; Machitidwe 20:28.

2. Kuitana kwambiri kwa Yesu Khristu ndi kobwerezabwereza. Mawu oti “unditsate”

agwiritsidwa ntchito koposa ka 20. Mwachitsanzo Simoni ndi Andreya; Mateyu 4:19;

Marko 1:17. Onani zitsanzo zina.

3. Mawu oti “ophunzira” sakupezeka Muchipangano Chakale, koma mfundo za kupereka

mwambo zikupezekamo. Mwachitsanzo Yoswa anali wophunzira kwa Mose

(Deuteronomo 3:28). Perekani zitsanzo zina.

4. Onani mmene Paulo anachitira kalondolondo kwa ophunzira ake:

Ndi kalata: I Atesalonika 1:1

Ndi pemphero: I Atesalonika 1:2; 3:10

Potuma nthumwi: I Atesalonika 3:1-5

Popita yekha I Atesalonika 2:18

Page 143: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

143

CHAPUTALA CHA 11

KUKULA MOPINIMBIRA

ZOLINGA:

Paakutha pa chaputalachi muyenera:

Kulemba Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

Kupereka tanthauzo la mawu oti “kupinimbira.”

Kuzindikira zinthu zimene zimatchinga kukula ku uzimu ndi kuchulukana.

Kupereka zithandizo zimene Baibulo limapereka pokonza mavuto amenewa.

VESI LOTSOGOLERA:

Wodala munthuyo wosayenda mu uphungu wa oipa, Kapena wosaimirira m'njira

ya ocimwa, Kapena wosakhala pansi pa bwalo la onyoza.

Komatu m'cilamulo ca Yehova muli cikondwerero cace, Ndipo m'cilamulo cace

amalingima usana ndi usiku.

Ndiye akunga mtengo wooka pa mitsinje ya madzi; Wakupatsa cipatso cace pa

nyengo yace, Tsamba lace lomwe losafota; Ndipo zonse azicita apindula nazo

(Masalmo 1:1-3)

MAWU OYAMBA

Pali zinthu zambiri zimene zimakhudza kukula kwa munthu. Kuperewera kwa chakudya

choyenera kumatchinga kukulaku. Matendanso a mitundumitundu amakhudza kukula. Pamene

kukula kukusowa mthupi, pakuyenera kukhala chopulumukirapo chimene chingakonze vutoli

kupanda kutero kukula kupinimbira. Pamene kukula kuli kopinimbira, thupi silikulanso bwino.

Pamene mukuphunzira phunziroli, Baibulo limaonetsera mpingo ngati thupi la munthu. Pokhala

thupi la munthu, makulidwe amakhudzidwa ndi zinthu zina. Nthawi zina mavuto amachitika mu

mpingo ndiwo amene amalepheretsa kukula ku uzimu. Pamene kukula mu uzimu kuli

kopinimbira, mpingo umalephera kukula. Pakusowa anthu ndi ophunzira ndi kusowa kwa

kukhwima mu uzimu.

Yesu anati, “ndidzamanga mpingo.” Sitingabweretse kuchulukana tokha, koma tikhoza kuchotsa

zinthu zimene zimalepheretsa kukula. Pamene tikutero, ndiye kuti tikupanga malo ati kukula

kungachitike. Chaputala ichi chikuonetsa mavuto amene amalepheretsa kuchulukana. Pa vuto

lililonse pali Vesi yake imene ingakonze vutolo.

KUKULA KOPINIMBIRA

VUTO: KUSOWA CHAKUDYA CHA UZIMU.

Page 144: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

144

Thupi la munthu liyenera kupatsidwa chakudya ndi madzi kupanda kutero limafa. Thupi la

uzimu liyenera kupatsidwanso chakudya ndi madzi kupanda kutero limafa. Mipingo ina

simaphunzitsa Mau a Mulungu koma amaphunzitsa ziphunzitso za anthu. Amanena zimene

anthu afuna kudzimva (II Timoteo 4:3). Kuperewera zakudya za ku uzimu kumabweretsa njala

ya Mau a Mulungu (Amosi 8:11-12). Ena amanh=gophunzita “mkaka” wa mau ndipo anthu

sakula ku uzimu. Okhulupirira amanyalanyaza kuwerenga Mau a Mulungu kapena sasanthula

maziko a choonadi cha ngati “nyama” ya Mau a Mulungu. Monga thupi limafa popanda

chakudya, thupi la uzimunsi limafa.

YANKHO:

Kutsindikanso kobwereza pa Mau a Mulungu (Aroma 10:17). Phunzitsani mkaka ndi nyama ya

Mau a Mulungu (I Akorinto 3:1, I Petro 2:22 ndi Ahebri 5:12-14). Thupi la munthu silingadalire

mkaka konse. Ngakhale mwana wang’ono ayenera kuphunzira kudya chakudya cholimba. Mau a

Mulungu ndi mkate wa moyo wa uzimu.

VUTO: KUSOWA MASOMPHENYA.

Baibulo limati “popanda masomphenya anthu amasochera” (Miyambo 29:18). Masomphenya a

uzimu a anthu ena ndi amalire kubanja ndi kudera lawo. Ena amatanganidwa ndi malo ena

akutali ndi zinthu za mayina a chilendo, pamene anthu kunja kwa mpingo akufa opanda Yesu.

YANKHO:

Pakuyenera kukhala kufanana masomphenya azochitika zathu ndi za uzimu. Mpingo ukuyenera

kukhala ndi masomphenya a dziko lonse koma osasiyanso iwo amene ali mdera lathu. Awa ndi

masomphenya amene Yesu anapatsa ophunzira ake a zokolola za uzimu zimene zapsa kale

mmunda. Mundawu ndi dziko. Werengani Yonane 4.

VUTO: KUKULA KOCHEPA.

Werengani fanizo la ofetsa mu Marko 4:1-20. Pamene mbewu ya Mau a Mulungu sikhala ndi

muzu mmoyo wanu, mumakhala ndi kukula kochepa. Pamene chizunzo ndi zovuta zabwera

mumafa ku uzimu (Marko 4:17).

YANKHO:

Phunzitsani anthu kuti kuwerenga, kumva ndi kuphunzitsa Mau a Mulungu sikokwanira.

Akuyenera kukhala ochita Mau a Mulungu. Akuyenera kusintha moyo wawo (Yakobo 1:22-25).

Ndi pakulowa kwa Mau mumtima kumene kumabweretsa kusintha (Masalmo 119:130).

VUTO: KUSOWA KUTSADZA

Mipingo kwanthawi yaitali yakhala yosabereka mu njira zawo ndi dongosolo lawo. Pamene

zochitikazi sizisadzidwa, kubala zipatso kumatha. Popanda kutsadza, Pang’ono ndi pang’ono

imfa imabwera imaononga moyo. Pamene mtengo sunatsadzidwe ukhoza kumakula moongoka

Page 145: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

145

koma uli wakufa. Palibe zipatso, kukula komanso kuchulukana. Mtengo kukhalapo koma opanda

moyo. Izi ndi chomodzimodzi ndi kudziko la uzimu.

YANKHO:

Nthambi zosabereka ziyenera kudulidwa ndi cholinga chofuna choti mtengowo ubereke zipatso

zambiri. Kudziko la uzimu tikuyenera kudula ntchito zosathandiza mmoyo wathu ndi mumpingo

wathu. Njira ndi ndondomeko zimene sizimabweretsa athu kwa Yesu ndi ophunzira zichotsedwe.

Mikumano iwonedwenso, kaya ndi ndondomeko ziunukilidwenso ngati ndi zothandiza.

VUTO: KULEPHERA KUDZIWA MALO AMENE ANGALANDIRE UTHENGA:

Mu fanizo la ofetsa mu Marko 4:1-20, panali dothi labwino ndi lina losakhala bwino. Kukula

kochepa kumachitika mu dothi losakhala bwino.

YANKHO:

Pali malo ena amene ali ndi mwayi wochepa wochulukana. Ndipo pali malo ena amene

amakhalaokonzeka pa zokolola za uzimu amene amapereka mwayi olalikira uthenga wabwino.

Anthu oyenera ayenera adziwike ndi kuchitapo kanthu kwa anthu amenewa. Pamene Paulo

anamva Mzimu Woyera kuti akubweretsa anthu amitundu kukhala ophunzira ku Antiokeya,

mwachangu anachoka ku Tarisi mkupita ku Antiokeya. Pamene nthawi inali isanakwane ku

mAsiya, Paulo anakhalabe kumene mpakana Mulungu anamutsekula maso. Khazikikani ku malo

kumene kuli kuthekera. Pitilizani kufesa ndi kudikira nthawi yoyenera kuti mudzatute zikapsa.

VUTO: ZOFUNIKA ZOLAKWIKA.

Atsogoleri a uzimu ali ndi zofunika zimene ndi zolakwika pamene ali ndi chidwi ndi zochita za

mpingo kuposa pemphero ndi kutumikira Mau a Mulungu. Zofunika zimakhala zachiwiri monga

mamangidwe ndi tchito zina. Kukoza mpingo kumakhala kofunika kuposa utumwi.

YANKHO:

Yesu sanalankhulepo za mamangidwe apamamba. Akhristu amapanga zochita zambiri. Ngakhale

izi sizolakwika, koma kuchulukana kumalephereka pamene chidwi chikukhala pa mamangidwe

osati kulalikira ndi kupanga ophunzira. Vuto la zofunika ndi ziti ndi mayankho ake zikupezeka

ku Machitidwe 6:1-6. Pamene atsogoleri aika chidwi pa pemphero ndi kutumikira Mau a

Mulungu kuchulukana kumabwera (Machitidwe 6:7).

VUTO: UTUMIKI WOSAGWIRIZANA NDI ANTHU

Mipingo ina yasiya kukula chifukwa choti utumiki sugwirizana ndi anthu. Mwina mtumiki

sakhala mmodzi wa anthuwo. Amakhala wa chikhalidwe china zimene ndi zovuta kupereka

uthenga mu chiyankhulo chimene angamve.

YANKHO:

Page 146: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

146

Atsogolera ayenera kuchokera ku mpingo umene akuchokera ngati kuli kotheka pamene mpingo

wadzalidwa (Tito 1:5). Atsogoleri a kudera amene ali ndi chikhalidwe ndi chiyankhulo cha

kumaloko amatha kulumikizana ndi anthu a kumeneko mosavuta.

VUTO: “BWERANI MUWONE” OSATI “PITANI MUKAWAUZE”

Mipingo yambiri yatenga njira ya “bwerani” osti “pitani” imene Yesu analamulira. Mipingoyi

imakhala ndi mikumano ndi dongosolo limene limakopa anthu osakhulupirira “kubwera” ku

mpingo. Sapita ku dziko kukawapeza ndi uthenga wabwino ndi kuwabweretsa ku mpingo.

Amatsekula zitseko mkumadikira anthu kuti abwere, koma palibe amene amabwera. Mu mpingo

umenewu mamembala amakangalika ndi mikumano, misonkhano, maphunziro mmalo mwa

maulaliki otuluka.

YANKHO:

Mpingo ukuyenera kukhala wogwirira ntchito Mulungu mdzikoli. Koma mpingo wakhala

okangalika kusiyana ndi kukhala maziko a Mulungu otumiza ophunzira mmunda wa dziko

kukachulukana. Mpingo ukuyenera kusiya kudzitumikira wokha ndi kuyamba kutumikira dziko.

Mpingo ukhale malo amene okhulupirira alandirapo maphunziro ndi kukonzekerdwa kupita ku

dziko lapansi kumene kuli ochimwa ndi kuwatengera kwa Yesu. Njira ya Yesu yopita iyenera

kutsindikizidwa (Mateyu 28:19; Machitidwe 1:8).

VUTO: TCHIMO LOSAVOMEREZA

Tchimo losavomereza mmoyo wa membala wa mpingo limatchinga kukula moyo wauzimu.

YANKHO:

Werengani malangizo a Paulo kwa mpingo wa kwa Akorinto othana ndi tchimo losavomereza

kwa munthu (I Akorinto 5:11-13). Ngati membalayi walapa, akuyenera kulandilidwanso (Onani

II Akorinto 2:4-8).

VUTO: MAVUTO A MUNTHU OSATHA:

Mikangano imakhala mu mpingo ngati membala wa mpingo akali ndi mangawa ndi munthu

wina. Ngati sakhala pamodzi kufuna kuthetsa magawano amayamba. Mavuto osatha

amalepheretsa kuchulukana.

YANKHO:

Mateyu 18:15-17 amapereka malangizo othetsa mavuto pakati pa anthu mu thupi la Yesu.

Werengani chitsanzo cha Paulo ndi Banaba mu Machitidwe 15:36-41. Ngati mabvutowa atha

bwinobwino, ngakhala kugawana kungabweretse kuchulukana mu ufumu wa Mulungu.

VUTO: UTSOGOLERI WA UZIMU WOSAYENERA:

Page 147: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

147

Kukula kumakhudzidwa ngati atsogoleri safikira makhalidwe a uzimu opezeka Mbaibulo.

Miyeso ya atsogoleri a mpingo oikidwa ndi Mulungu ndi zoyenereza ku uzimu. Sasamala za

maphunziro a munthu ndi kuthekera kwa munthu kuyerekeza ndi makhalidwe a uzimu wa

munthu (onani I Samueli 16:7).

YANKHO:

Mtaogoleri ayenera kusiya udindo wake kufikira aika “nyumba yake” (moyo wake wa uzimu ndi

banja lake) mmalo mwake. Atsogoleri ayenera kukhala ndi zowayenereza zomwe zili mu I

Timoteo 3 ndi Tito 1:5-9.

VUTO: KUKANA KUSINTHA.

Anthu ali ndi chikhalidwe chokana kusintha. Ambiri amakhutira ndi zinthu zimene zakhala

zikuyendera kwa zaka 40 zapitazo. Sakonda kuvomereza zinthu zatsopano.

YANKHO:

Kumbukirani kuti cholinga cha mpingo ndi kuchita maulaliki ndi kuchulukana ku uzimu

sikumasintha. Njira zokwaniritsa cholingachi zimatha. Ndi zoona kuti tiyenera kugwiritsa ntchito

njira za Mbaibulo za mpingo woyamba, koma dziko lasintha kuchokera nthawi imene ija.

Sitingakane njira zatsopano chifukwa sizimapezeka Mbaibulo. Monga makina a computer, ma

disiki a uthenga wabwino amene Paulo sanagwiritse ntchito. Pakuti kunalibe nthawi imeneyo.

VUTO: MAVUTO A KULUMIKIZANA

Kuchulukana kumalephereka ngati palibe kulumikizana bwino pa uthenga wabwino. Atumiki

amayeera kusangalasa anthu awo ndi mawu a pamwamba ndi kuonetsa chidziwitso cha

maphunziro awo a umulungu. Potero amalemphera kulumikizana ndi zosowa za anthu. Ntchito

zawo sizigwirizana ndi mawu awo.

YANKHO:

Uthenga ukuyenera kufalisidwa mu njira yoti anthu amvestere. Alaliki, aphunzitsi ndi avangeli

ayenera kupereka uthenga mu muyeso wa anthu amene akuwalalikira mmalo mwa mawu a akulu

ndi kuonetsa chidziwitso. Pamene Yesu amaphunzitsa, anthu amamvetsera ndi kumvetsetsa

(Marko 12:37).

Mmene uthenga ukuperekedwa uyenera kusinthidwa molingana ndi mmene anthu alili pa

maphunziro awo (Aroma 1:14). Kulumikizana kwa mmawu kuyenera kugwirizana ndi

makhalidwe a moyo. Tikuyenera kukhala ochita mawu ndi olengeza mawu. Kulengeza kwa

chikhulupiriro chathu kumakhala kopambana pamene zinthu za Mulungu zikuonekera mmoyo

wathu (Filemoni 6).

VUTO: KUSIYANA KWA ZIKHALIDWE, DERA NDI ZIPEMBEDZO.

Page 148: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

148

Mipingi ina simakwanitsa kufikira anthu mdera lawo chifukwa “Sali ngati ife.” Samatumikira

kwa iwo amene ndi osiyana chikhalidwe, mtundu, ngakhale chiyankhulo. Mpingo ina imakana

kuwoloka malire posafuna kuti anthu a dera lina akhale a mumpingo mwawo. Ena amakana

chiyanjano ndi mipingo ina. Ena anazipatula kudziko moti sangachulukane chifukwa

samalumikizana ndi osakhulupirira.

YANKHO:

Onani Aefeso 2:14. Palibe makoma a kusiyana mwa Yesu. Mpingo wamanga makoma a

kusiyana amene akuyenera kuchotsedwa. Tikuyenera kudutsa chikhalidwe chathu, chiyankhulo,

dera komanso zipembedzo ndi cholinga choti tikafikire anthu onse. Tikuyenera kusiya pambali

zomemera ndi machimo ndi kuyamba kuika chidwi pa kufikira anthu a dziko lonse ndi uthega

wabwino (Ahebri 12:1-2). Sitikuyenera kudzipatula kudziko, koma tikhale mdzikoli koma

osachita nawo ntchito za uchimo (Yohane 17:15). Kudzipatula kudziko sizitanthauza kusiyana

kapena kusalana.

VUTO: KUKHALA ONERERA OSATI OTENGA NAWO MBALI

Onera ndi anthu amene amangoyang’anira koma satenga now mbali mu zochitika za Mulungu.

Samaberekana mu uzimu. Amanyalanyaza kulalikira ndi kupanga ophunzira kwa atumiki

“ophunzira.” Mpingo wodzala ndi anthu ononerera sumakula.

YANKHO:

Munthu wina aliyense adziwe udindo wake pa lamulo la Yesu pa Mateyu 28:19-20. Anthu

akuyenera kutsogoleredwa kuti agwiritse ntchito mphatso zawo za uzimu ndi cholinga chakuti

mpingo ukule bwino (Timoteo 1:6). Atumiki ayenera kukonzekeretsa anthu ku utumiki (Aefeso

4:12). Munthu aliyense akhale wochitachita, ndi khomo lililonse likhale malo a ulakili (II Timote

2:2).

VUTO: OTEMBENUKA SAKHALA OPHUNZIRA

Okhulupirira atsopano sakula kukhala ophunzira. Amabwerera ku moyo wawo wakale kapena

kukhala ana mu uzimu amene sakwanitsa kuchulukana ku uzimu.

YANKHO:

Okhulupirira tsopano ayenera kuumbidwa ndi kukonzekeredwa ku utumiki ngati kuchulukana

kupitilire. Ulaliki sukhala okwanira kufikira wotembenuka mtima akhala wamphamvu wa Yesu.

Chiphuncityso chikuyenera kuchitika ukaliki pamene zikuchitika (Mateyu 28:19-20).

VUTO: MANTHA

Kuopa kulemphera ndi mdani wamkulu pa kuchulukana. Werengani fanizo la matalente pa

Mateyu 25:14-30. Kapolo amene amaopa sanachite bwino. Sanachulukane mu uzimu.

Page 149: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

149

YANKHO:

Khalani pa ubale ndi Mulungu mwachikondi osti mwa mantha (I Yohane 4:18).

VUTO: CHIDWI PA NTCHITO OSATI KULAMBIRA

Dongosolo, ndondomeko ndi zochitika za mpingo zikhoza kutenga malo a malambiro. Mwambo

wa mapemphero ukhoza kukhala wa zolemgeza, kupereka ndalama ndi zina.

YANKHO:

Ikani koyambirira zinthu zofunika mu mpingo. Chikondi ndi kulambira Mulungu zikhale

koyamba. Chikondi ndi utumiki kwa ena zibwere pambuyo. Mapulogalamu ena amabwera

pambuyo pa zochitika ziwiri zazakuluzi (Mateyu 12:29-31).

VUTO: KUTUMIKIRA DERA OSATI ANTHU.

Pali zosowa zambiri lero mu dziko lathupi. Pali osauka ambiri amene afunika chakudya, zovala,

ndi malo okhala. Pali anthu amene afunika mankhwala ndi ntchito. Pali mavuto ena a

kayendetsedwe ka boma, maphunziro amene akufunika kukonzedwa. Izi ndi zosowa zenizeni

zimene mpingo ungather kutumikira anthuwa mu dzina la Yesu. Koma nthawi zambiri chidwi

chathu chimakhala kutumikira dera osati kupulumutsa moyo wa anthu.

YANKHO:

Mkazi amene anali ndi Yesu pachitsime amafuna madzi a kuthupi koma Yesu anampatsa

chosowa chake chenicheni cha ku zuimu (onani Yohane 4). Maitanidwe a akulu a mpingo

sikutumikira dera, koma kupulumutsa anthu amene ndi ovutika ku uzimu. Kutenga nawo mbali

mu zochitika ndi kuchita mwa nzeru sikudzapangitsa anthu anjala kufuna mkate wa moyo.

VUTO: KUSAKHULUPIRIRA

Werengani nkhani ya Israyeli pa malire a dziko lolonjezedwa la Mulungu (Numeri 13). Israyeli

sanalowe mdziko la malonjezano chifukwa chosakhulupirira. Anabwerera mbuyo mu chipululu

muja ndipo mbadwo onse unatha kwa zaka 40.

Wokhulupirira aliyense ndi mpingo uliwonse ayenera afike pa “Kadesi” pa malo a uzimu.

Akhoza kupita chitsogolo mu chikhulupiriro mkufusa malonjezo a Mulungu, kapena abwerera

mbuyo mkusakhulupirira kwawo mkufa ku uzimu.

YANKHO:

Kusakhulupirira kumalepheretsa kukula komanso kuchulukana. Mpingo ukuyenera kukhulupirira

kuti kukwaniritsa chipambano pa ulaliki ndi kupanga phunzira kwagona pa chikhulupiriro

(Marko 6:15). Kukhulupirira kutenga malo a kusakhulupirira. Chikhulupiriro chimakula ndi Mau

Page 150: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

150

a Mulungu. Anthu ayenera kuchita zinthu mwachikhulupiriro. Ndipo chikhulupiriro chikhale ndi

ntchito yake (Yakobo 2:26).

VUTO: UNYINJI OSATI KHALIDWE

Chidwi pa unyinji osati khalidwe kumabweretsa nthu osakhwima mu uzimu. Zimatheka kukhala

ndi anthu ambiri koma olephera kukhala ophunzira ndi osakhwima.

YANKHO:

Onaninso chaputala cha 6 cha phunziroli. Gwiritsani ntchito mfundo kuti mukule ku uzimu.

VUTO: ANTHU AMASOCHERA MU KHAMU LA ANTHU.

Pamene mpingo ukukula, anthu “amataika mu gulu la anthu.” Amayamba kuzimvu kuti alipo

ambiri. Sipakhala kulumikizana, kusamalana ndi chidwi. Chidwi chimakhala pa khamu osati pa

munthu.

YANKHO:

Moyo umodzi ndi wopambana kuposa dziko lonse (Mateyu 16:26). Ngakhle tiyenera

kukhuzidwa ndi dziko lonse, koma tisachotse chidwi chathu pa munthu mu khamu. Anthu

amabadwa mu uzimu kwa nthawi imodzi koma amataika payekha.

Palibe chithu ngati kutembenuka mtima kwa gulu. Ngakhale gulu litembenuka ku ulaliki,

munthu aliyense amapnga chisankho yekha. Tisaike chidwi chathu pa khamu la anthu ndi

kuiwala munthu mmodzi. Yesu amaitana munthu mu khamu la anthu mkuyamba kumutumikira.

Kuyamba mautumiki ang’ono ndi njira imodzi yosunga utumiki wa anthu mu khamu ndipo

kuchulukana mumpingo kumatheka.

VUTO: TIMAGULU TA MUMPINGO

Nthawi zina “timagulu” tiyamba mu mpingo. Awa ndi magulu a ang’ono a anthu amene

amakhala pamodzi ndi cholinga chofuna kusiyanitsa kapena kukana kuyanjana ndi anzawo.

Gululi limalola anthu ena kukhala nawo koma ena amawakana.

YANKHO:

Baibulo limaphunzitsa kuti mchitidwe oterewo ndi wolakwika. Werengani Yakobo 2:1-10.

Chikhalidwe choterechi chimafuna kulapa chifukwa ndi tchimo.

VUTO: GULU LAMOYO, KOMA ANTHU AKUFA

Gulu ndi lofunika, koma kukula mu uzimu kumalephereka pamene chidwi chili pa gulu osati

kukhala ndi moyo wa Mulungu. Miyambo, malamulo, ndi zikhalidwe zimachotsa uzimu

Page 151: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

151

weniweni (Marko 7:13), gulu la mumpingo likhoza kukhala ndi moyo ndithu, koma anthu amene

ndi moyo weniweni wa uzimu mthupi umafa ngati palibe moyo wauzimu.

Mipingo yoterryi imakhala ndi ndondomeko zabwino ndipo amakhala ndi “dzina limene

amachitira izi” koma ku uzimu akufa (Chibvumbulutso 3:1). Moyo wa uzimu umafa. Amakhala

ndi maonekedwe a chipembedzo koma mphamvu yake adaikana (II Timoteo 3:5)

YANKHO:

Mpingo umafanizidwa ngati thupi. Thupi ndi lamoyo, osati chith cha ziwalo ayi. Gulu

silingapereke moyo. Koma chithu cha moyo chingathe kupereka moyo. Moyo wa thupi la

mpingo ukuyenera uphunzitsidwe ndipo utumiki utsindikidwe (I Akorinto 12).

VUTO: KUSOWA CHIKONDI

Mpingo ukhoza kukhala ndi machitichita a uzimu, koma opanda chikondi. Anthu samachezeka.

Samakondana wina ndi nzake. Pamakhala chiwawa, udani, malingaliro oyipa kwa wina.

YANKHO:

Utumiki uliwonse, mphatso iliyonse ndi ntchito iliyonse ya munthu kapena mpingo ili chabe

popanda chikondi. Werengani ndi kugwiritsa ntchito I Akorinto 13.

VUTO: KUSOWA KWA ZINTHU

Anthu ndi ndalama ndi zinthu zofunika pa kuchulukana. Kukula kukhoza kukhala kopinimbira

pamene palibe anthu odzipereka ku masomphenya. Kosowa kwa thandizo la ndalama

kungalepheretse kukula ndi kutukuka kwa mpingo.

YANKHO:

Tsindikani za Ufumu wa Mulungu osati kukamba za utumiki wa munthi. Yesu analonjeza kuti

zinthu zonse zimene tizifuna tidzapatsidwa tikachita zimene zili pa Mateyu 6:33. Pemphererani

anthu oyenera kugwira ntchito ya Mulungu kuti akakolole kholola la uzimu mmunda (Mateyu

9:37-38).

Page 152: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

152

MAYESO ODZIYETSA NOKHA

1. Lembani Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

2. Perekani tanthauzo la kukula “mopinimbira.”

________________________________________________________________________

________________________________________________________________________

3. Werengani zitsanzo za nyengo za mipingo yambiri mmene zilili. Zindikirani mavuto ndi

kupereka mayankho ake a Mbaibulo.

Chitsanzo A. Akazi awiri mumpingo samalankhulana wina ndi mzake. Mkazi A

anayankhula zinthu zosakhala bwino kwa mkazi B. Kodi mungapereke yankho laotani?

________________________________________________________________________

________________________________________________________________________

________________________________________________________________________

Chitsanzo B. Usiku wa sabata iliyonse mpingo umakhala ndi zochitika, koma anthu

ochepa ndiwo amene amabwera kwa Ambuye. Kodi pamenepa vuto ndi chiyani? Yankho

ndi liti?

________________________________________________________________________

________________________________________________________________________

________________________________________________________________________

Chitsanzo C. Okhulupirira atsopano ochepa ndiwo amene amapezeka ku mpingo

mwakanthawi, kenako amabwereranso ku zintchito zawo zakale za uchimo. Ena

amakhalabe mu mpingo, koma makanda mu uzimu. Kodi vuto ndi chiyani? Nanga

yankho ndi liti?

________________________________________________________________________

________________________________________________________________________

________________________________________________________________________

(Mayankho a mafunsowa akupezeka kumapeto kwenikweni kwa bukuli)

Page 153: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

153

KUPITILIZA KUPHUNZIRA

1. Bwerezani mavuto a kukula mu uzimu amene akambidwa mu chaputalachi. Pangani

mndandanda wa zinthu za mumpingo wanu zimene zimalepheretsa kukula ndi

kuchulukana. Kodi mavutowa mungawakonza bwanji?

2. Onaninso phunziro ndi kudziwa zinthu zimene zimalepheretsa kukula kwa moyo wanu

wa uzimu. Kodi mavutowa mungawathetse bwanji?

3. Unguzani mpingo wanu ndi moyo wanu wa uzimu. Kodi zinthuzi zikulepheretsa kukula

kwa moyo wanu wa uzimu kupatula zimene zatchulidwa mu chaputalachi? Ngati ndi

choncho lembani mndandanda wa mavutowa ndi kupeza mayankho mu Baibulo.

4. Werengani makalata 7 a kumpingo mu Chibvumbulutso chaputala 2-3. Lembani

mndandanda wa mavuto omwe amene amapezeka mmipingoyi ndi mayankho ake

ochokera kwa Mzimu Woyera.

Page 154: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

154

CHAPUTALA CHA 12

MALO OCHITIRAPO MAPHUNZIRO

ZOLINGA:

Pakutha pa chaputalachi muyenera:

Kulemba Vesi Lotsogolera kuchokera pamtima.

Kudziwa njira zimene Paulo anagwiritsa ntchito pophunzitsa okhulupirira a ku Aefeso.

Kulongosolo malo ochitirapo maphunziro ku Aefeso.

Kulongosola cholinga chokhala ndi malo ochitirapo maphunziro.

Kulemba chidule cha malangizo oyambitsa malo achitirapo maphunziro.

Kuyambitsa malo ochitirapo maphunziro.

VESI LOTSOGOLERA:

Koma pamene ena anaumitsa mtima ndi kusamvera, nanenera zoipa Njirayo

pamaso pa anthu, anawacokera, napatutsa akuphunzira, nafotokozera masiku onse

m'sukulu ya Turano.

Ndipo anacita comweco zaka ziwiri; kotero kuti onseakukhala m'Asiya anamva

mau a Ambuye, Ayuda ndi Ahelene (Machitidwe 19:9-10).

MAWU OYAMBA

Musanayambe kuphunzira chaputalachi, werengani Machitidwe 19:1-20. Ndimeyi imakamba za

utumiki wa Paulo ku mzinda wa Aefeso kumene Paulo anagwiritsa ntchito njira zapadera za

kuchulukana ku uzimu. Anakhazikitsa malo ochitirapo maphunziro. Mu chaputala ichi

muphunzira mmene mungachulukanire kudzera mu utumiki okhala ndi malo ochitirapo

maphuziro.

NJIRA YA AEFESO

Pamene Paulo anafika ku Aefeso, anafufuza ophunzira amene analiko. Anthuwa amenewa anali

atamva kale ndi kulandira uthenga wabwino mkukhala otsatira Yesu (Machitidwe 19:1).

Okhulupirira atsopanowa amafunika kupitiliza maphunziro ndi cholinga choti akhale atumiki

amphamvu mu mzinda mwawo. Chidwi choyamba cha Paulo chinali kuphunzitsa ophunzirawa

zokhudza Ufumu wa Mulungu.

Paulo anawaphunzitsa kudzera mu zimene amadziwa ndipo chinthu choyamba chimene anachita

kunali kuwatsogolera ku moyo watsopano wa uzimu, ndiwo ubatizo wa Mzimu Woyera (onani

Machitidwe 19:2-8). Kudzera mu chionetsero cha mphamvu ya Mulunngu mmoyo wake, Paulo

Page 155: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

155

anawaphunzitsa chitsanzo chake. Anachitira umboni za mphamvu zambiri zimene anachita mu

dzina la Yesu (Machitidwe 19:11-12). Iwo amene sanali otsatira enieni a Yesu anafika poyera

mkulapa (Machitidwe 19:13-17). Otembenuka mtima amapezeka ambiri (Machitidwe 19:17-20).

Pamene panali chitsutso pa uthenga wabwino kuchokera kwa atsogoleri a malamulo, Paulo

anakhazikitsa malo ochitirapo maphunziro a ophunzira a Yesu ku Aefeso:

Koma pamene ena anaumitsa mtima ndi kusamvera, nanenera zoipa Njirayo

pamaso pa anthu, anawacokera, napatutsa akuphunzira, nafotokozera masiku onse

m'sukulu ya Turano (Machitidwe 19:9-10).

Malo amene Paulo anakhazikitsa amapereka maphunziro a zaka ziwiri kwa ophunzira. Cholinga

cha sukuluyi chinali kufuna kuchulukitsa ophunzira amene akhoza kufalitsa uthenga wabwino:

Ndipo anacita comweco zaka ziwiri; kotero kuti onseakukhala m'Asiya anamva

mau a Ambuye, Ayuda ndi Ahelene (Machitidwe 19:10).

Malo a maphunzirowa analibe malire pa chikhalidwe. Ophunzira amatumikira kwa ayuda ndi

amitundu omwe. Sukuluyi inalibenso malire pa dera. Ophunzira samatumikira mu mzinda wawo

wa Aefeso okha, koma anafika mu chigawo chonse cha m’Asiya. Malo amphunziro amene Paulo

nakhazikitsa anakwaniritsa cholingachi:

Ndipo anacita comweco zaka ziwiri; kotero kuti onseakukhala m'Asiya anamva

mau a Ambuye, Ayuda ndi Ahelene (Machitidwe 19:9-10).

Cotero mau a Ambuye anacuruka mwamphamvu nalakika (Machitidwe 19:20)

Sukulu yak u Aefeso inaphunzitsa okhulupirira kuti akhale atumiki amphamvu a uthenga

wabwino. Ophunzirawa anachulukana mu uzimu kufikira onse amene anali mu m’Asiya ndi Mau

a Mulungu. Pokhazikitsa malowa Paulo anachulukitsa utumiki wake.

NTCHITO YOPITILIRA

Werengani Machitidwe 19:23-41 ndi 20:1. Kupanga komanso kugulitsa kwa zinthu za matsenga,

mabuku, ndi zina anali malonda a akulu ku Aefeso. Pamene anthu analapa machimo awo ndi

kuyamba kutsata njira ya uthenga wabwino, sanagulenso katunduyi zimene zimagwira ntchito pa

chipembedzo cha mafano. Zonse zimene anagula kale anaziotcha.

Amalonda amene amapezamo phindu mu zogulisa zawo anakwiya. Moti mpungwepungwe

unayamba koma kumapeto, Paulo anachoka ku mzindako. Koma atngochoka Paulo, anasiya

chinachake chofunika kwambiri. Anasiya gulu limene linali ophunzira amene amafalitsa uthenga

wabwino. Anasiya malo ochitirapo maphunziro amene anapitilira kutsogoleraanthu obadwa

mwatsopano mkukhala ophunzira. Malo amene Paulo anakhazikitsa anapitilira kuchuluka

ngakhale mu nthawi imene sanali ku mzindako.

CHOSOWA CHALERO

Page 156: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

156

Chosowa chokhala ndi malo ochitira maphunziro chilipobe lero. Pamene anthu atembenuka

mtima mkuchuluka, ndi zofunikira kuti akuphunzitsaidwa. Ophunzirawa ayenera kupatsidwa

udindo wofikira anzawo ndi uthenga wabwino.

Pamene dziko likukumana ndi kusintha kwa maboma, atumiki ambiri amishoni amakakamizidwa

kuchoka dziko limene akutumikira. Ngati kuchulukana kupitilre mu nthawi imene iwo kulibe,

akuyenera kusiya malo ochitira maphunziro ngati mmene zinalili ku Aefeso.

Zotsalira za chaputalachi zikupereka malangizo okhazikitsa malowa. Akhoza kuyambika ndi ka

gulu kakang’ono ka mipingo kapena ndi munthu mmodzi amene ngati Paulo anagwira

masomphenya ochulukitsa mu njira imeneyi.

KODI TINGAKHAZIKITSE BWANJI MALO OCHITIRAPO MAPHUNZIRO

Pofuna kuyamba malo ochitirapo maphunziro:

1. FUNANI DONGOSOLO LA MULUNGU:

Ngakhale Paulo anaphunzitsa ophunzira kulikonse amatumikira, sanakhazikitsa malo a

maphuziro kulikonse amapita. Mwaphunzira njira zambiri za kuchulukana ku uzimu mu

phunziroli. Cholinga cha Mulungu cha kuchulukana kwa ophunzira ndiko kufalisa uthenga

wabwino basi. Njira zimene anagwiritsa ntchito pofuna kufikira cholingachi zinali zosiyana.

Gawo loyamba lokhazikitsa malo ochitita maphunziro ndi kufunafuna chifuniro cha Mulungu.

Harvestime International Institute amapereka phunziro mutu wake, “Kudziwa Kulankhula kwa

Mulungu” limene lingakuthandizeni kumvetsa mmene Mulungu amaululira chifuniro chake kwa

munthu. Podziwa kuti dongosolo la Mulungu limasiyana potengera malo, chikhalidwe, chosowa

komanso njira za dongosolo la malowo zimasiyana.

2. KUMVETSA CHOLINGA:

Mukuyenera kumvetsa bwino cholinga chokhala ndi malo ochitapo maphunziro molingana ndi

chitsanzo cha Aefeso. Cholinga cha sukuluyi sikuphunzitsa anthu kupeza mapepala a ntchito,

malonda, kampani kapena ulimi ayi. Makoleji ndi masukulu a maluso amapanga izi.

Sukulu yaku Aefeso inaphunzitsa ophunzira ndi kuwakonzekeretsa ku ntchito ya utumiki.

Cholinga chinali kufalisa uthenga wabwino ku dziko lonse ndi kwa anthu a mitundu yonse.

Okhulupirira atsopano anaphunzitsidwa kukhala ophunzira ndi kupitilira kuchulukana. Ena mwa

ophunzirawa anali ochita malonda kapena alimi. Koma sukuluyi sinawaphunzitse mu zimenezi

koma mu kukhala okhulupirira ochitachita kaya akugwira kumsika kapena ndinu otumikira

nthawi yonse.

Malo ochitira maphunziro sanatenge malo a mpingo. Okhulupirira amapitilira kusonkhana mu

sunagoge, amene anali malo amodzi osonkhanira a mpingo woyamba. Okhulupirira ayenera

kupitilira kusonkhana mmipingo ya kumadera ndi kunyumba kwawo. Sukulu ya Aefeso inali

Page 157: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

157

mbali yopitiliza ntchito ya mpingo. Sukuluyi sinatenge malo a utumiki wa mpingo, koma

kukulisa. Cholinga cha maphunzirowa si kuchotsa malo ena ophunzitsira bwino ayi pofalisa

uthenga.

Ndi cha nzeru kulemba cholinga cha sukuluyi. Izi zimatchedwa “Mawu a Cholinga.”

Zimakuthandizirani kukhala owona ku cholinga cha malo ochitira maphunzirowa. Harvestime

International Institute ali ndi phunziro lotchedwa “Dongosolo la Zolinga” limene lingathe

kukuthandizani kulemba mawu a cholinga.

3. KHALANI NDI DONGOSOLO LA NDALAMA

Ili ndi dongosolo loyerekeza mitengo ya katundu amene mudzafune. Znthu zimene mugwiritse

ntchito pa skuluyi, mmene mulengezere kwa anthu, ndi ndondomeko ya maphunziro anu. Izi

zimafuna ndalama imene mudzagwiritse ntchito. Ngati muli ndi ndalama yoyambisira sukulu,

mukuyenera kupanga dongosolo la ndalamazi. Pamenepa mukuyenera kulemba mitengo ya

zinthu imene mwakonza.

Ngati ndalama mulibe yoyambitsira sukulu, pempherani kuti Mulungu akupatseni ndalama.

Ngati gulu la mpingo ndi limene likufuna kuyambitsa malowa, mwina mpingo uliwonse utha

kupereka zimene angathe, komanso ophunzira atha kupereka imene angathe. Kusowa kwa

ndalama kusakupangiseni kusayambitsa sukuluyi. Gwiritsani ntchito maphunziro a Harvestime

International Institute ndipo yambani sukulu kunyumba kapena malo amene simupereka

ndalama. Aphunzitsi kapena othandizira akhoza kudzipereka kuphunzitsa ophunzira.

4. SANKHANI MALO

Mzinda wa ku Aefeso umene Paulo anasankha kuti ukhale malo ochitirapo maphunziro unali

wotanganidwa ndi malonda. Unali malo okopa alendo ndi likulu la zamatsenga ndi mafano a

Mulungu wa mkazi wotchedwa Diyana. Zinthu izi zinapangitsa kuti anthu ambiri azikakhala

kumeneko. Kufikira anthu a ku Aefeso ndi uthenga unali mwayi wawo wa maphunziro. Osati

chifukwa uthenga ukanalalikidwa kwa anthu ambiyi ayi, koma kunali mwayi wofikira anthu

zikwi amene amabwera kumeneko ngati alendo ndi amalonda amene amabwerera kwawo atamva

uthenga. Ngati ophunzira amatha kuphunzira mmene amachitira za matsenga ndi ziwanda ndiye

kuti akhoza kutumikira madera ena ndi mphamvu yaoipa ya Satana. Paulo sanawachotse

ophunzirawa mu nyengo zawo ndi cholinga choti alandire maphunziro. Anawaphunzitsa mu

nyengo imene inali yodziwika kwa iwo. Anakhalabe ku malo awo ndi mu chiyankhulo chawo.

Paulo anasankha malo oyenera a sukulu ya maphunziro. Mufunseni Mulungu akutsogolereni

pamene mukufuna malo ochitirapo maphunziro.

Pamene mukuganiza za malo, dzifunseni mafunsowa:

Koyamba: Kodi malowa anthu amafikapo kuti angalandire maphunziro?

Anthu akuyenera kutha kuzapedza maphunziro. Ngati mulu kumudzi sukuluyo ikhale malo oti

anthu atha kuyenda. Kaya ndi mu mzinda anthu ayende kappa pa galimoto. Kaya ndi malo a

zochitika, anthu ambiri athe kufikapo.

Page 158: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

158

Kachiwiri: Kodi malowo ali kwabwino?

Kwa Aefeso kunali malo abwino ochitira malonda. Ngati mkotheka malowo akhale kotero

amene anthu pachikhalidwe amatha kubwerako kudzapanga zinhtu zina. Makamaka kumene kuli

chiwerengero cha anthu ambiri. Musaope kaya malowo kuli malinga a Satana, pakuti izi

zidzathandiza ophunzira kuona zimene akuphunzira.

Kachitatu: Kodi ndi zipangizo zanji zimene mugwiritse ntchito?

Sizofunika kumanga malo a maphunziro a chilendo, Paulo anagwiritsa ntchito zipangizo zimene

zinalipo kale. Mungayambitse sukuluyi mmasukulu, mumpingo, ndi malo a zochitika. Ngati

mkotheka malo akhale opanda mbali. Malo amene si ampingo ayi pofuna kupereka mwayi kwa

anthu onse. Abusa ena amaopa kuti anthu awo apita ku mipingo ina. Mipingo ina simalola anthu

awo kupita ku mipingo ina. Maganizowa si abwino, ngakhale alipo.

5. SANKHANI DONGOSOLO LA MAPHUNZIRO OYENERA:

Dongosolo la maphunzira ndi maphunziro amene mwakonza kuti aziphunzitsidwa. Onentsetsani

kuti maphunzirowo akhale amene akwaniritsa cholinga chophunzitsa ndi kukonzekeretsa

atumuki. Mwachitsanzo phunziro la mmene mungamvere kulankhula kwa Mulungu ndi lofunika

pokwaniritsa cholinga cha sukulu kusiyana ndi phunziro la mbiri ya mpingo wanu.

Maphunzirowa aziika chidwi pa zimene Yesu anaphunzitsa kwa anthu wamba amene

anasanduka pohunzira oflaitsa uthenga wabwino. Ndipo akhale ochkera Mbaibulo. Maphunziro

amenewa akupezeka kudzera kwa Harvestime International Institute. Posasankha maphunzirowa

muonenso mpahunziro a anthu amene mukufuna kuwaphunzitsa. Kodi amatha kulemba ndi

kuwerenga? Nanga amalankhula chiyankhulo chanji, kulemba ndi kuwerenga? Kodi muzafuna

owamasulira ziyankhulo kapena ayi?

6. SANKHANI APHUNZITSI NDI OGWIRA NTCHITO ZINA

Mfuseni Mulungu akutsogoleleni posankha aphunzitsi. Onetsetsani kuti mukugwirizana ndi

cholinga cha sukuluyo ndi maphunziro amene mukuphunzitsa. Maphunziro a aphunzitsi ndi

ofunika kuwaonanso. Akhale okhoza kuphunzitsa ophunzira molingana ndi maphunziro awo.

Koma koposa zonse moyo wawo wa uzimu ndi mphatso zawo ndizofunikanso. Sankhani

okhulupirira amene ali ndi mphatso yophunzitsa.

Kupatula aphunzitsi sankhani ogwira ntchito ena amene azikonza malo ophunzirira. Amene

akuyenera kumalankhula zambiri za sukuluyo ndi ena.

7. LENGEZETSANI SUKULUYO

Anthu sangabwere kusukuluko ngati sanamvepo zoti ilipo. Mukuyenera kulengeza uthenga wa

sukuluyo ku mudzi, mzinda ndi kumene mufuna kutumikira. Mmene mungalengezere zitengera

ndala zimene muli nazo ndi malo. Ngati ndi mudzi wochepa ndiye kuti mokhoza

Page 159: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

159

kumangoyendera, momwemonso ku mpingo. Kaya mukhoza kulankhulana ndi abusa anzanu

zokhuza sukuluyo. Mu mzinda uthenga umavuta kufalisa chifukwa cha chiwerengero

chochuluka. Izi ndi zina mwa njira zimene mungasate kufalisa uthenga wa sukuluyo.

Kuyenda mmipingo. Pezani mipingo imene ili mdera lanu poimba mafoni kwa abusa kenako

awuzeni za masomphenya anu. Apempheni kuti awuze mpingo wonse za masomphenya anuwo

mu mwambo wa mapemphero.

Nkhani za mu mpingo: Ngati mpingo wanu umalengezetsa nkhani kwa mamembala anu,

konzekerani kukalengezetsako za sukuluyi.

Nkhani zoulutsidwa: Konzekeraninso kukasiya uthenga wa sukulu yaniyi ku nyumba imene

amalembako ndi kufalitsa nkhani.

Mauthenga ofalitsidwa: Mukhozanso kuika uthengawu mutaulemba bwino mmasukulu,

mmitengo komanso malo amene aanthu amapezekako ambiri. Pemphani chilolezo kwa

akuluakulu mmalowa.

Zochitika za akhristu: Ngati pali mwambo waukulu, umene waitana anthu ambiri a

mumpingowo, pemphani atsogoleri kuti alengezetse za sukulu yanuyo ku mwambo wa

zochitikazo.

Njira zina ndi monga kupereka makalata kwa anthu, kupezeka ku malo amene atsogoleri

amakhalako. Komanso tumizani mauthenga ku mipingo yosiyanasiyana kwa abusa. Kuonjezera

apo, gwiritsani ncthito mabungwe a chikhristu amene ali mdera lanu. Pamphani atsogoleri kuti

akupatseni mwayi wolengezetsa uthanga kwa anthu awo mu mikumano yawo.

8. CHITANI MKUMANO WOYAMBA:

Kukumana koyamba mkalasi ndi kofunika kwambiri. Kukuyenera kukhala kwa abusa ndi

okhulupirira onse opezeka mderalo. Zimene mungachite ndi monga:

a. Kuwalandira aphunzitsi ndi ogwira ntchito ena.

b. Kufotokoza cholinga cha sukulu ya maphunziro.

c. Kufotokozapo za dongosolo la maphunziro ake.

d. Kupemphera, kulambira ndi kuyimba.

e. Kuyesera kuphunzitsa ngati chitsanzo

f. Pemphero lotsekera zonse.

g. Kulembetsa kwa iwo amene awonetsa chidwi choyamba. Izi zichitike kumapeto koma

musanaseke. Ophunzira akumane ndi aphunzitsi awo ndi kutenga dongosolo la

maphunziro awo. Izi ziwalimbikitsa kulembetsa ndi kumaliza maphunziro awo.

9. MAPHUNZIRO OPITILIRA

Izi ndi zina zimene mungamachite pamene sukulu yayambika: kukonzekera, kusunga nthawi,

kupemphera, kubwereza zomwe mwaphunzitsa, kugwiritsa ntchito njira zophunzitsira

Page 160: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

160

zosiyanasiyana, lolerani kuyenda kwa Mzimu Woyera ndipo tsogolerani ophunzira kuti ayambe

kugwiritsa ntchito zimene aphunzira. Komanso apatseni ophunzira ntchito yokachita kwawo pa

zimene aphunzira

Kumbukirani: cholinga cha sukuluyi ndi kukonzekeretsa ophunzira kupita kulikonse ndi uthenga

wabwino.

Page 161: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

161

MAYESO ODZIYETSA NOKHA

1. Lembani Vesi Yotsogolera kuchokea pamtima

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

__________________________________________________________________________

2. Kodi ndi njira ziti zimene Paulo anagwiritsa ntchito kukphunzitsa okhulupirira a ku

Aefeso?

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

3. Fotokozani za malo ochitirapo maphunziro a ku Aefeso.

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

__________________________________________________________________________

4. Kodi cholinga cha kukhala ndi malo ochitira maphunziro ndi chiyani?

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

5. Perekani chidule cha malangizo amene aperekedwa pofuna kutsekula sukulu ya

maphunziro.

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

___________________________________________________________________________

(Mayankho a mafunsowa akupezeka kumapeto kwenikweni kwa bukuli)

Page 162: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

162

KUPITILIZA KUPHUNZIRA

1. Eliya anali ndi sukulu ya aneneri mu Chipangano Chatsopano ndipo anali otsogolera

(onani II Mafumu 2:4). Poganizira utumiki wa aneneri, kodi ndi maphunziro anji amene

akuyenera kukhala nawo?

2. Harvestime International Institute imapereka maphunziro amene akhoza kugwiritsidwa

ntchito ku sukulu yamaphunziro potenga maphunziro akewa. Sukuluyi ili ndi pulogalamu

yoyendayenda ya akhristu komanso iwo amene ali ndi njala yotumikira Mulungu.

Maphunzirowa amakamba za zimene Yesu anaphunzitsa ndi kusintha anthu wamba

kukhala okhulupirika potengera uthenga kudziko lapansi ndi kuonetsera mphamvu yake.

Maphunziro ake agawidwa mmagawo monga chiyambi cha maphunziro ndi mabuku

asanu ndi limodzi a maphunziro.

Page 163: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

163

MAYANKHO A MAFUNSO ODZIYETSA NOKHA

CHAPUTALA CHA 1:

1. Ndipo Yesu ananena nao, Idzani pambuyo panga, ndipo ndidzakusandutsani inu asodzi a

anthu (Marko 1:17).

2. Lamulo loyamba ndi lomaliza la Yesu kwa ophunzira ake linali lowapanga kuti

achulukane. Onani Marko 1:17 ndi Machitidwe 1:8.

3. Kuchulukana ndi kukhala ambiri mu chiwerengero poberekana. Kuchulukana ndi njira

yochulukitsa. Pamene chinthu chikuchulukana chimachuluka nthawi ndi nthawi.

4. Kuchulukana ku uzimu kumachitikanso ku uzimu. Wokhulupirira amagawana uthenga

wabwibo ndi anthu ena, ndi kuwatsogolera kukhala okhazikika mwa Yesu.

5. Njira ndi ndongosolo lokwaniritsa cholinga chathu.

6. Ndondomeko ndi dongosolo la njira zimene zaikidwa pamodzi pofuna kufikira cholinga.

7. Ndondomeko za njira zochulukana mu uzimu ndi dongosolo la njira limene limapangitsa

okhulupirira kufikira cholinga chawo chochulukana ku uzimu.

8. Fananitsani chidule chanu ndi zimene mwaphunzira mu chaputala choyamba.

CHAPUTALA CHA 2:

1. Pakuti wapeputsa tsiku la tinthu tating'ono ndani? (Zakariya 4:10).

2. Fanizirani chidule chanu ndi zomwe mwaphunzira mu chaputala cha 2.

3. Kukula mmadera, mu chikhalidwe, mu chiwerengero ndi mu uzimu.

4. Ena mwa mavesi awa akhoza kugwiritsidwa ntchito: Numeri 1:1-3; 2:23-24; 26:1-4;

Mateyu 9:13; Luka 15:7; 19:10 Machitidwe 1:15; 2:41; 4:4; 6:7; 9:32; 12:24; 16:5; 19:20;

28:30-31; Yohane 3:16; II Petro 3:9

5. Fanizirani chidule chanu ndi zimene mwaphunzira mu chaputala cha 2.

6. a. Zonama b. Zonama

CHAPUTALA CHA 3:

Page 164: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

164

1. Ndipo ndi mafanizo otere ambiri analankhula nao mau, monga anakhoza kumva (Marko

4:33)

2. Fanizo ndi nkhani imene imachokera mu zochitika za anthu koma imakhala ndi tanthauzo

la kumwamba kapena la uzimu.

3. Kumvetsetsa choonadi cha uzimu chimene chimaphunzitsidwa mmapemphero

kunapatsidwa kwa ophunzira chifukwa anapatsidwa maganizo a uzimu. Iwo amene

analibe uzimu amalephera kumvetsa.

4. Onani zimene zili mu mafanizo mu chaputala cha 3.

CHAPUTALA CHA 4:

1. Ndipo zimene wazimva kwa ine mwa mboni zambiri, zomwezi uikize kwa anthu

okhulupirika, amene adzadziwa kuphunzitsa enanso (II Timoteo 2:2)

2. Kuchitira umboni ndi kuwauza anthu zimene wazimva, ndi kukumana nazo. Mu nyumba

ya malamulo, mboni ndiye amene amanena za munthu kapena chinthu. Monga mboni,

timanena za Yesu ndi dongosolo la chipulumutso kwa anthu onse.

3. Atumiki amene sanasankhidwe ndi amene amapezeka mu mpingo wa Mulungu. Kapena

kuti ndi anthu onse a Mulungu. Ena amatchedwa otumikira koma osati nthawi zonse mu

mpingo.

4. Mawu oti “akulu a mpingo” ndi atumiki amene anasankhidwa kutumikira mumpingo.

Iwo amene utumiki umakhala gawo la moyo wawo amene amakhala olembedwa ndi

mpingo.

5. Maitanidwe a anthu amene satumikira nthawi yonse ndi a kwa okhulupirira onse amene

ndi “ansembe” kapena atumiki a uthenga wabwino.

6. Dongosolo la Mulungu likupezeka pa Machitidwe 1:8. Mzimu Woyera ndiye mphamvu

ypoangitsa kuchulukana, Yesu ndiye uthenga wopita kudziko lonse. Okhulupirira ndiwo

zotengera za uthengawu.

7. Andreya ndi Hananiya.

8. Yambani kugawana uthenga wabwino ndi achibale, anzanu ndi ogwira ntchito limodzi.

Uthenga umafala mwachangu kwa magulu amenewa.

CHAPUTALA CHA 5:

Page 165: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

165

1. Ndiponso Ine ndinena kwa iwe, kuti iwe ndiwe Petro, ndipo pa thanthwe ili

ndidzakhazika Mpingo wanga; ndipo makomo a dziko la akufa sadzaulaka uwo (Mateyu

16:18-19).

2. Okhulupirira onse mwa Yesu abadwanso kachiwiri mu ufumu wa Mulungu.

3. Mpingo unabadwa mwa Mzimu Woyera pa tsiku la Pentekosite. Onani Machitidwe 4.

4. Fanizirani mayankho anu ndi zitsanzo za mu chaputala cha 5.

5. Kulambira, kutumikira, chiyanjano ndi utumwi.

6. Onani zokambirana za mu chaputala cha 5.

7. Onani zokhambira za mu chaputala cha 5.

CHAPUTALA CHA 6:

1. Pakuti kunamkomera Atate kuti mwa iye cidzalo conse cikhalire (Akolose 1:19).

2. Kukula mkati ndi kukula mu uzimu ndi kuumbika kwa mamembala a mpingo. Uku ndi

kukula kwa makhalidwe abwino osati kukula mu chiwerengero.

3. Kukula mu uzimu ndi kuchuluka kwa uzimu kumene kumabwera chifukwa chakukula

kwa moyo wa uzimu mmoyo wa okhulupirira.

4. Onani zokambirana za mu chaputala cha 6.

5. Onani zokambirana za mu chaputala cha 6.

6. Onani zokhambirana za mu chaputala cha 6.

CHAPUTALA CHA 7:

1. Ndipo mau a Mulungu anakula; ndipo ciwerengero ca akuphunzira cidacurukatu ku

Yerusalemu (Machitidwe 6:7).

2. Kukula mu chiwerengero ndi pamene okhulupirira apezera okhulupirira nzake kwa Yesu

ndi kuwabweretsa chiyanjano pa mpingo wawo. Zotsatira zake zimakhala kukula mu

chiwerengero cha mpingo.

3. Fanizirani ndi chidule chanu pa zokambirana za mu chaputala cha 7.

Page 166: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

166

4. Fanizirani ndi mayankho anu pa zokambirana za mu chaputala cha 7.

CHAPUTALA CHA 8:

1. Kotero Mipingoyo inalimbikitsidwa m'cikhulupiriro, nacuruka m'ciwerengo cao tsiku ndi

tsiku (Machitidwe 16:5).

2. Kukula mmadera kumachitika pamene mpingo uyambitsa mpingo wina mu zikhalidwe

zofanana. Mpingo watsopanowo ndi nthambi ina ya “likulu” la mpingo monga mmene

zimzkhalira mdziko kholo ndi mwana.

3. Kudzala mpingo ndi kukula ndi kulumikiza kwa mpingo. Mmodzi amadzala mpingo

watsopano monga mlimi wodzala mbeu. Mbue zimabereka mtengo watsopano wofanana

ndi kholo la mbeu ija.

4. Anthu a ku mpingo wa ku Yerusalemu anabalalikana chifukwa cha chizunzo. Anapita

mmalo osiyanasiyana kulalikira uthenga ndipo anthu amatembenuka mtima.

5. Izi ndi njira zokulitsira mpingo:

-mpingo kudzala mpingo wina

-mipingo kugwirizana kudzala mpingo

-mpingo waukulu kugawana mkupanga mipingo iwiri kapena yoposera apo.

-munthu wokhulupirira kupita kumalo ena kukayambitsa mpingo.

6. Pali mitundu ingapo ya kukula mmadera kwa mipingo:

-mipingo kukatumikira ku madera ena

-mipingo kukatumikira kumadera a mitundu ina

-mipingo ya cholinga chapadera.

7. Zofunikira za Mbaibulo ndi kudzala mipingo mmalo osafikilidwa, malo osalandilika,

mmizinda keneko mmidzi.

8. Uthenga umene umabadwitsa mipingo ndi wochokera Mbaibulo, wokamba za Khristu,

wofikira chosowa.

CHAPUTALA CHA 9:

1. …Kukawatsegulira maso ao, kuti atembenuke kucokera kumdima, kulinga kukuunika,

ndi kucokera ulamuliro wa Satana kulinga kwa Mulungu, kuti alandire iwo cikhululukiro

ca macimo, ndi colowa mwa iwo akuyeretsedwa ndi cikhulupiriro ca mwa Ine

(Machitdwe 26:18).

2. Kukula kolumikiza ndi pamene mpingo ukula polalikira ku madera ena, a zilankhulo

zina, mitundu ya anthu ena amene ndi osiyana zikhalidwe.

Page 167: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

167

3. Machitidwe 1:8. Uthenga wabwino umayenera kupita kutali kuchokera ku Yerusalemu

kufika ku “malekedzero a dziko” lapansi.

4. Mtumwi Paulo.

5. Fanizirani chidule chanu ndi zomwe zili mu chaputala cha 9.

CHAPUTALA CHA 10:

1. Pomwepo Yesu anati kwa ophunzira ace, Ngati munthu afuna kudza pambuyo panga,

adzikane yekha, natenge mtanda wace, nanditsate Ine (Mateyu 16:24).

2. Mawu oti “kutembenuka” amakamba za wokhulupirira watsopano mwa Yesu amene

wabadwa mwatsopano mwa chikhulupiriro mkukhala gawo la ufumu wa Mulungu.

3. Mawu oti “wophunzira” ndi munthu amene watembenuka mtima mkukhazikika pa

maziko a chikhristu ndipo amakhala wokonzeka kupanga ophunzira ena. Wophunzira ali

ngati mwana wa sukulu amene amaphuzira potsatira. Ndi kuposa kukhala ndi mzeru. Ndi

kuphunzira kumene kumasintha makhalidwe a moyo wamunthuyo.

4. Zinthu zofunika pa kukhala wophunzira ndi kuwerengera mtengo wake, kuchita zofunika,

ndi kukhala ndi cholinga chenicheni.

5. Mfundo 9 zofunika pa kukhala wophunzira ndi:

Kusankha malangizo chiyanjano

Chionetsero kudzipatula kutenga nawo mbali

Kuyang’anira kupatsa ena zochita masomphenya

6. Wophuzira ndiye amene:

Amazikaniza yekha amasiya zonse amakhala Mmau

Amatsatira Yesu amakhala womvera amakhala wotumikira

Ufumu umakhala choyamba amabala chipatso amaonetsera chikondi

7. Yesero lenileni la wophunzira ndi zimene zimachitika pamene simukupezeka ndi

ophunzira anu. Kodi amakhalabe okhulupirika ndi kuphunzitsa ena amene ali ndi

kuthekera kopitilira kuchulukana?

CHAPUTALA CHA 11:

1. Wodala munthuyo wosayenda mu uphungu wa oipa, Kapena wosaimirira m'njira ya

ocimwa, Kapena wosakhala pansi pa bwalo la onyoza. Komatu m'cilamulo ca Yehova

muli cikondwerero cace; Ndipo m'cilamulo cace amalingima usana ndi usiku. Ndiye

akunga mtengo wooka pa mitsinje ya madzi; Wakupatsa cipatso cace pa nyengo yace,

Tsamba lace lomwe losafota; Ndipo zonse azicita apindula nazo (Masalmo 1:1-3).

Page 168: NDONDOMEKO ZA NJIRA ZA KUCHULUKITSAharvestime.org/translations/chichewa/principles of... · 2019-06-03 · Kodi ndi chifukwa chiyani Yesu adagwiritsa chitsanzo cha usodzi poitana

168

2. Pamene kukula kuli kopinimbira kudziko, thupi silimakula moyenera. Pamene kuluka

kwa uzimu kuli kopinimbira, anthu sakula mu uzimu ndipo mpingo sukulanso.

3. Chitsanzo A: Mlongo wolakwiridwa ayenera atsatire malangizo amene ali pa Mateyu

18:15-17

Chitsanzo B: Mpingo ukuyenera kugwiritsa ntchito njira ya “bwerani” osati ya “pitani.”

Pakhoza kukhala ntchito zina zosayenera zimene ziyenera kusadzidwa.

Chitsanzo C: Mpingowo mkutheka sumaphunzitsa anthu atsopano mwa Yesu kuti akhale

ophunzira.

CHAPUTALA CHA 12:

1. Koma pamene ena anaumitsa mtima ndi kusamvera, nanenera zoipa Njirayo pamaso pa

anthu, anawacokera, napatutsa akuphunzira, nafotokozera masiku onse m'sukulu ya

Turano (Machitidwe 19:9-10).

2. Paulo anaphunzitsa zimene anakumana nazo (Machitidwe 19:2-8), poonetsa chitsanzo

(Machitidwe 19:11-12), ndi pochititsa maphunziro (Machitidwe 19:9).

3. Malo ochitira maphunziro a ku Aefeso amapereka maphunziro a zaka ziwiri amene

amaphunzitsa atumiki mu zikhalidwe ndi mmadera pofafalita uthenga wabwino

(Machitidwe 19:10-20).

4. Cholinga cha kukhala ndi malo ochitira maphunziro ndi kuphunzitsa ophunzira ndi

kuwakonzekeretsa ku ntchito ya utumiki.

5. Fanizirani chidule chanu ndi zomwe zili mu chaputala cha 12.